Agamulidwa miyezi isanu ndi umodzi (6) chifukwa chotukwana

Advertisement
Mangochi

Inu nonse okonda kutsuka mkamwa ndi mau aululu, samalani tsopano. Lamulo likuchitani tintini.

Bambo wina wa zaka makumi atatu ndi mphambu zisanu ndi imodzi (36) wagamulidwa ndi bwalo la majisitireti mu boma la Machinga kuti akagwile ukaidi wa kalavula gaga kwa miyezi isanu ndi umodzi (6)chifukwa chotukwana.

Malinga ndi malipoti a Polisi, bamboyu a Lloyd Wazili ati anatukwana chikunja Mayi wina.

Ati bamboyu anapeza mayiyu atayima pa malo ena. Iye ati analonjela Mayi uja ndi mawu opempha kuti akagone naye. Koma mayiyu anakana ndi kumupempha kuti achoke.

cuffsBambo Wazili mmalo moti achoke, ati anayamba kutukwana Mayi uja. Iwo anatchula ziwalo zobisika za Mayiyo ati chifukwa anakana kuti akagone nawo.

Bambo Wazili anagwilidwa ndi Anthu a zachitetezo a ku midzi amene anawauza a Polisi. A Polisi atabwela ndi kunjata Bambo Wazili, anachoka nawo chothawa ati chifukwa anzawo a Bambo Wazili amafuna kuthila makofi apolisiwo.

Ena mwa anzawo a Bambo otukwana mochititsa manyaziyu ati mpaka anatsatila ku Polisi komweko ati akamutulutse mzawo. Koma anagwidwa ndi kutsekeledwa.

Pa bwalo la Milandu, oweruza agamula a Wazili kuti akagwile kwa miyezi isanu ndi umodzi (6) kamba kotukwana pamene anzawo anayi amene anagwidwa akuti akatulutse a Wazili ku Polisi, awauza apeleke chindapusa.

Advertisement

116 Comments

  1. I dedent wont conthises mutharika all presedent in malawi is wrong is asalantilly now live for god is seve pleblems hi she fogtern cocision only god can jug pleblems thank you

  2. Ndatopa ndi kumva andale akuyankhula modzikudza nayenso mutharika akuyenjeza tinangobetsa mavoti athu njala ilimbwelekete ku malawi nanga tisankha ndani

  3. Eva Nthete, Ine Ndi Xabi Mauwo, Gomondah Gomondah Africa Skybuzzy, Matthew Paul Chibambo, Davie Kush Kuchilunda, Boy Nangwa, Santos Clever Bouy Kanada, Evans Nappyboy Kalumphalinga

  4. Ndie muyambe mwamanga nduna zonse zaboma + president coz ndi amene amaziyamba ndie mumati tisatukwane???? Tikukwana ngati zithu sizili bwino, kodi malamulo mungoonjezera onjezerabe bwanji? Aope ndani zimenezo. Lodi anthu ake ndi inu mukulemba bible part 2 aja ndinu eti? Mitu ngat mbuzi kuyambira yemwe anapanga lamuloro mpaka wa police amene angammange munthu otukwana. Mixm

  5. Nanga paja boma limadandaula ndi kuchepa kwa ndende za m’dziko muno. Nanga uku si ndiye kutha malo ko? Poti ndi ntchimobe mwina adzingolipitsa.

  6. Aphungu nosee akumalawi panyapanu
    chikhalilenosho kusukulu
    munapita zaka zankhani nkhani
    koma zelu mulibee kuyambila
    pita muthalikayo nyamakee
    aliyese amene ada4meleza zalamulolo
    bolo yabambo akee

  7. hahahaha koma adha…. komadi anthu ena amanyanya kutukwana, ofunika apolisi achonchi azipezekaso kuma bus stands…. komaso china anthu akumabaso chimangawa ofunika kuwamanga osamaona za mbali imodzi

  8. happy new months friends my name is Priscilla Mbangwe doctor abumen help me to cure my HIV/AIDS virus with an herbal medicine, am sharing this to the world to save some lives, believe me there is a cure, you can contact dr abumen on his email address [email protected] and you can also call or whatsapp his number which is {+2347085071418} please share to save lives.

  9. ZANTI, KULEKA KUMANGA WATHA KUBA NDALAMA M’BOMAWA PANO NDALAMA ZATHA WAYAMBA KUBA CHIMANGA. CHAKA CHINO TIKOLOLA CHATHU. NDIYE MUKATELO ADZIPANI DZAKUBADZI AONJEZELA DZIMANGA PASALU.

    1. Bweran kuno Kumangochi kuli anthu oziwa kumuvula munthu koma atavala muwamange ngati sazakuphulisani just try, Lamulo liposa mphamvu koma si Lamulo lake ili mmm am telling you start from the beginning again reform it, then I think it will work, but for now muona chiwelengero cha a police chikwera okufa pa Lamulo limenero.

  10. Zopusa zimenezo kutukwana nanga inu mumatukwana in english tipange nanu bwanj ine nde ndi tsiku lililonse kutukwana mubwere mudzandimange tione ngat simukadziika nokha ku prison mbuziiiiii za a2

  11. Kubweraku timva..aliyense oyenda ndawala amangidwe bwanji akuyenda ndawala akupita kut mwina akupita kokaba ameneyo kkkkkk Aphungu kusowa zokambirana atatopa ndikumwa tea wamkaka kuyamba kukambirana zopepera….zanziiiiiiii

    1. Hy #Manes usakhale ngat okhulupilika apa wamva..ukati vuto ndi inuyo simudziwa iweyo kuzivaka kudziwa zithu kwambiri..oky let me ask u…Miyezi yapitayo Aphungu amavomereza kut pakhale lamulo lovomereza kuchotsa mimba tsono ngat Amalora lamuro lomweso lili ntchimo kwambiri nde ukanene kutukwana ?? Mulandu ochotsa mimba ndi kutukwana zoyenera kukalowera kundende ndi ziti ?? osamangobakira zithu zofoila aunt #Manes mwanva ?? Am not saying kutukwana ndikwabwino ayi komano nkhalidwe ngat limeneli munthu amayenera kuzipanga control ekha not kumangidwayi..

    2. kkkk eti chemwali #Nancy nde wina aziti Boma lachita bwino pomumanga munthuyo aaaaa Kutukwana kumangokha kusowekera umunthu wako otukwanawe..ndikachiwanda koti ngakhale ku police ko azikatukwanabe kkkkkkk

  12. Otukwana ambiri ku Malawi ndi ambuli, osaka abwannoni, opanda mwambo, alibe chalichi, kuba basi, sanapite ku thezo. Ndiofunika kuwatumiza ku gule wankulu akawakunthe, abweleko alibe mano. Mungopangisa Malawi manyazi basi.

  13. Kuyambira apresdent mpakana nduna zonse za boma ndinu zitsiru coz simungamaononge nthawi yanu pokambirana nkhani zopusa ayi, inu mungamange munthu kamba kotukwana zoona? Bwanji simukummanga uyu wakubayu? Ndinu zitsiru eti

    1. nanu atakumangenipo apa.iwe ndi osauka ngati ine ogona ndinjala ngati ine ungamalalatile anthu opata ngati chaponda?uganize bwino blow.

  14. Kodi kutukwana ndi chani? Amalawi chatisowa chilungamo. Buku loyera, Mateyu, limatchula mwachindunji kuti, .. amene adzakwata… Mwambi umati, wakwata kwa mphezi… Koma wina kuti atchule zomwezo mukuti watukwana. Pachingerezi timatchula kuti penis, vagina, clitoris, testis. Why. Kapena munene kuti wamangidwa chifukwa chonyoza bwa? Once again, what is kutukwana?

    1. Just shows that you don’t know the difference between a name, abusive word and an insult. Kukwata, mbolo sikutukwana. Koma kumakhala kutukwana ngati pali kunyoza. Ukhonza kumutukwana munthu pogwilitsa ntchito mwendo, dzanja, mutu kapena thako. Komanso mau olaula sikutukwana, kumakhala kutukwana molingana ndi momwe wagwilitsira ntchito mauwo.

    2. I know more than what you know, and more than this. You may be the one full of emptiness. That’s why kumapetoko ndafunsa kuti, osati amumanga chifukwa chonyoza bwa? Unawerenga ndikumva funso limeneli? Kapena unangowerenga chabe? Kodi iwe sudamvepo munthu akunena kuti, uyu watukwana pamene munthuyo anangofotokoza potchula ziwalozo? I am against such misconceptions.You can follow the English version of the same story, where expressions like “insulting a woman” have been used. So, your argument doesn’t hold water at all.

    3. Iweyo usazembe apa uli against ndi nkhani yoti wina wamangidwa chifukwa chotukwana ukuona ngati ndizosatheka kumangidwa chifukwa chotukwana don’t try to be very clever walemba wekha zamveka bwino zomwe wanenazo osazipanga contradict.

    4. Critics and authors are able to express one idea using various devices. Some can use irony, others can use paradox and many more depending on their choice. They don’t explain the particular style they have used. In this way, it becomes the duty of the audience to interpret the way they want. So, whether you construe or misconstrue, is none of my business.

    1. Kukhwimisa malamulo pa anthu osowa pomwe yawo milandu ikumangogonera , what a crazy Malawi!! Am tired of MW.Guys ndipanga passport bas.

  15. Za ziiii ndende mukuzazikamo otukwana pamene okuba zaboma akunjoya muleka kumusekela uyu waba chimangayu. Zipangani

  16. Apite ku Nsanje kapena ku Ntcheu sati kutukwana ai koma kutchula chiwalo, kutsuka mkamwa. olo pomunyadila mnzako amatsuka mkamwa chimodzimodzi

Comments are closed.