A Kamlepo atulukamo mu tchire muja: abwela ali onjatwa

Advertisement

Phungu wa dera la kummawa mu boma la Rumphi, a Kamlepo Kalua, apezeka patatha sabata osaoneka.

Kamlepo Kalua
A Kamlepo

A Kalua apezeka lero cha kummawaku mu boma la Blantyre, mmbali mwa mseu.

Malinga ndi malipoti, a Kalua ati anaponyedwa mmbali mwa mseu wa pa Njamba ndi anthu amene sakuwadziwa. Iwo ati anthuwo anangowaponya iwo ndi kubanduka basi.

Atafunsidwa kuti anthuwo amawasunga kuti, a Kalua anena kuti sangathe kukumbukila kumene amawasunga.

A Kalua apezeka atamangidwa ndi zingwe za Blue umene ndi mtundu wa chipani cholamula cha DPP.

Koma a Malawi ambiri anena kuti a Kalua samasungidwa mokakamiza ndipo iwo anangobisala pofuna kuipitsa mbiri ya chipani cholamula cha DPP.

Anthu akudabwa kuti a Kalua apezeka akuoneka osamba bwino, ndevu zometa bwino ndi tsitsi lotchetcha bwinobwino.

Advertisement

273 Comments

  1. AVE MADZI MTUMBUKA AMENEYU , MAYENJE AMENE AMAKUMBIRA ANZAKE WAXAMBA KUGWERAMO YEKHA. MUMU FINYE KWAMBIRI ASANZE MABANZI AMENE WAKHALA AKUDYA

  2. kaya bola kukandichera ine ndimayamika ambuye komaso kumupempha kuti andininkhe chakudya zikatero nkuyambapo kuthamangathamanga koma dza awa mumati andalewa aaaaaa sanandipangirepo chokma chiyambireni democracy aliyense amangokhutisa mimba yache ndie kuwasapota iz a total waste of time .eeeeetu

  3. kaya bola kukandichera ine ndimayamika ambuye komaso kumupempha kuti andininkhe chakudya zikatero nkuyambapo kuthamangathamanga koma dza awa mumati andalewa aaaaaa sanandipangirepo chokma chiyambireni democracy aliyense amangokhutisa mimba yache ndie kuwasapota iz a total waste of time .eeeeetu

  4. Kkkkkkkk kunja kukangoti kukangoch kwacha nkhani zake zokhazokhazo kumangolimbana ndi boma basi,ziti tiziganiza kuti biznezi yanga ingatukuke bwanji,naga chito yanga ndikuyenda bwanji? Ndi zona zotelo, koma eee kamulep eee peter eeee Chakwela eeee Bakili iiiiiiii, muzingolimbana ndi zimene mumapanga pakhomo panu kuti Moyo wanu ndi wa ana and utukuke,Sindine wandale ai ndipo ndilibe chipani izi ndangonena sindili uko muli,ndili uko komwe inu musali

  5. Amalawi Timakhala Ndi Mind Set Ofuna Kuyitsa Mbiri Ya Azathu Khani Ndiyakuti Kaluwa Watchela Ku Paliament Basi Ngati Anali Ku Chibwezi Angonena Akazi Ake Amukhulukila Akambila Kma Osati Zabodzazo

  6. I’m not surprised at Malawians ladies and gentlemen. True Malawian would agree with me that for along time our enemies have been hunger,disease and jealousy. At least we were done away with the two half way but jealousy is right there untouched. Let’s pray that God should do it for us.Even outside Malawi, you can’t trust your fellow Malawian. It’s better to live with someone else but not Malawian for the same reason ( jealousy)

  7. zabodza izi munthu wopangidwa chipongwe sangakhale pansi atafunda jacket koma osamba bwinobwino,anachita kulawilila mammawa kukatulidwa ndi munthu nkuzikhazika pansi paja atasamba kale wausilu zachamba izooo

  8. Kkkkkkkkkk koma amalawi sitidzathekadi ndie kuti akanakhala kuti wamangidwa ndi chingwe cha rainbow m’maonekedwe mukanati wanjatidwa ku joni? Ok nanga chikanakhala cha white mukanati chani chingwe ndi chingwe basi vuto ndiloti ife anthu timalephera kusata chilungamo pazolinga zathu,timachuluka nzeru koma osapeleka solution ya vutolo shame to all those who thought they are wise enough than others we are all in the same boat

  9. Tingodikira freddokiss awulura paja ndiyemwe amatiululira mu ndakatulo zake zija “anapha mphwiyo ndani? Mchifukwa chain? Nothing is impossible, yesu anadzutsatu Lazaro atadiwa” π kkkkkkkkkk timumvaso akutokota za madalawa

  10. Kuyambila lero inemwana wabambo billiat ndikulengezakuti phungutisanamusankheazipita kukayezedwa mmutumwake kuchipatala kutimutuwakewasalazakazingati kutiuzungulire akati zitatu ngatiakamulepowa tisamawasankhe

  11. the whole of kalua doing that,,,,malawi full of shameful legislators.Pa dzana wina anagona m,pariament ,lero mukut kalua.Fuko langa,why coming only after the openning of parliament?you are coming and with no explanation!!or bodza ulibeko ayi??ukanangolikocha tikanakhulupilira.Bambo amunthu kuthawa udindo,,l could love if they could take you a place where you could get on the track before joinning the parliament cos theres nothing you will contribute…Shame on you

  12. Anthuni ndinu atulo,mukungo bwetuka,zoona muzimva.khalani pheee,atsilikali sanena akamapanga chinthu,

    Anthu akumukonda Kaluwa,musaiwale munamanga mussa lelo ndi kamulepo.mkanika tiona

  13. kamlepo amatimilira umanena zoona teach them zandale enawa samazidzwa ngt zinthu szkuyenda osasiya kuyankhla ku boma kumangdwa kulibe ntchto sanakumange pakamwa speak out kamlepo am proud of u….

  14. Wayamba misala Kamlepo komanso kufuna kuipitsa mbiri ya chipani cholamula ndizibwenzi zake,,,,,komanso anawuza girlfriend wake kuti amunjate, chutsiru chamunthu.

  15. Wandale ndiwovuta kumvesetsa kapena kumvela chisoni chifukwa choona amachiziwa ndi eni ake andalewo nde kutaya nthawi za kalua kapena pita kwaine ndikuona zosathandiza anthu ofuna anzawo zikavuta koma pakalowa mbewa ndikumba ndekha

  16. A kamulepo mudakula bwino bwanj , kulolela kukagona pa lound about kuli kufuna dolla kumeneko? Aaa ukhalike ayise ngat munali ku room tangonenani akaxanu mukambilana nawo man osa yokalikayo ayise

  17. Akamlepo pliz pliz chamba mukusuta panochi kaya mukumachigula kuti pepani ndithu chisiyeni pliz mubanda udyo kuchita kumposa manganya

  18. Musakambe zambiri ngati maganizo ake mukuwadziwa. Kamlepo ndi khuluku.walemba mmadzi,achule awerenga.waona kuti ma allowance aku parament sawaona kkkkk.Kuthawa anthu anamvotera ku Rumphi kudzabisala kuno.mukutithera malo kuno osakatukula kumpoto bwanji?nkhalango yokhayokha osakazimangirira kumpoto kwanu konko?hehede misala ija yayamba kulowelera

  19. This is exactly like what happened to late Chasowa. He was dumped at a spot where he was not initially killed and remember the stories that were told. Mind you those killers are still out there enjoying normal life. Wait for true facts to come out people.

    1. Sizikugwirizana kumene chasowa anali atafa nanga babawa anali nditizingwe ta blue cholinga azinamizila DPP watchera kumwezi nkhanga za thaima Mwana Tchwee

  20. We are too quick to judge even in the absence of all or enough information.

    What if? What if? What if the kidnappers deliberately staged the release of Kamplepo Kalua in this manner knowing that people will react exactly the way they have?

    He was clean. In tidy clothes. Well shaved.

    The only reason or main reason why people are doubting Kamplepo is that he was clean.

    Hypothetically speaking, he was sedated. Cleaned and dumped.

    Lets see this from another angle.

    That said, I am not saying Kamplepo is caught pants down or that the people are wrong.

    Just look at it from another angle. Copied from PK

  21. thiuzeni soona bt dis guy stlu live to same the.ry bt. duwhing sath. ulong loock.is not nys guys rykyt dis Dpp ai thik wht too dis ayenela kumpitha. kumeto basi

  22. There was a byelection in Dedza central west in 2001. UDF was in power then with aTcheya at the helm. Marshal the Duke was the UDF campaign director for that by election. It was catastrophic. People were not patronising the UDF rallies but MCP’s. On this day Justin Malewezi VP then had a rally outside Lobi. Marshal and his friends ( young democrats) went there paraded all the chiefs before Malewezi having UDF badges stack on their jackets. All of them unwillingly had been put on UDF t- shirts. Yellow!!! This has reminded me of Hon. Kamlepo Kalua tied with blue strings (DPP colours) to indoctrinate Kamlepo or in other words DPP showing to the whole world they are in command. They couldn’t kill Kamlepo because the whole world was watching with their cameras full throttle. Malawian politics!! I like history to relate events as repeats.

  23. Kamulepo Ndiwamkulu ndipo amalankhula mutamufunsa akumati anali kuti?asatipusitse ameneyu mwinatu anakangana ndi dona yake ndiye amakapitidwa mphepo kaya

  24. admini kawauze amakutumao kut alipo angapo akutha kuzindizikira kut mwangokanika kumupha like u did wth chasowa and njaunju… and ali ndi nkhawa kut chilipo mwamuchita

  25. Ine ndingokambako zayapa tsangano yokhayo zinazi mmmm ayi ndingayambe kuchimwa nazo coz Dzikoli lafika pondikwiitsa. Nde mwati a police patsangano anasambisidwa chokweza makofi ndanyamata achipani cha bambo Awo?? kkkkkk akudziwana asiyeni akana kuikoka kwambiri akudziwa kuti awonekela ng’amba ndamodzi amasapota munthu mmodzi nde sangalimbane. akanakhala wa Otsutsa ndithu pano komusunga kusakudziwika, Nde apapa chongofunika ndikumangoyang’ana Kuchitila kuti tikakamba zambiri Abwera kwa wina Mudzina la MRA akufuna kudzakutenga nde eeeeeh ayi tiziona kkkkk koma osamakhala mowopsezana Tonse ndilathu dzikoli

  26. ndie ngati a polisi anavulazidwa ndi a chipani, kuli kovuta bwanji munthu mmodzi pano ma cadet awopsya ndie poti anaphatikizana ndi ma young democrate eeeee ziliko ofunika apite ku darfu kapena ku nigeria

    1. U know wat Kelvin if this was his first attempt it could have bin another issue but akuti nkachiwiri kupanga film yomweyomweyi…..Last tym he did this in UDF regime that’s why people have lost hope in him

  27. kkkkkkkk kma ma journalist enawa nde chabwno akanamangidwa nd chigwe cha red mukananena kut nd MCP??? Or orange mukananane kut PP…..be profesional wen wrttng ur stories. …aint a DPP supporter bt aaaahh shame on u!!!!

  28. kodi ndizimene mwayamba kumuzunza munthu nkuyambaso kumusemera nkhani, kodi osathana kaye ndi nkhani yopunphuntha amene akugwira ncthito

  29. mseweroli anyoni anali kamlepo kaluwa, Giring,ande anali a MRA, Dimingu anali Fredokis ndipo amfumu anali a DPP walemba ndi Kamlepo Kaluwa wakonza ndi a DPP

  30. Zoona muthuwakuluyo akasowe zachamba kuteloku zachezayela pamenepo sitidziwa watumayo wamulonjeza zingati koma ndalama ndiyachabe ndawonela kaluwa

  31. Chiwerengero cha anthu a misala chikukwerebe wina nde nd ameneyi, posachedwapa uyamba kupezeka mmisika iwe, Wapupwa iwe Kamlepo, bambo ache Fredokiss

  32. Ndemwati Kamulepo Angazimange Yekha? Lalephera Chabe Boma Kumupha, Analimbana Ndi Kamuzu, Buluzi, Bingu Nde Bwampini Munthu Wopanda Mano Mkamwa Angatani? Tisiyilen Ndiyekhayu Munthu Wolimba Mtimatu,

  33. Ngati ili mbili azionongera okha osati kutchula za chipani, kodi nkhani yake kuti mpaka afike posowa zinali za ndale ngati. a Kalua kulani bwino osati za uchitsiluzo, kusungidwa ndi zigawenga osalandira chipyera a! zabodza izi a kalua, ndale siizi. Nyengo ino tayambayi ndiyokuti tizionera ndikumvera mpira osati zambwererazo. Izo ndi nyakanyaka zanu mwamva…..

    1. Mbuzi kaluwa galu weniweni ndale yanji iyi ara kukhala uko mkumanama kt Dpp ikufuna kuwapha kutitenga opha kwambiri chani? Mbuziiii!!!! Ndisaveso 2019 tili mBoma be

  34. Munthu akuoneka kuti amamwabe tea wamkaka achikhala amasungidwa mokakamizidwa sakanaoneka chonchi kkk koma mtundu inai mmmh

  35. Let’s wait, atiyakhula bambo kamlepo paja anyamata antambo wa blue mumathakupanga chilichose,dzana mwakwapula a police pa tsangano chingakuvuteni ndichani.

  36. Mr kamulepo wayamba misala ndi ofunika kumutengela Ku chipatala cha anthu a misala Ku Zomba. munthu osowesedwa samaoneka ngati uyu. I hope some went missing in his medulla

    1. palibe vuto bola ndanena chilungamo mukachedwa naye akuvutisani. muthoyu wayamba kuchitisa manyanzi anthu omwe adamuvotela and i don’t think he will win again this coming election 2019

    2. not on surface but deep down. ndiye ngati alibe misala tamufuseni bwino akuuze kuti anthu anamubisawo ndi akuti naga amusiya chifukwa chani.? this is nonsense

  37. Kkkk Kamulepo wayiwerenga kuti ngati angamakhalebe kuchibwezi mudzina loti wasowa aphonyana ndi ma allowance aku parliament hahaha akalongosola bwino kwa mkazi wake

    1. Ungandichite chani iweyo Mselema Roddy Felix ? Zopusa basi. Ngati Kamulepo ali malume ako uwauze kuti dziko silinayambe ndi iwo.

    2. inu mzanu anali mmavuto(aakulutu Willard Chikomo Cosmas Kholowa Evance Gopanje Noel Wathanzi Kasinja Maxy Kay Phiri Pempherai Likome

  38. last time when chaponda burn his office people was sayn thats not true chaponda cant burn his office alipo waotcha akufuna kuti tiziganiza kuti waotcha yekha after 1 week ndalama zinapezeka and everyone started believn kuti Dr burnt his office!!! same in this scenario wht if those guys abducted him want us to think mmene mukuganizira kuti he’s jyst kidding!! the trueth will be reviewed

    1. man ndnu akape heavy are yu saying muthu opangidwa kidnap amaoneka choncho hahaha akufna kunamiza mwana chan ,, ndye bwezi mwana wake ali busy ma dance ku comesa last friday bambo ake atasowa think malume ndi tricky offcourse zthu dziko muno szikuenda bhoo kmano tasamange zthu zoti tizipuzana wats dat ,,childship mission zachikalekale

    2. U r ryt my bro the problem is :,most of DPP guys r on social media trying to defend their masters but we as malawians know the truth so if u see these cadetes all over social media just leave them ,thus y they r beating police now by blaming them kut akusapota mcp ,ungoziwilatu kut ambiri ndi mbuli

  39. hahahaha koma kamlepo tazikulani madram amenewa penapake aaaaaa olo bola akanazipaka matope ndi kuvala kabudula kukhala opanda malaya mwina koma dram imeneyi ndiye aaaa

    1. Apeze njila inaso bwanji oti ife timadziwa kale kuti DPP ndiyakupha Chasowa, komaso pa 2o July ina ndikhani ikukanikayi yamunthu waACB adaphedwa uja, ndiye mufuna Kamulepo ndiye akudziwitseni zimenezi?

    2. Kamulepo kaluwa mutu wake sugwira paja mankhwala aanthu openga ngat awa adatha et…. Mu2 mkulukulu kumanama ngat chimwana aone zina osati njira yake imeneyi aaaa kumakula

    1. Big! simukunama chingakhale panopakati alomwewa adzadza kumautenant koma chomwe chimandidabwitsa ndiichi amati tivotela wakwathu koma mavuto sawachokaso kumadzapemphetsaso pakati pano ndikumpoto aleke kuganiza mwauchitsilu chifukwa tidzaleka kuzilandila zitsilu zimenezi.

    2. @Gondwe & Mphamba # Kambani zandale basi osati mtundu kapena chigawo muziganiza mwakuya ngati wanthu osati zinyama!Abale anu nonsenu timakhala nawo bwino kuno kumwera ndipo ena ndima best friend.Samalani polankhula!!!!!

  40. watopamo mtchire waona kuti palibe uyo akumutsata mtchiremo komanso after kunva kuti anzake ayamba kulandila ma alawamce ku parliament ndiy wangoti ndinjateni ndikachotse manyanzi kunjako

  41. Muzati akufuna kuipitsa mbiri munthu akufa uku. ……..ndani angaipitse mbiri ya DPP popeza mbiri yawo inaipa kale kale ndi chipani chokupha aliyense amadziwa. …….mwawamanga ndi zingwe za blue basi ife taona kkkkkk

    1. Somehow chinachake chachitika kwamkuluyu kuti anthu ife tione ngati azipanga yekha soon after apolisi atanena kuti sangamusake basi iye kupezeka mmmmm

    2. Yah these people r killers and if w Malawians will keep silent and watch will finish all by this idiot mtchona. ……. koma amumva chwe mwana chwe!!

    3. Fulture Wise Ndikugwilizana Nanu Coz DPP Yomwe Ilipoyi Si Yomwe Idalipo Kale Lija Mbiri Yao Idaipa Awa Ndipo Akupanga Mwakufuna Kwao Posawelengela Za Ufulu, Kod Munthu Wamkulu Ngat Ameneo Angapange Zinthu Zot Aipitse Chipan? Kod Jessy Kabwila Sadasakidwe Atabisala Kufuna Kuchitidwa Chipongwe Ndi Akanganya Omweo A DPP Kuno Ku 36? Kuotcha Galimoto Yake Ku Golf Club? Ndie Tidziti Naenso Amafuna Kuipitsa Chipan? Akadafanso Bwez Akut Wapanganso Dala ? Malawi Wafika Pa Chilombo Safuna Oposition

    4. Ndamva zoti ma cadets amenya apolice…..nde amalawi umboni wake ukhale waukulu bwanji kut amvetsese kut DPP ndi yokupha? ??? Still in remembering Chasowa and Njaunju DPP the killers

    5. Munthu sangakabe kwa a neba mkusiyako Malaya ake odziwika bwino ikanakhala DPP akanawamanga ndi mawaya kapena mtundu wins wake osati blue amalawi mmaso mudzayela liti?

    6. Bodza inu nzeru zanuzi izi nde za akafula iwe u dnt knw kut akupangila dala cholinga ife tisakhulupilire zimenezi? DPP cadets yamenya apolice two days ago this is another witness kut chipan chimenechi mchakhaza kmanso chokupha…….mukawauze aputa nkhondo yomwe saimaliza Kamlepo iiiiiiiih ndi chwee mwana chwee

Comments are closed.