Abambo atatu apha mzawo ndi zikwanje

Advertisement
knife-blood

Apolisi m’boma la Machinga akwidzinga ndi kutsekera abambo atatu chifukwa chowaganizila kuti adachotsa moyo wa bambo wina wa zaka 60 pomukhapa ndi zikwanje.

M’malingana ndi oyankhulira apolisi m’bomali Davie Sulumba, a polisi amangadi John Daudi a zaka 30, Henry Dawa, 19, komanso a Sinoya Petro a zaka 32 powaganizira kuti ndiwo adachita za upandu okuphawu.

knife-bloodA Sulumba anati ophedwayu, Jaison Thom, yemwe amagulitsa makala adakumana ndi tsokali mu m’bandakucha wa pa 23 Okotobala pamene adachoka kunyumba kwake ndi thumba limodzi ulendo wa ku Liwonde kuti akalitakate kwa kasitomala wake wa nthawi zonse.

Koma podutsa m’mudzi mwa a Chilonga, mwadzidzidzi kudavumbuluka abambo atatu omwe amagona panja pa nyumba ndipo anayamba kumenya ndi kutema ndi zikwanje a Jaison Thom modetsa nkhawa ndi mopanda chisoni powaganizila kuti adali okuba.

A Thom adatengeredwera ku chipatala cha boma cha Machinga komwe madotolo adatsimikiza kuti iwo adamwalira kamba kotaya magazi ambiri chifukwa cha mabala akulu omwe adali mthupi mwawo.

Potsatila kafukufuku, a polisi mderali akwanitsa kumanga atatuwa pa 24 mwezi omwewu ndipo abambowa akuyembekezera kukaonekera ku bwalo la milandu kukayankha mlandu wa kupha omwe umasemphama ndi gawo 209 la malamulo oweluzira milandu

Potsatila izi a Sulumba apitiliza kudzudzula anthu m’bomali kuti apewe kutengera malamulo m’manja mwawo popeza kumakhala kuzikalasulira makala a moto, koma kutengera oganizilidwawo kwa a chitetezo cha m’mudzi kapenanso ku police kumene.

A Jaison Thom adali ochokera m’mudzi mwa a Chipamba mfumu yaikuli Sitola m’boma la Machinga, pamene a Daudi, a Dawa ndi a Petro onse ndi mmudzi mwa Issa mfumu yaikulu Sitola m’boma lomweli.

 

 

Advertisement

53 Comments

  1. Kodi 3 akutivuta bwanji? Azimayi atatu aku 25 aja kenako azimayi atatunso aku 24 then ndi amuna atatu aku machinga zoona Koma 3 utisowetse mtendere, Iwe 3 tisamale.

  2. Malawi ankaziwika bwino pa nkhani yopemphela muno mu Africa kma wazaza ndizoypa …apa ndsaname Malawi wapanga apazi ndza agalatiya …nde chiweluzo chinawe pafupi koz unali ndicholinga posalisaina lamulo la okupha nzake aphedwe …unkafna anthu aziphana chonchi ngt nkhuku ..chenjela Malawi ndimasiku ano otsiliza…

    1. I think the number of sinners is decreasing and the number of devils is increasing in the Warm Heart of Africa. The Devil cannot be forgiven because doesn’t know that language. A sinner can convert and forgiven but not the devil.

  3. Mwawona bwanji malamulo kuwadereratu kumeneko nanga mmalo moti angokhapa ndi munthu mmodzi koma onse! atatu,ndimanena ine anthuwa sasamala za moyo wanzawo inu simuva! akatero muwaona one week abwera kundende kuja pobweraposo ngati timabwana ataphuzira ntchito za manja alipheeee koma wa nzawo moyo atachotsa Eeee! koma ku Malawi!

  4. Mateyu 24:12 “Tsono popeza kuti zoipa zizidzachulukirachulukira, chikondi chizidzacheperachepera pakati pa anthu”. Abale Yendani ndi Mulungu kuopa kugwera mmayesero.

  5. Koma anzathu kumwera uko umbuli wanuwo ukugwira ntchito.blood sucker, ndinuyo kupha anthu osalakwa.each and every evil doing it’s you infront southerners why ?ignorance and illiterate at it’s best.kenaka tukumu tukumu anthu ozindikira ife!

Comments are closed.