Agamulidwa miyezi makumi anayi (40) kamba kogwila mtsikana bele

Advertisement

Palibenso zonyengelela amuna onse a chimasomaso chaka chino. Akapezeka akagwila ukaidi wa kalavula gaga.

Mkulu wina wa zaka makumi awiri ndi mphambu zisanu (25) wa mu boma la Machinga walamulidwa kukagwila ukaidi wa kalavula gaga kwa miyezi makumi anayi (40) ati kamba koti anagwila bele la msungwana wina.

Bwalo la Milandu la Majisitireti mu boma la Machinga linamva kuti pa 10 January chaka chomwe chino, a Gilbert John anapita pa sukulu ina ya sekondale mu bomalo.

Iwo atafika kumeneko anapeza mwana wa sukulu wa Fomu 4 wa zaka 19 akugwila chibalo.

Ati a John atafika anamugwila mtsikana uja bele kenako ndi kumugwilanso Mbina mochita chomukakamiza.

Iwo sanasiyile pamenepo komanso ati anaononga ndowa ziwiri pa sukulupo ati chifukwa a sukuluwo anali ndi ngongole yawo yokwana 3 sauzande Kwacha.

Izi zinapangitsa kuti a chitetezo aitanidwe pa sukulupo ndipo anagwila Bambo John.

Iwo atafika pa bwalo la Milandu anapezeka olakwa pa mlandu oononga katundu ndi mlandu ogwila munthu malo osayenela mwachipongwe.

Bambo John analira pa bwalo kupempha kuti asawapatse chilango chokhwima kamba koti aka kanali koyamba iwo kulakwila lamulo.

Koma oweruza Milandu anawagamula kuti akagwile ukaidi wa kalavula gaga kwa miyezi isanu ndi inayi (9) pa mlandu oononga katundu. Pa mlandu ogwila munthu malo osayenela, mwachipongwe anawagamula miyezi makumi anayi (40).

Advertisement

196 Comments

  1. Ngat ulamuliro ukuvuta uauzen atulepasi udindo Mr Peter chifukwa munthu sanagwile bere koma wagwila chovala chomwe chinali pa fupi nd bere zopusa et osamanga obachimanga bwanj February ikubwera njala mkat ndie mkumalimbana nd zogwilana mabere ulamuliro opoila

  2. Malawi wamabvuto. The one who stole government money are kept for less year but just to touch a woman breast costed someone that much in prison thats a nonsense judgement.

  3. Koma malawi akupita kuti uyu munthu kuba ndalama zankhaninkhani osamangidwa kapena kuti kuba ndalama za chimanga osamangidwa mpaka pano uyu wangogwiri bele sanalichosepo lili ndi mwini wake yemweyo koma mukumumanga kodi inu majaji umbuli kapena kusaganiza.

  4. Kodi belero anakaoda kut? Kodi iyeyo mamuna wake wagwila kangati? Kodi iyeyo sadzayamwitsa? Nanga mwana wake azakamumangitsa? Amalawi tizikhala ndi chisoni ndi azathu ukaidi ndiwowawa. Nanu akhothi kumaona ndi nkhani zake. Koma mumangoti ma section kodi munayamba mwawadziwitsa anthu asanalakwe. Koma malamulo timawadziwa ife Amalawi tikalakwa basi ma judge nonse wakumoto kwamulungu kulibe chanu anthu opondeleza inu. Mmalo molimbana ndi maizegate mukukalimbana ndi belegate Ngat munthuyo wachita kudula belero.

  5. Nice amuna anyanya kumatenga zamkabudula kuika poyera mkazi modzi osawakwana mau odyera amati akazi ngambiri yet mulungu analenga modzi kwa modzi nde masiku ano bwalo likugomera azimai adatipondereza kudakwana tipna tiina akutha osaugwira mtima

  6. Fucken chit ndi malamulo anuwo mwamva ndipo ndikanakhala ndi mfuti bwezi nditakuombelani chifukwa zikundiwawa mmasuleni munthuyo inu ma satanic

  7. Had it been it were a minister who did that no arrest would be done due to the fact the minister could not even go t appear before court due to his superiority, the ruling is illegal and biased, demolished all the courts and prisons if they are there for ordinary people

  8. akuluakuli tiyeni tizikhala ngati ndife mzika tiziziwa malamulo aziko lathu ndipo chigamulo chimenecho zili mmalamulo ndithu and ambiri timapalamula koma chifukwa amene timalakwilawo saikoka mkhaniyo timaona ngati ndizosalakwika chonde tiyeni tizigulako buku lija silodula kumawerengako pliz tizazizimuka wina titamugwira muchunu ulendo mpka kukasekeredwa zanga ziwiri mdithu

  9. AAAAAAAAAAAAAAAAAA azikazi WO NDE akumachita kutigunda dala malisani ndeife tiziopa kubwezera iwe wozamanga zakowe uzayelekeze kundi gunda ndizakuonesa zakuda ndukuza mukujaila malo mopanga zazelu kumalawiko mukumakhalakhala ndikumataya nthawi ndizaku nyelo tisiileni tokha tinaziyamba tokha timalizitsaso tokha zachamba ife ay

  10. Ambiri amagidwa chifuKwa salivala bo mafanawa azifufuza Kaye azamanga chibwenzi chake. Azibisanso maberewo. KungowayaniKa,mwana mamuna akadatani?? Koposa Kugwira. Flash ndi Kutchurch Komw?? Amangansotu Abusa!!!!!

  11. Ok any way. Akagwire ukaidiwo but y taking minor issues so serious though anthu ofunika ukaidi akungolambasha mwa mtendere? Such as. ……………..nda.

  12. Alephela muthu okupha alobino kumumanga 40 years ndiye muthu ongogwila bele pakachoncho inu mukunama ine ndyesakugwila bele ndiwonechichitike.

  13. Alephela muthu okupha alobino kumumanga 40 years ndiye muthu ongogwila bele pakachoncho inu mukunama ine ndyesakugwila bele ndiwonechichitike.

  14. .ndasiya kuwerenga nkhani za amenewa zimakhala zaboza mpaka kunamizira imfa munthu ife kuononga airtyme yathu kumalemba ma RIP

  15. No way, just touching no harm, kkkkkkkkk okey, what about these who store maize money the serious of fence, is he surviving.?

  16. Since you guys, Malawi24, have mistakes infused in your blood, do you really mean 40 years or 4 years. Murderers and housebreakers are given soft ones, why this man who only touched a body part? The judge involved is surely sarcastic.

  17. Eeeeeeh but this topic has atracted a lot of attention just like the woman herself atracted the guy.Anyway whatever everybody is saying here is making plenty of sense and I’m just speachless.Pena pake azimayiwa akumationjezadi kwabasi ndi mavalidwe awo amakonowa.Wuzaona mu American wapanga timalegeni ndicholinga choti atsikana adzivala akamalowa mu netball pitch kapena akamakaimba pa stage, iwo akumatigula timene tija nkumativala mtown ali pheeeee! Zosawakhuza iyayi.Nde kuli timadress tinatake akumati tima see through, akumakhala ngati kuti avala zadzitali bwinobwino koma wukawayang’ana amangokhala ngati kuti sanavalepo chinachilichonse.Zovala zoyenera kumavala mudzipinda mwaomo kuti amupange arouse mwamuna wawoyo iwo akumavala mtown nkumakakopa nazo wina aliyense.Nde pena mavenda tu amapangira dala, yimakhala ngati mbali yimodzi ya punishment.Akumationjeza anthuwaaaaa.They feel very much better when they are exposing their private parts.Expose them to your hasbands! Or if you are not yet married then expose them to your boyfriends if you think it is right to be doing these before getting married! But don’t just expose it anyhow to the public.Mukumationjeza kwabasi.

  18. ma court ali bizzy kulimbana ndizogwirana ma bere m’malo moti alimbane ndizama billion.achina chaponda akukuderelani kupita kunja pamene ali pa mirandu akudziwa kuti ma court akumalawi ndi opusa auchitsiru.ma court akumalawi lamulo siligwira tchito pa munthu wa dolla koma pa kafunyanya malawi sadzatheka.

  19. Nkhoti zogamula zake za ziiiiii!!! Mmalo mokhazikisa mamvalidwe abwino kwa azimayiwa akuchita kuwatokosa dala ndi zovala zowonesa tsonga zamatakowa koma kumalawiii! Eish!!

  20. Akuti ndinthawi yolimbikitsa azimayiwa kuyenda maliphyata, malichaje ,kapena kuti aziyenda maliseche kaya sakudziwa amakhotiwa azimayiwa akumapanga dala zimenezi kuti azitikopa ,muyambe mwazimitsa moto asanapyse osadikila katundu kupysa nkumazimitsa moto simukuthayi amakhothi pamenepa

  21. Osadabwa ayi Amalawi sitikondwera ndi munthu wopalamula mulandu waung’ono koma wakuba cashgate (Joice banda) kapena wakuba ndalama ya chimanga (George Chaponda) ndithu ndithu mukhale maso ndi mbava zimenezi sizidzamangidwa olo pang’ono. mmmm kodi kukhala tizitero?

  22. Eeeeeeeeeh uyo nde ampweteka.Dats too much.Sitikukana ndinjira yimodzi yotetezera atsikana komanso kuthetsa mtchitidwe wogwilira ana komabe 40 years is just too much for just touching a woman’s breast.Peaple are stealing billions of kwachas but they are just moving scort free koma mwamunayo kungomugwira bele mkazi basi 40 years? Ummmm, its too much.What about real raping? How many years do they give to a rapist?

    1. Ndiye anakakhala kuti wagwiriratu, basi unali moyo wake onse pa 40years-po. Umawerenga, ukuganiza chiyani? Kanundutu uyu, koma zachabe zilipano.

    2. Kkkkkkkkkkkkkkkkk koma eeeeeeee amalawi sitizatheka ndi zaka zitatu(3) ndi miyezi inayi(4) osati zaka 40 eeeeee kucita kumupotsa odya misokho ya amphawife.

  23. Ma court aku Malawi too corrupt plus kukondera zachamba basi.. Kungogwira bele ngati kuti anamuvula zachamba chosecho okuba ndalama ndi aja mumawapatsa 3 yrs fodya….

  24. Bele lokhalo mpaka munthu mumuzunze kundende miyezi 40?, bele lake lotani limenelo? tagwilatu mabele ife mwamva inu kukhothi uko, that’s a FUCKING judgement.

  25. What’s wrong with our Courts?. 3 years & 4 months in jail for only touching one’s breasts when another gets 4 or 5 years for raping an under aged & 7 years for rape & infecting with HIV.

  26. Pena akaziwa akumaonjeza akumayenda ali kale mbulanda ndiye ma swazi atani?kumangomangana zopusa basi january mwanya naye mwayamba kumangomang zilizonse

  27. Koma wakuba ma billion miyezi itatu kuwafusa kuti mwachitlanji izi akuti tikufuna kuti ndalama zomwe adabazi zidzikagwira ntchito

  28. Fool why u not tell them that they must stop moving naked kukaniza chilengedwe osamanga Chaponda bwanji wapha mtundu wa amalawi ndinjala

  29. munthuyu mwantani kodi?mesa anthuwo anafunana? mukumumangilanji?akhoti mumakondela. opalamula osauka simuchedwa kuwamanga.anthu akuba olemera mumangowasiya adziyenda momasuka osawamanga. uyuyu mumutulutse kundende mwamsanga kuti adzakwatilane ndi bwezi lakelo.

    1. its tru story war happened in machinga a man who touch a breast of secondary sxul student has been sentenced to 40 months in prison wth hard labour

  30. wakuba chimanga is just the same as killing nde mumutani ameneyu poti wogwira bele mwati 40 months. Umphawi umalowetsa anthu kundende koma olemera amangovakacha ali phee kuno mpaka ku Germany and back osamukwizinga. That’s justice pa Malawi.

  31. Wina adaba chimanga moti agogo anga akuvutika ndinjala kamba kaiye koma muli phe osapanga kathu mukugwira munthu woti wagwira bere ,osati

Comments are closed.