Midoli, Win ikupangabe makani pamsika

Advertisement
Midori

Ngakhale bungwe loyeza zakudya m’dziko muno la Malawi Bureau of Standards (MBS) lidaletsa mowa wa mmabotolo a plastic, mowawu ukupezekabe pa msika mma boma ambiri mdziko muno.

Diso lakuthwa la Malawi24 lapeza kuti mowawu omwe ukukhalabe mu mabotolo a plastic ukugulitsidwa m’misika ngakhale MBS idaletsa zomwe zasonyeza kuti ogulitsa sakufuna kumvera zomwe MBS ikufuna.

Mkalabongo
Mowa onga uwu ulibe pa msika.

Ngakhale kupakila mowa mu ma pakete komanso m’mabotolo a plastic kuli koletsedwa M’malawi muno Malawi24 yapeza kut ku Lilongwe madera ena monga area 36, 23, Mtandile ndi Mitundu mowawu ukupezekabe pa Nsika.

Mu mzinda wa zamalonda mdziko muno wa Blantyre, Midoli, win, Shooter ndi mowa wina ukupezekabe mu ma dera ena monga Mbayani, Manje, Bangwe ndi ma dera ochuluka ena mu Mzindawu.

Malingana ndi Chigamulo kuchokera ku bwalo la milandu Mdziko muno pa 4 January lidaikira kumbuyo MBS kuti kupanga ndi kulongedza ndi kugulitsa mowa mma sacheti ndi m’mabotolo a plastic mkoletsedwaa.

Mchaka cha 2010 kuletsa mowa wa mtunduwu kudaomba m’golo pamene ma kampane opanga ndi kupakila mowawu adakatenga chiletso ku bwalo la milandu kutsutsana ndi kukanizidwa kupanga mowawu.

M’malingana ndi MBS, iwo anenetsa kuti ulendo uno palibe kampani yomwe ichite matukutuku kupangabe mowawu ndi kulongedza m’mabotolo a plastic.

“MBS ikudziwitsa anthu ndi ma kampani onse opanga mowa wa ma spirits kuti ulendo uno akwanilitsa kuletsa mowawu (MBS therefore wushes to inform the general public and manufacturees of the spiritious liquor that it will implement the ban following the rulling the general public and all manufacturers are heteby advised to comply with the MBS Act Cap 51:02 as stipulated in MS 210 (1990)”. idatero MBS mchikalat chawo.

Advertisement

78 Comments

  1. kodi mukudana ndi mabotolo a plastic kapena mowa??? kapena inu a MBS mwangotumidwa ndima company ena amene akupanga moyo koma pano mwina sizikuyenda kamba kakubwera ka mowayu kkkkk

  2. Kodi akasiya Muwapatsa tchito ndikunena ndiiwe wa police galu wa munthu wa kutumayo ndani kapena iweyo pita mbuzi yamunthu anthuwo akadyaa Kunyumba kwanu zitsiru inu galu nonse mukulephera ku Manga akuba ndalama za boma

  3. Super midoli its a best beer in malawi,what is M. B.S.?asiyeni anthu azimwa wotchipawu mukufuna muwabele alimi asoya,ndi fodya powagulitsa mowa wodulawo? mapazi anu.

  4. Muhule ndiye kumachita kuwatamandila kuwapasa makondomu 30000 aliyense pamwezi chifukwa ndi akazi tisiye ni mowawu ndi wamabiggie ngati ife tinalakwa chani kukhala olezera mowa supereka edzi mwamva tumwe tumwe basi

  5. kuyambila muchaka cha 2010 Malawi lakhala dziko limodzi muno mu Africa limene anthu akumwa mowa mwawuchidakwa chifukwa chopezeka mowa wamasachets kapena mutimabotolo tatingonotingono.koma zomvetsa chisoni ndichakuti anthu akumwalira nawo kwambili mowawu ngakhale boma likungopenya pano ndinthawi yoti boma lichitepo kanthu monga anzathu aku zambia ndi Tanzania anachitila.

  6. Ndiotchipa komaso ukupangisa achinyamata ambili kumwalila kulibwino kumwa mowa odula koma kukhala ndi good life ife tikudandaula kwambili ndipo tikulipepha boma chonde chende pelekani lamulo lolimba zisapezekeso muno malawi

  7. After frozzy mwati muletse zakumwa zamafumu chifukwa sanakukhuthuriren chithumba cha ma K2000… Super Midoli for life

  8. kma boma ilii aaa akulesa mowa wotchipa komanso wamkaka right choice?ine ndaipidwa nazo sopano,ndingozikhweza basi nanga chibuku ndikwanisa mene mukundioneramu

Comments are closed.