Malamulo a pamseu aja ayamba kuluma: wa minibus amulipilitsa K180,000 chifukwa chonyamula ma 4 – 4

Advertisement
MINIBUSES

Ukali wa malamulo a pamseu amene aopseza oyendetsa minibus wayamba kuoneka.

MINIBUSES
Malamulo a pamseu ayamba kuluma

Bwalo la Milandu mu boma la Mulanje lalamula dalayiva wina wa minibus kuti alipile chindapusa cha K180,000 kapena akagwile ukaidi wa kalavula gaga kwa miyezi isanu ndi inayi.

Malinga ndi malipoti, bwaloli lapeza Bambo Ellias James olakwa pa mlandu oika moyo wa anthu pa chiopsezo atawapakila ngati nsomba mu minibus.

Apolisi ati Bambo James anaimitsidwa pa Mkando mu boma la Mulanje ndi mlandu oti anapakila anthu ambiri zomwe zinali kuika moyo wa anthuwo pa chiopsezo.

Iwo ati anawauza Bambo James kuti ulendo wathela pomwepo ndipo iwo anjatidwa. Koma atamva izi Bambo James anayamba kuchita mavuvu.

Apolisi ati pakuchita mavuvu paja, a James anang’amba yunifomu ya wa Polisi ndi kuwathotholela ena awiri zizindikiro pa zisoti zawo. Komabe Apolisi anawagonjetsa ndi kuwathila unyolo.

Atapita nawo pa bwalo, a Khoti anawapeza olakwa pa mlandu oika miyoyo ya anthu pa chiopsezo ndi okana kumangidwa.

Pa mlandu oika anthu pa chiopsezo kamba kopakila ma folo folo, Bambo James analamulidwa kupeleka K150, 000 ndipo pa mlandu okana kumangidwa, analamulidwa kupeleka K30, 000.

A bwalo anaonjezelapo kuti akalephela kupeleka, akatsekeledwe kwa miyezi isanu ndi inayi.

Advertisement

281 Comments

  1. Vuto ndilakuti zimene akuchitana zukathera pamunthu amene ndi osauka akakwera amukwezere mtengo zimene zikutanthauza kuti akuchita dala zonsezi ndicholinga choti pokana zimenezi madriver azingowapatsa zammanja kuti aonjezere pazomwe alinazo kale.

  2. Well-done our law enforcers. Musabwelere mbuyo ndi malamulo amenewa alipilitseni kapena kuwakwizinga akanganya amenewa anationjeza kutiphwanyira ufulu okwerafe. Psya! koka! luma!!!!

  3. Its unfortunate that zotsatira za Virgil ija ma min bus anakwezedwa mitengo chimene anthu tinagwirizana ndi ganizo loti tizikhala atatu atatu pa mpando koma lero zokhala 4 pampando zabweleranso n tikulipilabe mtengo okwerawo. It’s unfair kuti ma fruits a virgil ija ovulala ndi ma passengers and yet some one claims kuti Passengers Association mdziko muno

  4. Malamlo awa apanga ndi anyani okonda zimphu andi alibe maminibasi, 1 salunu imapanga ngozi mli farmily,lole imapanga ngozi itanyamla matabwa, fodya, chimanga or ilibe katundu imagwa waminibasi walakwa chani kuno kujoni ngozi pamwezi anthu amafa kopitilila 400 koma misewu ikulu ikulu fork akhwangwala

  5. Kod a malawi munakhala bwanji u always react whn thing r getting worse kod mesa zot pampando tizikhala 3-3 zinanenedwa kalekale ? Now u hav seen it very important coz more lives hav been perished just like that? Shame to u mai malawi and ur foolish rules! Mxiiiiii

  6. Achita bwino okwerafe ufulu amatilanda wokhala 3-3 ukati ukane amati sikani pamenepa aziopa lamulo sopano munthu aziopa lamulo ndemunthu amene

  7. akukweza mtengo in the name of three three and akufuna kupakila 4.eish.thats public stealing and another case levelled against him and stealing z has nothing to do with fine but jail term

  8. Boma likungofuna kuononga business ya minibus linazolowera kupondeleza a Malawi 4 4 4 palibe cholakwika coz 3 3 3 mpana wina umatsala

  9. Times and things have changed don’t politicise these issues,that’s the betterment of passenger welfare!we are in the 21st century!we want that to be adhered and nomore standing passengers in big buses!

  10. INE NDIMADABWA DIRIVER ALIBE VUTO KOMA ANTHU OKWERAWO. KODI AKATI FODYA AMAONGA MOYO , IWE KUGULA FODYA. DIRIVER ALIBE PROBLEM M’MASULENI MWACHANGU.

  11. If u say kuti 4-4 imapangisa ngozi nde nanga mchifukwa chani galimoto imachita ngozi even driver alimo yekha? just find other solution not this or else u should focus on speed osati zamkutu zanuzo

    1. ngati achita ngozi atapakira 4-4 afamo ambiri ngati achita ngozi atapakira 3-3 afamo ochepa chiwerengero chitsika osati amati singapange ngozi ‘funso lina bwana

  12. ngat malemu bingu ankakwera chibasi chija okhaokha,nde ifeyo tizikwera anthu mpaka 20 mukabongo??? zausiru amene sakufuna 4 4 akagule yake….

  13. Zili bwino koma pena athufe tili ndi ufulu cz tiona kut minbus yazaza atatu atatu ndiye timapira pompo ndachedwa sindingakhalepo apo ndiye pameneponso tisamale

  14. Good development keep t up police we need an accident free country. Some accidents r caused by neglegency of drivers so deal with them. Palibe samadxiwa how reckless minbus drivers r.

  15. Palibe chinthu chimandiwawa ngati driver ndi conductor kupulumuka pangozi yapamseu,mbuzi zimenezi zinakati zizifa nao ndikukhulupilira kuti ngozi zapamseuzi ili mbiri yakale.Bravo police.

    1. Zitsiru inu,mumasogoza ndalama m’malo mwa miyoyo ya anthu,pamene tulankhula pano ena ndiamasiye ndipo ena analumala chifukwa chakusasamala kwanu.

    2. Makape inu,mumatsogoza ndalama m’malo mwa miyoyo ya anthu,pamene tulankhula pano ena ndiamasiye ndipo ena analumala chifukwa chakusasamala kwanu anthu mwapha aja akwana pano lamulo lithana nanu ndibwelezenso kuti pangozi zomwe mumapangitsazo inuyo munakati muzifa nazo,sibwenzi tudandaula.

  16. to all tax drivers ,tomorrow start loading 5-5 as u are aware of the fine,before it goes up to K350,000(yr jail term),becoz u aren’t satisfied with the capacity of ur motor vehicles.welldone to those who are respossible for the fiines.

  17. kodi inu ama Min-bus mukufuna chan?….munakweza mitengo kut tizakhala 3-3 koma mukumatiyikabe 4-4 … Koma mukhaula Coz boma silikusiyani

  18. Usaumire, kuwafumbatisa iwe, ukaumira, uzaziona waona tcheleman. Anaumira sakanamugwira achina JP akupakira 4_4 onse achina langabwai akupanga zomwezo Sunday < Sunday 1<30 jenorobia < December koma samagwidwa chifukwa saumira ko drink onse achina Thom mufunse Vic.

  19. Adziweso Amenewa! Mitengo Anakweza Kale And Kutsitsila Amakana But Kungodusa Roadblock Akumayamba Kutisanjikiza Madengu, Abakha Yet Akuti Lamulo Linati Tizikhala 3,3. Anya Aona.

  20. Vuto ndinu okwela mtengo wa kwa mkando ndi 1000 munthu mmodzi mumalephela kulipila mumafuna 500 ndinu anthu oyipa inu

  21. thus totally stupid, are they saying all the accidents that have been happening it’s cause of 4 4? This government is full of shot.

  22. Malawi dzuka, minbus mpando wakumbuyo sakhala anthu, amakhala 3. Apapa akukamba zamipando inayo. Maiiko anzathu ixi sidxichitika. dxuka Malawi, 53 yrs u a old.

  23. big up @ #Rod_traffic moyo ndi mphamba ofunika kumawukonda………ndinapita ku Mozambique last week koma kutipakira kwakweko mu minibus mmmmmmm anthu 5-5 pampando ine kudabwa buss sikunyamuka,, kudzafusa Y akut sinadzadze ena amayimirira ine shaaaaa better @ my home MW kuli malamulo amzeru

  24. Inensotu zimandinyansa zimenezi umapezeka kuti wakwera bwinobwino muli pakati pa ulendo akangouzidwa kutj kutsogolo komwe akupitako kuli a traffic amakutsitsani mkukupatsanso ndalama yosakwana akuenera adzipeleka K500000 akagwidwa nonsense

  25. Amaminibas Avomeleze Chifukwa Minibas Anayaba Kale Kunena . Zimatheka Kupakila 4 4 Ena Kuyima . Makamaka Mseu Wa Mulanje Zapabana Mgati Akuwona Kuti Minibas Akatenga 3 3 Sikuwonesa Akasiye Minibas Kwabwana .

  26. It pains indeed and they must be punished more than that. Passengers are being loaded like lifeless things despite having paid alike. Life is not buyable and must be treated accordingly especially when we come to using road tranportsr

  27. It pains indeed and they must be punished more than that. Passengers are being loaded like lifeless things despite having paid alike. Life is not buyable and must be treated accordingly especially when we come to using road tranportsr

  28. I accept ena mwa malamulowo koma enawo i don’t. Zoti ma bus asamayende usiku ndiye fodyayo. Zoti mpando wa mmbuyo wa anthu 4 uja azikwela 3 ndikudananazo ngakhale ndilibe minibus. Malamulo awa atipweteka okwelafe chifukwa anthuwa akweza mitengo kuti azichita cover pakupelewelapo. Koma zoti no standing passenger komanso zoti 3 seat for 3 i salute that.

  29. amangwe basiii kusakhutitsidwa ndi capacity e same atakhala waudindo angakhale wadyera ameneyo osamakhutitsidwa ndikumapondereza amnzake ngat awowo awo……

  30. Its Simple, Anthu Amenewa Amafunika Adzilipilipira Ndalama Yocholuka Kuposa 180,000.Amangotipakira Ngati Mitembo Kumotchale,akapezekaso Oteloyo Lamulo Limugwire TChito.

  31. Ineyo ndinakhulupirira kuti zomwe adapanga ma driver a ma minibus ziwatsata.Panopa ziziti ka mulandu kakang’ono pa court pomwe mmbuyo muja amangoti ife ndi amalawi tasiyeni.Koma kukawotcha ma police units amayoooooooooo.

  32. akulipisa mtengo odula ati chifukwa ndi 3 3 3 ,,kuyenda pang’ono uwona mukukhala 4 4 4 what’s that????alangidwe kumene,,bongo mpaka 4 4 4???

    1. lives are not lost by packing 4-4 kuipa kwa misewu yathu nkumene kukuchititsa ngozi, boma lilibe ndalama angofuna kukama zoonda kale, amalawi osaukafe tikhale migodi yaboma?

    2. Ayi pepani ndithu ma minibus amathamanga zosowa zija ngati kuti sananyamule miyoyo ya wanthu ndalama zilibe kanthu apa ofunika awonjeze punishment kuti oyendetsa ndi eni a ma minibus asinthe kayendetsedwe

    3. Komatu somewhere tiziganizira miyoyo and safety. The seats in a minibus are designed to accommodate three persons period!!!

  33. this is totally nonsense akanamugamula life imprisonment agalu amenewa akujaila kwabasi 4 4 kt chani ma driver nonse a minbus lisani lalikululo mwamva pa ujeni panu axikumangani kumene

  34. Ku lilongwe kuno akunyamulabe 4 pa one seat so pathetic . Kodi a police bwanji sapanga patrol mainly pick hours ? Please police help us we beg you stop this malpractice in our city lilongwe .

    1. Zoonadi ineyo on sunday 9 july anatipakiranso 4-4 ndipo titawapeza apolice pa centuary tinauza and zotsatira zake anapatsana ndalama tikuona ndipo anangoti musamatero malu

  35. Lamulo liposa mphamvu amalawi timakonda zomapanga unkhutukumve chenjezo lita pelekedwa yachepaso ndalamayo amatilongeza ngati madengu ansomba anthu amenewa

  36. Bodza ili malamulo ameneyo adapangidwa liti? Ku nyumba ya malamuli sikunavomerezeko malamulo otero inali chabe presidential directive during Bingu administration.
    The driver can challenge this through an appeal. Ndizoona amalakwitsa koma likhale lamulo through parliament.

    1. Enemies of progress! Yamikani poyenera kuyamika osamangothamangira kunyoza boma pachilichose!
      Izi sizikugwirizanaso ndi ndale

    2. Acar or minibus has capacity, ie 15 exceeding the recommended capacity it’s wrong, bt miniming it’s capacity is evn awfull

    3. Chilichonse aphungu? Malamulo a mumpingonso ku parliament. Anyakwawanso malamulo a mmudzi mwawo azikapangidwa ku parliament. Ali ndi zambiri zochita aphungu ku parliament kuja.
      Tiyeni tikafuna kutsutsa development iliyonse tizibwera ndi mfundo yozibakilila. Tisamangolowesa ndale pa chilichonse.

    4. Amenewo simalamulo adziko laMalawi lokha it is supposed to b world wide pipo u just surport things which doznt even favour or cover us during accidents,n we r used kuyika umoyo wathu pachipyinjo tikunziwa kuti siziti thandiza

    5. che Richard Mphande Lyson apa bwanji manyadzi mulibe aliyense akukusutsani zinazi tamavomerani anthu afa mminseu aja 4 akanakhala ma brother ndi sister anu bola tikanaona kuti ndale zanuzo zithera pati ndangudutsamo….

    6. Not every goes through parliament.. For the constitution a law passes thru parliament laws for some government agents such the road traffic doesn’t necessarily need Parliament to deliberate.

    7. Malamulo anapangidwa kalekale alipo ngati uli real driver kapena minibus owner pita ukawerenge RTA (Road Traffic Act) chinavuta pakatipa enforcing the law sinali pa 100% panopo angoonjezera ma fines komanso milandu ina izipita ku court

  37. Congrats muziwatero atikwezera mitengo kumatiikanso 4_4 nde ife a Malawi ndikupusa kwathu sitimalankhulanso nde nkamanva zimenezi Ai ndithu zilibwino pitilizani kuwamangako alipo ambiri

  38. Tiona komwe zithere anayamba kuletsa kale. Ine ndinapakira 4 -4 popita kumangochi ndakumana ndi atraffic muzombamu mpaka lionde timangowaweva pobweraso ndapakira 4 4 plus matumba ndakumananawo ali busy pa whatsap ndangowapatsa moni zatha

  39. Personally, ifill it’s nt the way it should be, considering the fact tht a car has capacity, exceeding the capacity it’s a crime bt saying, a 4–4-3-3 should carry 3-3-3-3 it’s nosence. Iwonder hw did the authority reach on tht. Plus saying no acar aftr 10 it’s jst pathetic.

  40. Silamulo koma ndimene zimakhalila since kwa amene amapanga ma minibus ngati mipando yili 10 muyenera mukhale anthu 10 koma amamibus anali kutitenga ngati zisilu okwelafe mupando wa anthu 3 kupezekapo anthu 5 ndawi zina minibus kuzaza mpaka pakhomo komanso pomwepo papezekenso space ya condactor chonchi ngozi zapamsewu zingathe

    1. @ Julio dnt tell pple lies, a minibus has capacity of either 15, 14 or 16 ihv bin in SA thr is no such a thing tht a minibus should carry less thn it’s capacity,dnt misslead pple

    2. Ku SA amanyamura,4-4 -3-3 pamene kumalawi,akuti or mpando ukhale,wa 4 inyamule,3, thus y enafe,we are saying tsidzoona,cz the issue here is the new law says every minibus should carry, 3-3-3-3 or itakhara,ya 4-4-3-3,same wth ma bus thy are allowed to carry standing passengers bt the the new law says no,let’s b honest here, acar has capacity, exceeding it its a crime, bt minimising it is awfull too

    3. Asisi inenso ndili komkunotu koma minibus imadzadza mkupezeka ena oyimilila. Ndipo ma driver ambiri a kuno ndi ampwesa kuposanso a kumudziko. Ambirinso opanda ma license.
      Tiyeni tingokamba za kwathu tisafanizile ndi mayiko ena mapeto ake tisiya nkhani ili apa mkuyamba mtsutso wa ziii.

    4. Next time ukadzafuna kutchura dzina la a Tembo udzatchule mwa ulemu komanso udziwona ndinkhani zake zokhuzitsa anthu akulu-kulu ulemu ndiofunika

    5. Komatu apa Julio Nkuna ukunena zowona..ndankhara ndikukwera from pretoria to randberg..taxie imanyamula exactly anthu ofunika kukweramo.ndipo pamakhara anthu owonera amene akukwera .koma kukwanthu mmmmm aima njira yonse kuzaza anthu ngati matumba achimanga..koma even ma bus akwanthu kuzaza kwambiri ndichimene chimapangisa kuti driver agwese galimoto .

    6. Let me repeat what Julio Nkuna said: Thats good even here in RSA minibus singanyamule anthu odutsa muyeso ngati chimanga. Translation: A minibus cannot load more people than it’s capacity like bags of maize. Mwina simunamvetse. She didn’t say kuti minibus imanyamula anthu ochepera muyeso. Munakhalika bwanji anthu a mpanje. Jo’burg yake iti yomwe munaona minibus ikupanga overload anthu? I think mukunena mmene amakunyamulurani ngati matumba achimanga mukamapita kodyetsera ma horse mma farmer mwanumo…case closed. Julio Nkuna is right amene ukutsutsa izi joburg umangobwerako umakhala either ku Mozambique or Congo ndikomwe mukuchokera. Osandikwiitsapo apa….

    7. ndiekut chifukwa choti munapita kukagwira ukaidi Ku Jon mpaka mwaiwala chichewa eeeh koma aMalawi,mzanu walemba bwino Chichewa inu mukut simukumvesa

    8. Hey one ndimayendetsa taxi paweekend kuno kulibe 444. Quantum back sit 4 then ena 3 then yapafupi ndiye driver 4. That is 15 passengers and driver 16 no conductor.

    9. Harold phiri amene muli kundende ndinuyo kaya manyasa dziko lomvetsa chisoni ngati limenero sindidaliwone chakudya chomvala pogona zomvutikila kunyasalande ndikugahena

    10. OMWE MUNATHAWA KU MALAWI MUNALIBE POGWILA IFE KONKUNO TIKUPHAKA LIFE NO CHEU CHEU ZENOFOBIYA IKAYAMBIKA MESA MUMALILA INU KKKKKKKKK

    1. W@ da fuck u can tell me to keep qiet? U wanna tell me dat accident happenz only in a9t? Accident happens any tym day or 9t boss so there is no need to fine some1 so much money jst becoz of dat silly nonsense @ mac henz t banda,what ever u call ur self ok?

    1. Amwene apo zingoonekeratu kuti lamulolo linabwera kalekale simungavutikeso ndikufusa nokha mmaziwa kut galumoto imakhala ndi mlingo wakanyamulidwe ka anthu nde sizingafuneso paliament izi zimapangidwa pomwe galimotolo likupangidwa

Comments are closed.