Pofika 2019 sipakhala mseu wa fumbi – atelo Mutharika

Advertisement
Peter Mutharika
Peter Mutharika
Peter Mutharika: Akuti misewu ya fumbi itha mdziko muno.

Ozapikisana ndi a Peter Mutharika mu chisankho cha 2019 azalimbe.

Mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika anena kuti iwo achita zodabwitsa ndi miseu ya dziko lino pofika mu chaka cha 2019.

Polankhuka pa msonkhano mu chigawo cha kumpoto kumene akukhalila pakali pano, a Mutharika ananena kuti Boma lawo layambapo kutukula dziko lino.

Iwo ananena kuti Boma lawo lili pakalikiliki okonza miseu ya dziko lino. Iwo ananena kuti chikonzelo chimene ayamba chokonza miseu chipitilila.

“Tikonza miseu yambili, ndipo tionetsetsa kuti pofika 2019 pasakhale mseu wa fumbi,”anatelo a Mutharika.

Iwo analonjeza kuti chitukuko ichi chipita Malawi yonse.

A Mutharika anatsimikizilanso anthu okhala mu chigawo cha kumpoto kuti Boma lawo litukula deralo.

Advertisement

5 Comments

  1. Kuyakhula ndikosamvuta koma kuchita ndiye komvuta. Ife kwathu ku Dedza timadandaulira msewo ochoka ku Lilongwe kupita ku Mayani ngati kukafika mpaka ku Msalima

  2. Thats good coming but the contractors need to be told to be constructing water ways if ever the already constracted roads have to stay longer otherwise come 2019 all these roads will require huge maintainance as the roads are prone to damage when there are no effective drainage system.

  3. Mmalo moti apange zoti atsitse mitengo ya chimanga ku admarc uko akamange misewu amalawi tikufa ndi njala ambuye mulowelelepo,,,ngongole zosabwezanso zili tho,,

Comments are closed.