Makoswe athamangitsa Pulezidenti mu ofesi

Advertisement
Buhari

Anthu ena akudabwa kuti anali aakulu ngati n’gombe mwina kapena ochepa koma msinkhu wa mphaka kapena mwana wa khanda.

Mtsogoleri wa dziko la Nigeria a Muhammadu Buhari alengeza kuti sazipita ku ofesi yawo ati chifukwa kuli makoswe amene aononga ofesiyo.

Buhari
Muhammadu Buhari: Asiya kupita ku ofesi kamba ka makoswe.

A Buhari amene afika ku Nigeria kumapeto a sabata yatha kuchokela ku dziko la Mangalande kumene anali kuchipatala kwa miyezi yoposa itatu anauza mtundu wa anthu ku Nigeria kuti iwo akhala akugwilila ntchito kunyumba kwawo. A Buhari ananena izi kudzela kwa othandizila.

‘Chachitika ndi chakuti pa nthawi imene ofesi yawo sinali kugwila ntchito, makoswe anasandutsa mphala yawo ndiye aonongamo,’ anatelo owathandizila a Bushiri kuuza mtundu wa anthu a ku Nigeria.

Koma ngakhale alengeza zotele, sikuti anthu akhulupilila kuti a Buhari akuthawa makoswe. Anthu ena mu dzikomo akuganiza kuti a Buhari sanachile zenizeni ndipo akufuna azigonabe.

A Buhari akhala akudwala kuyambila chaka chatha ndipo chaka chino nthawi yawo yochuluka yathela ku chipatala ku Mangalande.

 

 

 

 

 

 

 

 

 

 

 

 

Advertisement

2 Comments

Comments are closed.