A President, mukhiyeni Chaponda – atero anthu a DPP

Advertisement
George Chaponda

Zafika pano mzawo wa a Chaponda atha kukhala a Peter Mutharika okha ndi oyimba uja Joseph Nkasa.

Anthu otsatila chipani cholamula cha Democratic Progressive (DPP) apempha mtsogoleri wa dziko lino amenenso ndi mtogoleri wawo a Peter Mutharika kuti amuvule unduna George Chaponda amene ndi nduna ya za malimidwe.

Malingana ndi chikalata chimene Malawi24 yaona chopita kwa mtsogoleri wa dziko lino kuchokera kwa anthu omukonda, iwo akupempha kuti a Mutharika achotse pa udindo a Chaponda.

“Ife ndi mzika zenizeni za DPP ndipo mukudziwa inu kuti sitinayambe takuponyanipo miyala,” alemba choncho mu chikalatamo kuuza a Mutharika.

“Akulu anu aja atatisiya, ife tinali nanu. Mayi Joyce Banda atakumangani, ife tinali nanu. Pa nthawi ya kampeni komanso ya zisankho, ifenso tinalipo. Ife timakonda chipanichi,” alemba chomwecho mu kalatamu kufuna kuonetsa kuti iwo ndi eni a chipani.

Anthuwo anenanso kuti ngakhale iwo ali okonda chipani motere, koma akhumudwa ndi mmene ikuyendera nkhani yokhudza nduna ya za ulimi a George Chaponda.

Iwo ati ali okwiya maka ndi kuti President Mutharika sakuchitapo kanthu pa ndunayi ngakhale bungwe lofufuza limene anakhazikitsa kuti lifufuze za kagulidwe ka chimanga ku Zambia linauza a Mutharika kuti a Chaponda akukhala ngati amafuna kuchita utambwali pogula chimanga.

“Bwana munalonjeza kuti muchitapo kanthu pa zimene bungwe limeneli lifufuze, apa labwela ndi zotsatila tikufuna muchitepo kanthu,” atelo mu kalatayo.

Iwo ati ngakhale akuvomeleza kuti Bambo Chaponda ndi msanamira wa chipanichi koma zafikapa madzi achita katondo ndipo palibe kuchitila mwina koma kumupitikitsa basi pa unduna.

Anthuwonso anena kuti a Chaponda akusokoneza zhipanichi chifukwa adani onse a chipani cha DPP ndi utosgoleri wa a Peter Mutharika akupezelapo mwayi onyoza kudzera mwa a Chaponda.

“Akutinyozetsatu mtaunimu Chapondayu. Adani athu a zipani zina, enanso obisalila mu mabungwe ndi ena onamizila kuti ndi atolankhani akupezelapo mwayi otinyoza,” atelo anthuwo.

Advertisement

71 Comments

  1. ine ine zaunyani ine ndatopa ndi okuba aphunzitsi aphunzira aja adikilira ntchito osatenga ayiko chelete what for baibulo linati mutailanji ndalama ndi zinthu zosadya agaluwo anawelenga koma

  2. A Joyce banda mulikuti azanu akumaliza ndalama munasiyako zinja bwerani musawawopeso pano mumanena zowona kuti cash get anayambitsa ndi aDpp Malawi uja wathadi

  3. Mkasa pamutu pake spamayenda amazfuna zobedwazo umphawi ngat ine unamkwana koma samazkumaniza.haaa!!! Changamuka iwe!!!!!

  4. Pamene zafika apa,timati zinthu zavuta.Khoswe wapasidwa aulura makoswe apazala.WHEN TWO THIEVES HAVE MEET IN THE SAME HOUSE STEALING,NEITHER OF THE ONE CAN SHOUT.

  5. Pitala Pitala..Chaponda Chapomda A Lomwe Alomwe No Piya Kodi Ndalama Sizinakukwane..Nde Mukuwona Ngati Ife Tipita Kuti ..Chimanga Waba,ndalama Waba, ..Vuto Siiwe Koma Pitala Amene Anakupasa Udindo…Shame On DPP GVr

  6. A Nkasa nawo azafela za eni ake dyela ndilo likumuvuta mkuluyi, aliyense wandale amafuna atamudyelapo… Samala pakamwa Nkasa tsiku lina uzaona ngati malodza…ngati nyimbo zinakuthela ndibwino uyambe ndakatulo

  7. Chaponda amangidwa tsopano ngati pamalawi tikuyesesa kuti tidalisidwe ndi Chauta yemwe analenga dzikoli.Peter Mutharika ngatidi akusata chilungamo chofumira kuchipani cha DPP ayenera kumanga chaponda.Aziwe kuti ndalama amaba chaponda zazuzitsa osauka komanso okalamba omwe alibe thandizo lililonse.

  8. Dont arrest da guy send him fo exile,atalowera chapa Zimbabwe zingatichitireko ubwino,do something Mr Preident,;show da europeans dat we r very serius,reform

  9. Ine sindikumva kuwawa ndipo moyo wanga uli m’malo chifukwa sindinavoterepo DPP tiyeni tonse tivomereze za ulamuliro wa Dpp mpaka 2024,kufuna oro osafuna 2019 boma kulamulanso Malawi mbali zonse.

  10. Mzake wina ndne !! Musatinamize apa ngati anthu onse mwawafunsa !! Apa ndye mwanama mwawanamiza anthu kuti mzake wacaponda ndi peter ndi mkasa ine mwandifunsa ? When posting dont generalise everything . Dont forget even jesus was the son of god but during his time its not all the pple who like him its not also all the pple who hate him. Ndye sianthu onse omwe amagwirizana ndizomwe mukuganiza . This r my ideas idont want citsilu camunthu cikunditukwana if u want to argue with me argue with acts not hate . Iwe robins banda idont want ur comment here .

  11. Eeeh koma chiChaponda chitha kuvala Bomba la timkenawo kuti chiphe gulu amwene eeh eeh!!! Kakaka osazitaya bwanji? Money chikazidyeladi ku Manda sure

  12. Joseph Nkasa ndi mfiti yodya maliro,Joyce Banda ndazinzake akutibela ndalama zamisonkho yathu ndi Nkasa yekha yemwe amati JB ngwabwino lero ndizi tonse tuti Chaponda asowe iye yekha akuti ayi a Chaponda alibe problem.

  13. Apatu ngati ali munthu wamaganizo yekha akuyenera kutula pansi udindo, posadikira kuti a president kapena amabungwe kumuuza kuti tulapansi udindowu. Uyu akufunika, apite kudera lake anthu akamukoke masaya mwina angamve galu ameneyu.

Comments are closed.