Boma lipempha a Malawi kuti ayambe kukonda njuga


Boma lipempha a Malawi kuti ayambe kukonda njuga- Malawi24

A Malawi apemphedwa kukhala anthu olola ndi omasuka pa nkhani za njuga. Malinga ndi wamkulu wa mu unduna wa zamalonda, a Elsie Tembo, a Malawi sakuyenela kuona njuga ngati chinthu choipa.

A Tembo ananena izi mu mzinda wa Lilongwe pamene amatsegulila malo ochitilapo njuga otchedwa Marina Casino.

“Anthu akuyenela kumvetsa kuti njuga si chinthu choipa, chinthu chilichonse chili ndi ubwino ndi kuipa kwake. Nayo njuga ili motelo,” anatelo a Tembo.

Iwo anaonjezelanso kunenapo kuti anthu akamasewela njuga akuyenela kukhala omvetsetsa ndi oleza mtima.

“Anthu azidziwa kuti awa ndi masewela, utha kupambana kapena kugonja.”

204 thoughts on “Boma lipempha a Malawi kuti ayambe kukonda njuga

  1. Gambling is in many ways but we dont know. Insurance, medical scheme, game betting,(indirect gambling). Look at NICO, MASM, TNM-kulosera tnm league games.

  2. Malawi nde ameneyo kulesa frozy kuloleza mowa,akuti odwala achuluka mzipatala ndichfukwa chomwa frozy,imfa zuuchulukaz akuyambixa ndi frozy,akut ma driver akamwa akumalezera mchifukwa chake ngoz zikuchuluka.Akut amuna tokhatokha tizikwatirana,akazixo okhaokha,akuti mimba titha kumatenga nkumazichotsa momwe tikufunira,lero akuti tizipanga njuga ndipo tilemera khasu tipachike.what a nation?malawi.no wonder mvula ikungogwa yoononga mphezi ndi izi zikutikanthazi.uchimo wachuluka.Mmera ku admarc akugulixa modula ngat ndi gold,katundu wazinthu akungokwera koma malipiro ndiomwe aja.Zafikapa nyasaland tizimutanthauzira mchichewa kut dera lonyasa muzochitika osat nyanjaland.

  3. Zomwe kale anthu timaziopa kut nditchimo pamaso pa Mulungu pano kumufusa munthu umva malamulo amalawi akulora kutero..Gambling,,Abortion,,Amuna kapena akazi kukwatilana okhaokha,Sex out side mariage..kuvala mosazilemekeza makamaka atsikana pano unva zili mu fashion komaso malamulo zonvetsa chisoni..zithu zoti anthu simungakhale carbinet ndikumakambirana coz ndizochita kuonetseratu kut siziloledwa kwa Mulungu kutero koma umva akut aphungu anyumba yamalamuro akukambirana mfundo yoti pakhale chilorezo choyenda njuga mwaufulu aaaaa koma zoona imeneyo ikhale nkhani yokakambirana mavuto onse ali kumalawi ndikumakaonjezeraso mfundo zina zobweretsa minyama pamoyo wa aanthu.. yes malamulo anuwo akulora kutero komano nanga malamulo a Mulungu akuloraso kutero ?? nanga chabwino ndichani kusiya zomwe Mulungu akuletsa ndikutsatira zomwe malamulo apadziko akulora ?? afta 2yrs ndikukutsimikizirani muzanva akut kwamene akufuna ku joiner Satanic malamuloso akulora kutero bolani dziko lathuli likhale ndichithandizo chokwanira so bad… God forgive us..

  4. Amene walamulayo aziwapatsaso athu ndalama yoyendela njugayo cz athu akusowa chakudya angakapange njuga yachani aaaaa sheme

Comments are closed.

Discover more from Malawi24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading