Agamulidwa zaka zitatu ndi theka kamba kolemba zabodza pa Facebook


Facebook Malawi

Inu nonse amene mumabwela pa Facebook ndi kulemba zabodza ndi zofuna kuipitsa mbiri ya ena, samalani. Anzanu akumangidwa nazo.

Facebook MalawiBwalo la majisitireti mu boma la Mchinji lagamula Bambo wina kuti akagwile ukaidi wa kalavula gaga kwa miyezi makumi anayi ndi mphambu ziwiri (42) atapezeka olakwa pa mlandu onyanzitsa mbiri ya munthu.

Malinga ndi malipoti,  a Pratozio Nkhoma a zaka 23 analemba nkhani ya bodza pa 10 February chaka chomwe chino cha 2017 pa tsamba lawo la Facebook.

Iwo ati analemba kuti a Lonzoe Defector Zimba apha anthu awiri ku nyumba kwawo powaombela ndi mfuti. Iwo anati anthuwo ndi mzika za ku Amereka. Izi anangolemba mofuna kuipitsa mbiri ya a Zimba.

A Zimba anakamang’ala ku Polisi ndipo Bambo Nkhoma anatsekeledwa. Atapita pa bwalo la Milandu, a Nkhoma anakana nkhaniyi koma umboni utabwela iwo anapezeka olakwa.

Podandaula asanapatsidwe chilango, iwo anati Mayi wawo akudwala ndiye awafewetsele chilango. Anaonjezelanso kuti mkazi wawo wabeleka kumene ndiye akufunika azikathandiza kusamala mwana. Iwo anaonjezelapo kuti amagwa khunyu.

Koma a bwalo ananena kuti mlandu umene anapalamula ndi ovuta ndipo anawagamula kuti akasewenze miyezi 42.

89 thoughts on “Agamulidwa zaka zitatu ndi theka kamba kolemba zabodza pa Facebook

  1. Aaaa uyu ndiye tobacco ndiye kuzaza kundendekotu koma musanapange matukutuku anuwo nkwizingeni chapotokola chimanga chapondaponda

  2. Aaaa uyu ndiye tobacco ndiye kuzaza kundendekotu koma musanapange matukutuku anuwo nkwizingeni chapotokola chimanga chapondaponda

  3. Inu amisala eti ndipo ndithesa ka M24hrs kanuko ngati mukufuna mubweretse ka M48hrs anthu akuba inu osayamba mwamanga amwene George Chaponda wo bwanji anthu opusa inu mitu yayikulu ngati wachaponda

  4. Getrude munthalika ,g chaponda, Petala wamunthalika wonsewa ndi mbava zoba chovula kkkk koma nde tikukunjoyani mafana

  5. Inuyo ndiye mukuzitenga 100%?Popeza 3/4 za nkhani zanu ndizabodza ndiye nanunso waku Maula to dz I kaki one ran limodzi ndi Hon.G.Chaponda pawaya paja.

  6. ogamula ndi omanga nose pa chakuti chamanu anthu akuba simuku wamanga anthu ongo tsuka nkamwa nkumawamanga miyezi yoseyi pa #pantumbo panu ndithu ntchito zaku boma zukukanikani demeti

  7. Inuso a Mozambique 24 mukuyenela kumangidwa pa mulandu ngati uwu,ndikumbuka bwino m’mbuyomu mumafalisa zaboza kuti plzdent peter munthalika wa mwalira pomwe amapuma umoyo wina ku America.

  8. Inu musakhale busy kumanga anthu onama. Chilango chamunthu onama wachisunga mwini mulengi us at I ofe tokhatokha zachamba!!! U min now ndende izidzadza ndi anthu Onama??? Chabwino, Zoti #Chaponda amugwira ndi chimulu chandrama mnyumba mwake zabooza??? Nanga zoti #Peterwamutharika pobwelera Ku USA anagwiritsira ntchito Moni mkono wamamzere mzaboza???? Zotinso anagwa kokazala maluwa mzaboza??? Muziganizatu wina akanena ndondomeko izo mwati wanama mpaka Ku cell kukhuta zakumaliro et

  9. always pa Malawi amene amapezeka ndi mulandu wawung’ono ndiamane
    amalandira
    chirango chokhwima ???.
    that’s
    why our government is fully of criminals.

  10. Wayika lamulo lopusa ngati limenelo nindani? Nanga ndi section yanji imeneyo? Tinene kuti pamalemba wabuye mulungu lamulo limenelo lilipo? Ngati ndichamba mwakoka chowawa mwene ndipo mwauponda ife amalawi tidazelela kunama,migedu,sanje nde wina aziti mumangidwa aaaaaaa bwela umange ine.

    1. True,,,, Malawi 24 will be arrested for Posting Lies… Where exact the Person was arrested???? Which Court convicted the Munthu???? Which Prison is the Munthu being kept?????

Comments are closed.

Discover more from Malawi 24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading