Bullets yatuluka mu chikho cha Airtel Top 8

Advertisement
Malawi Indendepence

Ikakuona litsiro mvula sikata pofuna kukuchititsa gombe kuti uwonekere ng’amba ku wanthu kuti ndiwe wa umve. Izi zikufanana ndi zomwe zikuchitikira timu yayikulu ya Nyasa Big Bullets.

Mwambiwu ukulumana mapiko kwambiri ndi timu ya Bullets zomwe zitsekule maso kuti penapake pali vuto ku timu yayikuluyi.

Mavuto a kusachita bwino kwa Bullets ayangata ndi kumanga nthenje pamene zavundukuka kuti chiyambireni chaka cha mpira cha 2017 Bullets yavutika ndi kusosoledwa dzitsukwa mu masewero aliwonse.

Bullets vs Silver
Bullets (Mu zofiila) mumasewera ake ndi Silver Strikers ku Mulanje.

Chachikulu chachitika pamene timuyi yasenzetsedwa akatundu awo onse ndi kutulutsidwa mu chikho cha ma timu asanu ndi atatu a m’dziko muno cha Airtel.

Kuyambira tsiku limene bungwe loyendetsa masewero a mpira wa miyendo m’dziko muno la Football Association of Malawi (FAM) lidatsekulira chaka cha masewero mu 2017, timu ya Bullets yomwe idatenga chikho cha ligi chaka cha 2015 sidapambanepo masewero aliwonse.

Timuyi koyamba idatherana zilo kwa zilo pamene idasewera ndi Chitipa United mu chikho cha TNM, masewero awo a chiwiri adasewera ndi Silver Strikers pa bwalo la Bingu national sabata latha ndipo iwo adaluza ndi chigoli chimodzi kwa duu. Chigoli cha Silver adagoletsa ndi wosewera wakale wa Bullets Victor Limbani.

Mu masewero omwe iwo atulukira mu chikho cha tsopanochi lamulungu Bullets sidachinyane ndi timu ya Silver pa bwalo la Mulanje kupangitsa iwo kutuluka koma asadachinye chigoli ngakhale chimodzi cheni-chenichi mu chikho cha ndalama za nkhani nkhanichi.

Malingana ndi maganizo a anthu wena, timuyi ikuvutika kwambiri chifukwa ikusowa anyamata a njala kutsogolo pamene iwo a Bullets ati kusapambanaku m’chifukwa cha kuchoka kwa wawo wakale Chiukepo Msowoya yemwe pakali pano akusewera mpira m’dziko la South Africa.

Ena akuti osewera monga Muhammad Sulumba, Bright Munthali ndi Collins Nkhulambe akulephera kukhala ndi ukali, njala, nkhwidzi, chibaba ndi golo ngati m’mene adalili Chiukepo ali ku Nyasa.

Maso a Bullets tsopano ayang’ana chikho chachikulu chokha cha m’dziko muno cha TNM supa ligi pamene asemphana ndi ndalama zokwana 15 miliyoni kwacha kwa owina chikho choseweredwa nthawi yochepachi.

Ma timu a Nyasa Big Bullets, Azam Tigers, Mafco ndi Blue Eagles atuluka mu chikho cha Airtel pamene Mighty Beforward Wanderers, Silver Strikers, Moyale ndi Kamuzu Barracks apitilira mu ndime ina kuyandikira fungo la ndalama zochokera ku kampani ya ma foni a m’manjayi.

Advertisement

60 Comments

  1. Neba Mutu sukugwira,nanga athawira kuti poti nayo chitipa united akuyiopa

  2. Takamba ya Bushiru takamba ya Chaponda pano ndinthawi yokamba za Bullets nsopano Kkkkkkkkkk koma Neba anyway bola wabwerako wamoyo

  3. Bullets nd Mafco,,afa mwamanyaz ds season,,matimuwa amadalira striker mmodz at atym,,example,,adasiya Eneya banda nd victor Limban,,@ kukatenga SULUMBA,,pali mzeru..? Sulumba nd striker..? Mchoopsezera ana chja,,,, anya aona….

  4. Dakuwuzani Kale Abuletsi Palibechanu Chakachino Simuvapati Mulungu Amatenga Odzikweza Amamutsitsa Odzichepetsa Amamukweza Isiyeni Wandalazi Itenge Zikhozi Mudziwakale

  5. Admi nkhan ya bullents ndiye mwachita kukomesela chinyanja chenicheni chapakhomo osalemba mu chingelezi bwnji?nanu mungopitiliza ku ndikanda pachilondapopa iyaaaaaa mukufuna ndzingokwiyabe?

  6. Ine kuyambira lero nditsadzamvenso wina akuti peoples timu kunena Bullets , people’s timu ndi Noma , dzoona 4games no goal , ichi tsichitimu .

  7. Banker /Bwandiro United Timavomekenza,chawawavuta Ndi Mwano Kusaona Ena Ngati Ma Timu, Okumba Fulu Sakhala Ndi Phuma, Kupata Kwa Ana Akulu Sakodwa,nde Ayatsanso Bus,madoro Alero Ndi Makape Amawa.

  8. Eishh! Pepani. Komabe tamalimbikirani, nanga mukamapanda kutero Nyerere zizilimbana ndindani mu brantyre muno? Pull up ur socks please! Sizikukoma ata pang’ono.

  9. Admin Daily nkhani zina ulibe….

    This page is now useless
    We used to read so many stories but nowadays its all about football each and every hour

    Just change it to Malawi 24 Football …..whatever u like

    Moreover our Flames coach says we not playing football but tennis….the ball is being kicked end- to- end of the pitch aimlessly he says…

  10. inunso mutha kumameya miyendo mukinayo tiwone kuti muzingowina thawizonse, masewera ena amawina ena kulephera zizingatheke onse kuwina,

  11. Coach dont be panic mantain first eleven that will be starting not today another players sanga ngwilane miyendo nchoncho.monalakwitsa chotsa ana abwino ngati achina anzeru joseph ma midfielder abwino ma long balls zinatha kale kale .kodi engine yapa centre mkwate amamosilanje panja .Guyz chimango kaira salimwa kale or fodya .give them chance achina dave banda & collens nkhulambe kotsogolo & bright muthali we hve gud strike.koma ma midfielder adziyambita ana wothamanga dalitso sailesi ndi mkwate apanga create ma chance ndi ma freekick zomwe zipangitsa pressure ma team ena.

  12. Osamati team yaikulu ayi, enawa ndi maina chabe, ma team akuluakulu adanka ndokamuzu, uyu timamutcha #sizimthela fc kufikila ataupeza mtendele

Comments are closed.