A Malawi 300 ayenda wa uyo uyo ku Joni

Advertisement
South Africa Police

Nzika za ku Malawi zokwana 300 zomwe zimakhala m’dziko la South Africa koma opanda zikalata zokwanira azitumiza kuno kumudzi.

Potsimikiza za nkhaniyi, wachiwiri kwa m’neneli wa nthambi ya boma yowona zotuluka ndi kulowa a Wellington Chiponde ati theka la anthuwa lafika kale kuno kumudzi lachiwiri kudzera pa bwalo la ndege la Kamuzu ku Lilongwe.

Malingana ndi a Chiponde, anthu okwana 150 afika m’dziko muno ndipo ena akuyembekezeka kufika masiku akubwerawa.

Iwo anaonjezera kuti pamene anthuwa akufika kuno kumudzi, athu ena okwana 849 awambwandila ndipo akusungidwa chifukwa chosatsatila ndondomeko zofikira ndi kukhalira m’dziko la chilendolo.

Chiponde wachenjeza a Malawi kuti azitsata ndondomeko ndi malamulo otulukira m’dziko muno kupita ku mayiko a kunja popewa kubwezedwa mokakamiza, mwa chipongwe ndi mochotsa ulemu.

“Tikupempha a Malawi kuti adzitsata ndondomeko ndi malamulo oyendera nthawi zonse, kukhala ndi chiphaso sikokwana koma kudziwa zonse za zomwe dziko lililonse lomwe akupitalo limafuna pa anthu onse olowa m’dzikomo,” adalankhula choncho a Chiponde.

A Malawi ambiri amalowera ku South Africa komwe amakasaka mwayi wa ntchito, ndipo choopsa kwambiri ndi choti amalawi ena amadzera njira za chidule komanso opanda zikalata zoyendera pa ulendo kupita ku dzikolo.

Pafupifupi chaka chilichonse boma la Malawi limaononga ndalama zochuluka kubweretsa anthuwa kuno kumudzi ku South Africa kukasokonekera kapena akathothedwako mwa chikhadzakhadza zomwe zimasokoneza ndondomeko ya za chuma cha dziko lino ngati silidaike ndalama zapadera.

Advertisement

165 Comments

  1. kodi ngat pali a2 omwe tikukhala mopanda ma paper a dziko lino nd ife amalawi and ine ndimakhala ngat ndili kwathu Ku mangochi sindidanda zoti eeeh police what what No kugwidwa nd nthawi ine kunditumiza lero mawa kukwera kumabwelanso konkuno chifukwa Malawi palibe chomwe ndingapange kulibe ntchito nde Ku nkhan yogwira kuno akugwira daily and azigwirabe koma ife nde sitisiya kubwera dziko lino mayaz osatheka tizibwera Iwo azigwira nd ntchito yawo

  2. Hahahahahahahahahahaha I don’t care about deportation kkkk ubwino wake samakumenya ayi komanso umakagona malo abwino kudya chakudya chabwino plus kumwanso tea kkkkkkkkkk chodandaulitsa ndi chani pamenepo

    Ndipo ndangotsala ndi miyezi yochepa chabe kuti ndibwere ndizakukembeni ntchito amalawinu including uyu walemba nkhaniyi get ready to be employed

  3. If in Mw there z no deportation wich minz its a dead country coz ich and country deportation tek place .So dnt b surprised ,bt jst undrstsnd that!

  4. A Malawi ku South Africa ali pawiri.
    {1}Pali omwe akungodyelela sakukumbukila kumudzi moti alibe kalikonse kumudzi.
    {1} Pali omwe amadziwa kuti anazela umphawi ndipo anapanga zazikulu zomwe wonyozawe ulibe. Ndikunenapano ena amene mukunyozanu kuphatikizapo wolembayu mulibe nyumba. Enanu ndi ma tenant a munthu wa ku Joni yemweyo. Pali ena sli ndi ma plot kumudziko pa mwezi akumatolela K200,000. Enanu abale anu ndi ma driver akusamala mabanja awo chifukwa choti akuyendesa mini bus ya munthu wa Joni. Ena a Malawi akuyenda mma galimoto apamwamba pomwe wonyozawe kakaka njinga ya Humber. Anthu oterewa olo asabwelele sikuti angavutike. Azangobwelela chifukwa choti ali ndi maso mphenya akuluakulu omwe akufuna kuti akwanilise.
    Ndipo ma document akunenedwawo ndi ma work permit ndi asylums omwe amapelekedwa ndi boma la South Africa, omwe bomalo silikupeleka kwa anthu. Paliponse pamene pali zabwino pali mavuto. Ndipo deportation inaliko munthu ukamabwera umadziwa kuti kuli deportation. Ndipo a Malawi ali paliponse pa dziko lapansili si ku Joni kokha. Ena akutumizidwa ku UK bwanji simulemba? Ndiye wina ukuti akuthawa kulima, yes you are right akuthawadi kulima chifukwa mulibe phindu mu ulimimo. Anthu mukuvutika koma busy kunyonza.

  5. IFE TIDZAPANGIDWA DEPORT KOMA SIIDZASIYA KUKHALA DZIKO LINO LA SOUTH AFRICA NDIPO NDIYE AMENE APANGIDWA DEPORT WO MUWAUZE ADZABWELA TRANSPORT TIDZAWATHANDIZA KUTUMIZA KAYA NDI PAY FORWAD AZIBWELA BASI NYASALANDE UMPHAWI ULI THOOOO NDI NDANI ANGAMALIPILE LEBALA MK 150,000,00 kadzibwelani guys asiyileni chidziko cha mbava chawocho

  6. A Malawi amene tilibe ma pepala okwanira kuno Ku Joni timaziwa kale kuti anytime something can happen nothing strange amene agwidwawo abweranso …… Ndiye izo zakuti ……ayenda uyo uyo mmmmm it doesn’t make sense

  7. Mukamati uyo uyo ndiye kuti chiyani? Mukanakhala anthu achulungamo potsongolera dzikolo sibwezi anthu akuthawa koma mukungoba ndalama za boma basi ibani ndalama za aphawizo, tikuthawa umphawi umene mutisaukitsau.

    1. muwuzeni man manyasalande ena ambiriwa ndi opusa okula ngati dzungu lokalambila pomwe linabadwila akuwona ngati ku nyasalande chomwe unganyadile ndi chiyani umphawi uli thoooo

  8. malawi 24 phuma….. mmene tinkapita ku joniko tidakusanzikani???? nde pot tkubwera mwati mutitchukise??? kusowa zolemba bax,,, mphuno ngat pagwada chule

  9. Mmmmmm mmwamuna akuyenera kupita kosaka .zotumizanaz zimangochitika.koma bvuo la likulu ku south Africa ndi apolice.Apolice amavuta or uli ndi passport ngakhale kut imnakhala itatha matsiku amat zipulumuse cozz iwo amafuna dola ndipo ngat ulibe umachita mwayi kukwera galimoto yosalipira.chinyengo mdziko lapansi ndithu sichizatha.koma pot kwa eni ndi kwa eni zatilaka ndife.

  10. South african home affairs,Ife tikuthokodza potigwilila ndikutumizila m’bale wathu yomwe anapita kumeneko pakanthawi ndithu koma palibe chomwe amapangako,mtima umeneu musausiye muagwililenso ena azibale awo omwe ndalama akungothela mowa,akadzi ndi zina,cuz palibe chaphindu,azingobwela mwina kuno azizapanga zooneka,zikomo.

  11. South african home affairs,Ife tikuthokodza potigwilila ndikutumizila m’bale wathu yomwe anapita kumeneko pakanthawi ndithu koma palibe chomwe amapangako,mtima umeneu musausiye muagwililenso ena azibale awo omwe ndalama akungothela mowa,akadzi ndi zina,cuz palibe chaphindu,azingobwela mwina kuno azizapanga zooneka,zikomo.

    1. ukanakha kut unabadwa mwa umunthu siukananena mbwelera zakozi. zimangochitika malingana ndi mmene anakonzera mulungu koma ndizokut faz imazunzika hvy,samala ndimalankhulidwe akowo iweso ndimunthu wamamuna uzakumana nazo

    2. Amalawianianz omwe akuvutika ndi amalawianianz omwe akupanga zibwana isn’t de same cuz nobody gonna feel sorry 4de latter,olo atagwidwa.

  12. Ndiye pali chifukwa cholbela zonyoza apa apita kwao kumalawi sanapite ku zambia kapena kumozambique ,palibe chifukwa chonyozela apa .atipezaso amenewa tiwafunila zabwino zose .Inu ba nyozan

  13. Za pa chipyenthe basi mwasowa zalembaa? ? Uyo uyo nde kuti chani ?Kapena chiyani? ? Busy kupempherera abale ndi alongosi zoipa Kutereku mtima wakuphwani ophunzira koma mbuli mbuzi ya meeeee mwasowa zalembaa???? Zithe!!! Wats funny wen u say uyo uyo! Who or wat tell us now!!! If u were given an assignment,
    U have got 0%. At least your brothers and sisters are seriously trying their luckies. Never post such dirty history please please.

  14. Olembawo Mongoziwa kuti iwowo ndiajerasi Kono tikusukunula sikwacha ndi Rand Abale musakhumudwe bwelani tizisukunula Amenewo Oyankhula asiyeni saziwa Aka mayimba Foni kuti madam NDA tumiza pitani mukatenge Zimawanyasa

  15. Inu ndi abale a2 ,osadanda ife kuno tayamba kale kusokhelana ndalama za transport yobwererela Ku thebako , kuti mukamalizitse zomwe munapitila.

  16. Ife tikanadya KFC,Buliyani ndi zina zotelo,Therere ndi Usipa tapumako for Fucken three years.Kwama fanz omwe munavayanu,Zabwino zonse Transport ikapezeka Zibwelani,coz Bolako kusiyana ndikupalasa Dam’pa + kuumba njewra.Off couse fanz ima talker zambiri za joz koma sitimalabada coz Sitinakapemphe Dollar yobwerela kuno mmakwao.

  17. Yes we are blaming our government why they are failing to give them proper documents?Zimbabwe,Lesotho & other countries…….why Malawi?All you know is cash gate kukamwa kwa president wanuyo.

    1. The government isn’t failing to give them proper documents but they not applying for visas of any kind like working permits,business so on.

    2. Permits ndiyodula,Munthu oti ukungonyamuka kuchoka kumalawi kubwela kuno,Sukudziwa kuti ukangwira ntchito yanji,Ndipovuta kuti upeze Zi kalata.

  18. Ine ndili muno ndipo ndikumva kukomaa ndimangomva chisoni mukamanyoza kaya mumangwila vep yanji koma pa land simungamake mayaz kuno fanz simakumba zimbuzi uncle musazanamizindwee SA singafane ndi mpanje mayaz kulibe thelele kuno mukamanyoza muziziwa zimenezo and kut ubwele kuno ndi ndrama kwa omwe mumanyoza muzizipenya Kaye oky hahahaha anthu enanu

  19. Ananditenga cha mma 13:00 pa Delville koma ananditaya patangotha 10min nditawapatsa R60. Passport ndinayisiya kunyumba dala chifukwa muli Work permit ya fake

  20. Hendrex! you have spocken. lyf is lyk that its difficult to get good things on siliver planter. we wish them all the best as they are travelling back home. hope they will get us here

  21. Bola oyenda “uyo uyo” chifukwa wakwela ndege abwelaso..kusiyana ndi amene akuphedwa ndi a zimayi amene akukugwililidwa opanda ma documents..mtipeza guys osadanda bola moyo

  22. kkkkkk koma guys munthu olemba nkhani zachichewa ndi otsangalatsa kwambiri ayenda uyo uyo ziko lonse south Africa mulibe chilangulindwe chotere anu anthu olemba nkhani za chichewa mukudzithenga kuti zimenezo

  23. Munkatiopseza za zenophobia,,
    pano mwasowa zolemba,,,uyo uyo,,,what meaning????
    Forsake
    sabisa ezingan ayii mina,,
    angnsaba ,,,,,,

  24. takulandlan ku malaw kma zithu sinasitha kuli k200 yogwlana ena akumat trump, magetsi asiya kuzima sugar ndi k1015 bola mulimbe

  25. KUSOWA CHOLEMBA BWELANI MUDZADYE NAWO VOLOSO KUNO ZAUSILU ETI ANABWELA KWANU KUDZAPEPHA TRANSPORT? Ubwino wake abwela alimoyo kumeneko abwelaso tiwalandila joz Ku koma iiiiiii

  26. Paja mwakolala kumene chimanga mwayamba kukhuta ndichifukwa chake mwayamba kulemba zopenga ndi ma comment anuwa opusa max

  27. This happen every country. If one has no proper docoments ,that one is not allowed to stay in that country. Nothing strange here….no proper docoment expect to be deported!!!!

    1. Inetu si mlimi and if u want to know more about me, ask APM atha kundifufuza pa payroll ya ntchito za boma n’kundipeza. Sikuti ngati ndanena zolimazo nde kuti ndmalima ayi. Kupita ku South Africa komwe mukuthamangisidwako mesa mukusowa chochita ku Malawi kuno? Ine m’mene ndilili kuno ndinganyasidwe kumapita dziko loti ndizikakumba zimbuzi za eni m’malo modikira month-end kuti salary yanga ilowe? Hahahaha, mukhalira yomweyo yomayennda chothawa kuopa kubalamusidwa dziko la eni ake

    2. Those who run away from Malawi to SA do not have greener pastures in Malawi but I do,,,, and I can’t go to a country full of deportation like that

    1. mukupusitsana inu manyasalande okula ngati dzungu lokalambiri pomwe linabadwira za ziii chamzeru ndi chiyani chomwe mungatiwuze kupatula kuba

  28. Ifeyo tikamabwela timaziwakuti amangwila ndiye mukamalemba khani zanuzo muziwona ayenda bwauyouyo ndiye kutichini,osadandaula guyz mutipezaso ena ndikunena pano anyamuka kale akubwela.

    1. mbuli zambili ku nyasalande zimawona ngati zikadya gaga ndiwo thelere kupangidwa deport ndiye kuti wabvutika kwambiri ndiwopusa amenewa

    1. why gvmnt shud give them something to do??? there are many pipo who are here and have nothing to do. How special are they than those who are already here????????

Comments are closed.