Neba walira kuti nto! Nyerere lero zakokela jombo kuuna

Advertisement
Wanderers FC

Mphenzi simenya pamalo kawiri. Kufa kwa pachiweru sikunakhudzane ndi kwa lamulungu.

Nyerere lero zakhoma chikhomo pa malo ake a pamwamba pa Supa ligi muno mu Malawi.

Wanderers FC
Nyerere kumwa wa mkaka

Pa masewelo amene nyerere zinakumana ndi Apolisi a Blue Eagles, adani awo anafinya makolona kuti noma ione mbwadza ati kuti ligi ikhale yotsekula.

Anali mnyamata Essau Kanyenda amene anaonetsetsa kuti mapemphero a adani a Noma asagwile ntchito.

Kanyenda mu ukadaulo wake anakwapulilamo chigoli mu golo la Apolisi kuti asiye aganyu onse manja kukamwa.

Aganyu ena anali ndi chiyembekezo kuti Apolisi ndi kuuka pa Nankhaka kuti mwina achiteko za Siliva dzulo koma Kanyenda anabwelanso ndi kukhazikitsa mitima pansi kwa onse a nyerere.

beforward.jp Wanderers FC
Nyerere

Pokutha masewelo pa Nankhaka, manoma anali akuyimba olire olire ma pointi awo atatu mthumba ndi zigoli ziwiri, aganyu anali akutsonya uku misonzi ikutsika.

Padakali pano, noma ili ndi mapointi 47 itasewela masewelo 20 ndipo pachiwili pali a Siliva ndi mapointi 42 nawo atasewela masewelo 20.

Advertisement