Boma lipempha a Malawi kuti ayambe kukonda njuga

Advertisement

A Malawi apemphedwa kukhala anthu olola ndi omasuka pa nkhani za njuga. Malinga ndi wamkulu wa mu unduna wa zamalonda, a Elsie Tembo, a Malawi sakuyenela kuona njuga ngati chinthu choipa.

A Tembo ananena izi mu mzinda wa Lilongwe pamene amatsegulila malo ochitilapo njuga otchedwa Marina Casino.

“Anthu akuyenela kumvetsa kuti njuga si chinthu choipa, chinthu chilichonse chili ndi ubwino ndi kuipa kwake. Nayo njuga ili motelo,” anatelo a Tembo.

Iwo anaonjezelanso kunenapo kuti anthu akamasewela njuga akuyenela kukhala omvetsetsa ndi oleza mtima.

“Anthu azidziwa kuti awa ndi masewela, utha kupambana kapena kugonja.”

Advertisement

204 Comments

  1. Mbuli za anthudi zimenezieti? Kukalimbikisa khalidwe lachabe koma abale dziko lathu likunka kt makamaka! Last week amakambilana at nkhani zololeza abortion koma zooona? Lelo akubwelesaso ina akt boma lanyong’ola kt amalawi aziyenda juga, our country is damage by stupid leaders

  2. Mhhhh!!! Kukadakhala kuti kuli mwayi, osinthanitsa kutenga Wa moyo munthu nkukamuika kumanda nkukatenga wakufa kuti akhale ndimoyo chinali bola kukasiya Pitarayu nkukatenga Bigu chifukwa bolani ada ajawo ankakana za chifinezi ,osati INJA uyu/ ( Galu uyu )

  3. Kkkkkkkkk ndinali ndisansione nkhaniyi Mwati Boma kupempha Amalawi kuti ayambe kukonda njuga? kkkkkk Mukamamva kuti uchitsilu wa Anthu akulu akulu ndiumeneu basi kufatsa nkufatsa amvekele Amalawi azikonda njuga asaaaaaaa!!! mukauze akwanu zopusazo mwamva kuganiza uku nde bolanso Mwana anganize zanzerutu Mbuzi za wathu

  4. Gambling is in many ways but we dont know. Insurance, medical scheme, game betting,(indirect gambling). Look at NICO, MASM, TNM-kulosera tnm league games.

  5. Malawi nde ameneyo kulesa frozy kuloleza mowa,akuti odwala achuluka mzipatala ndichfukwa chomwa frozy,imfa zuuchulukaz akuyambixa ndi frozy,akut ma driver akamwa akumalezera mchifukwa chake ngoz zikuchuluka.Akut amuna tokhatokha tizikwatirana,akazixo okhaokha,akuti mimba titha kumatenga nkumazichotsa momwe tikufunira,lero akuti tizipanga njuga ndipo tilemera khasu tipachike.what a nation?malawi.no wonder mvula ikungogwa yoononga mphezi ndi izi zikutikanthazi.uchimo wachuluka.Mmera ku admarc akugulixa modula ngat ndi gold,katundu wazinthu akungokwera koma malipiro ndiomwe aja.Zafikapa nyasaland tizimutanthauzira mchichewa kut dera lonyasa muzochitika osat nyanjaland.

  6. Zomwe kale anthu timaziopa kut nditchimo pamaso pa Mulungu pano kumufusa munthu umva malamulo amalawi akulora kutero..Gambling,,Abortion,,Amuna kapena akazi kukwatilana okhaokha,Sex out side mariage..kuvala mosazilemekeza makamaka atsikana pano unva zili mu fashion komaso malamulo zonvetsa chisoni..zithu zoti anthu simungakhale carbinet ndikumakambirana coz ndizochita kuonetseratu kut siziloledwa kwa Mulungu kutero koma umva akut aphungu anyumba yamalamuro akukambirana mfundo yoti pakhale chilorezo choyenda njuga mwaufulu aaaaa koma zoona imeneyo ikhale nkhani yokakambirana mavuto onse ali kumalawi ndikumakaonjezeraso mfundo zina zobweretsa minyama pamoyo wa aanthu.. yes malamulo anuwo akulora kutero komano nanga malamulo a Mulungu akuloraso kutero ?? nanga chabwino ndichani kusiya zomwe Mulungu akuletsa ndikutsatira zomwe malamulo apadziko akulora ?? afta 2yrs ndikukutsimikizirani muzanva akut kwamene akufuna ku joiner Satanic malamuloso akulora kutero bolani dziko lathuli likhale ndichithandizo chokwanira so bad… God forgive us..

  7. Amene walamulayo aziwapatsaso athu ndalama yoyendela njugayo cz athu akusowa chakudya angakapange njuga yachani aaaaa sheme

  8. Munthu asewera njunga ku Cassino ngati Salary ukulephera kukwanitsa kugula zofunika gi ve better salaries muone ngati sitizipita kukapanga Poker

  9. Kamano inu amene mukupanga mfundo zopanda phiduzi mukuganiza bwanji? Jugayo iwapanga anthu kuvutika kuposela mene akuvutikikamu wina azibesa ndalama yogulila chakudya

  10. zautsiru basi…umbavatu….umenewo….koma mau a Mulungu mumawatsatadi…kapena inu mwaposter zakumtima kwanu..pofuna kuona ma comment ochuluka….mukuzitenga kuti zimenezi….am vry sorry…

  11. though tli osauk we all obey GOD so ths is a god fealing country hw come the pple in it might indudge thm selves in that sin,,shame malaw

  12. Zizindikiro zonse zamu bible zosonyeza kutha kwadziko Malawi yamalizamo. Abale ndi alongo mulekelanji kulapa machimo anu?

  13. Kumeneko ndiye kulimbikitsa mchitidwe wawumbava apolice gwirani ntchito yanu pamenepa m’malawi muno mulibe lamulo losewera njuga aboma mwatani kodi ngati mwasowa zokamba ingokhalani

  14. Pantumbo pake ameneyo kwa december ino npaka december ya chaka chamawa mumakambilana fundo zopoila bwanji kumipandoko pankholo panu nose ku phatikiza ndinduna zose zamu dziko lino mukufuna muti onongele ana mudziko muno zoyambitsa chisokonezo muno ayi muzikapangila kwina manyi amenewo

  15. Za ziiii zikuonesa poyelayela kuti president wathu saziwa kuyipa kwa njuga mupaka lelo iyi ndiye mbuzi yamunthu akuvomeleza kuti anthu akuba achuluke mudziko lathu

  16. Mavuto. Angokula. Basi. Mwalephera. Lolani. Mulungu. Alamulire. . taona. Anthu. Akukhala. Pa. Rent. Cz. Analandidwa. Nyumba. Ndi. Anrhu. Ajuga. Anzawo. Ubwino. Uli. Pati. Apa?

  17. Kenako adzalipeleka dzikoli mmanja mwa zambia,mozambique ndi tanzania kuti aligawane . Chifukwano uku ndiye kusowa kolowela . Let us wait and see.

  18. Uchtsiru umenewo! ndi zmene mukumakambirana ku parliament mukakhuta? shame on you! what malawians should benefit from gambling? a china adzachotse parliament yawo dzitsirudzi dzikusowa kosewerera dzkakhuta shooter!

    1. That awkward moment when you try to look wise by commenting something… Only to realise you just made a fool of yourself because your comment was total bullcrap……lmfao

    2. Aaaaa guys,, bac muli busy kupanga reply ma comment anxanu monyoxa chonchi?? Kodi mesa aliyense akupereka maganixo ake? Musapange xa ena mbuxi inu. Aliyese atokote xake mwamva?

  19. Sapemphela Tembo akadakhakuti Bible amalidziwa akadadziwa kuti njuga ndiyoletsedwa Bible ndipo inatembeleledwa anthawi imene amkapanga mayele zovala za yesu

  20. Njuga ndi uchimo-chifukwa zinthu izi zimachita involve kuba komanso kupha.Ndiye boma povomereza avomereza zonsezo GOD PLZ ABIDE WITH LAND OF MALAWI

  21. Asowatu malonda opanga tsopano ndiye tingolowa Ku njunga kkkkkk Malawi alibe chochita atsogoleli nawoso mutu yangosonekera mabvuto achuluka.Dziko ngati lavuta tiyeni tiwapatse mwayi azungu athu aja tidawathangitsa kuti mwina tingawoneko kuwala ngati mmene azathu akujoyela mmayiko awo pali mzungu sipanama ife anthu akuda aaaaa mbola kudzikundikila too much

  22. Hili ni shirika lisilo la kiserikali (NGO) lenye Makao makuu yake nchini UFILIPINO na sasa limefungua ofisi zake nchini Tanzania. Shirika linalilojihusisha na utoaji misaada kwa:
    (1) Watoto yatima
    (2) Wajane
    (3) Watu wenye changamoto mbalimbali za kiuchumi
    Hivyo shirika kwa sasa linatafuta mabalozi/ wawakilishi popote pale nchini Tanzania ambao watalipwa na shirika kwa mshahara mzuri. Kwa maelezo zaidi tembelea.
    OFFICE: kivulini, Mlimani city Dar es salaam.
    WEBSITE: http://www.helpinghandsinternational.biz
    CONTACT: +255 677 898 941, +255 655 216 136, +255 767 216 136 or
    +255 621 892634.
    USITUME MESEJI HAZITOJIBIWA.
    Wote mnakaribishwa HELPING HANDS INTERNATIONAL.
    HELP US TO HELP OTHERS.

    http://www.helpinghandsinternational.biz

  23. Apeter abalalika akutiso aliyese osuta fodya azita chamba opezeka akusuta Embasy azimangidwa koma ku Malawi eeeesh!!!!!

  24. eshiii kom inu mbunzi zina eti kupanda manyazi ndikusowa mzimu kumati “kayendani njuga”what is njuga?aonereni akhakhatha,atombolombo agulukunyinda simudzathekaso ananchidwe inu

  25. Wachiwona ndani mmene azimayi ankadyetsera ndalama yokagula chimanga ku admarc muja mukufuna ayambirenso? Mwachitika nasi uli tanyinu? Imwi mutchaya cha mbwenu isi titchayengi, hinya ukavu ngwidu ndatchayapu cha.

  26. Ooooh NO this is a really corupt goernment, DPP umbava wanu mkufuna ukhale palipose eti? njuga zimayambisa kuba kumeneko nde kupepela koma pitala ndi boma lake awa nde akanikilathu kuyendesa dziko eish

  27. Kkkkkk njunga yake mukuona ngati yachisawawa eti kkkk siyomwe mukuganizayo ndi lotto anthu a mwayi amatha kuyalura mphasa ndianthu kkkkk

  28. Is that ur plan guys its better to lieve if ur tired to work Gvmnt ndizimene mukumakambilana kumeneko mwasowa zochita eti mbuli za anthu inu dzika lalowa satanic baSi

  29. Chakula apa ndi usatana zowona zake ndizakuti aliyese wandale ndi satana coz malamulo omwe amatipatsa amakhala ochokera kupasi kwanyanja mkumatulukila kumtunda ndiye sizachilendo dziko kuti lithe pakufunika zizizndikilo zomwe mwini wake namalenga analosera zichitike ndiye izizi ndizochepA zenizeni zikubwera koma tsoka ndiiyemwe akukwanilitsa zizindikilo za kutha kwadziko ndiye alinditsoka kenako atipatsa ufulu oyendano maliseche azimayife

  30. Koma mulungu ngati adalanga kapena kukwiila Sodom ndi gomolla zifukwa zoti mulungu atikwiile zakwana ndipo tikapanda ku sintha mulankhulide,zochitazathu mulungu achita nafe

  31. Ndiye ose ogulisa chamba,okuba ndimahule apasidwe ufulu atuluseso andende ose popesa zifukwa zomwe anawamangila pano siuchimoso

  32. kkkkkkkkkkkkkkk.atsogoleri akumalawi oganiza ngati galu ot atasaza nthawi yomweyo ndikumadya MASAZI AKE. kkkkkkkkkkk WHICH BENEFITY CAN WE GET TO GAMBLING WE US ANATION?KKKKKKKK. ndathedwa zeru. inu cheni cheni chomwe akufuna anthu awa ndichani?

  33. Gambling is, has been, and will always be there just that there hasn’t been more promoters of responsible gambling. It’s a game actually but it is a sin on religious grounds. Nonetheless, people play that game responsibly even irresponsibly.

    1. You are right mr Timothy,only other pple dont knw the meaning of “gambling” Come to South Africa,pple make millions of rands–lotto,casinoes!

  34. Eeeeeeeh MALAWI kwachaa, wasanduka kwadaaa, ambuye musalolere kt ana anu tiyende muchionongeko ,tichotseleni ziwanda zomwe zikufuna kuononga dzikori ,kutenga tchito zakumidima kubweletsa poyerah achite manyanzi dyerekezi ameneyi muonetseleni ukulu wanu ndipo ndi pemphero langa ndi pembedzelo kt oipao achite manyazi..AMEN

  35. Malawi wapitadi basi mpaka pamenapa,mmalo molimbikira kupemphera kuti Mulungu atichotsere mavuto tili naowa,ndimmene mukwaudza anthu kuti adzichimwabe,kapena malemba simunawaone

    1. unkolo ,,,muti kulimbikila kupephela kuti asiye ,mmmmmh i think its good but if somene knows its better just to leave that bad thing,,,panopa zomangoyang’anana basi.

    2. unkolo ,,,muti kulimbikila kupephela kuti asiye ,mmmmmh i think its good but if somene knows its better just to leave that bad thing,,,panopa zomangoyang’anana basi.

    3. kuno kumalawi zinthu zikutipeza mochedwa nkuona chilichose timaona ngati dziko likutha kkkk,,,,kumangoti ambuye alowelelepo zilizose,,,,,,,kkkkkkkk tamaendani abale osamangoti machimo zilizose,,,,

  36. Ngati nzeru zachepa chifukwa cha kukula tipaseni ife dzikoli tiyendatsa bwino ndithu njuga ndiyolesedwa angakha mma holy books,inu muli ku njuga panopa?musasokoneze mitundu ya anthu ngati mwasochela ,sokelani nokha amene pemphani kwa Chauta nzeru musanayankhula kuopa kuti mungaonongeke komanso kuonongesa anthu ena

  37. kodi Malawi ukupita kut mmmm ma last days timva zinthu koma iwe Tembo mutu wako umagwira bwino koma ndipo ndiwe opusa wava ufuna kut umbanda ukule et

  38. Ndiye tikati atsogoleri athu ndi amene akuononga dzikoli tikunama? amalawi tiyeni tipemphere kwambiri chifukwa oyenera kumanga Malawi ndio akumasula Aaaaaa! Shame Malawi!

Comments are closed.