Boma lipempha a Malawi kuti ayambe kukonda njuga


Boma lipempha a Malawi kuti ayambe kukonda njuga- Malawi24

A Malawi apemphedwa kukhala anthu olola ndi omasuka pa nkhani za njuga. Malinga ndi wamkulu wa mu unduna wa zamalonda, a Elsie Tembo, a Malawi sakuyenela kuona njuga ngati chinthu choipa.

A Tembo ananena izi mu mzinda wa Lilongwe pamene amatsegulila malo ochitilapo njuga otchedwa Marina Casino.

“Anthu akuyenela kumvetsa kuti njuga si chinthu choipa, chinthu chilichonse chili ndi ubwino ndi kuipa kwake. Nayo njuga ili motelo,” anatelo a Tembo.

Iwo anaonjezelanso kunenapo kuti anthu akamasewela njuga akuyenela kukhala omvetsetsa ndi oleza mtima.

“Anthu azidziwa kuti awa ndi masewela, utha kupambana kapena kugonja.”

Sponsored

204 thoughts on “Boma lipempha a Malawi kuti ayambe kukonda njuga

  1. Mbuli za anthudi zimenezieti? Kukalimbikisa khalidwe lachabe koma abale dziko lathu likunka kt makamaka! Last week amakambilana at nkhani zololeza abortion koma zooona? Lelo akubwelesaso ina akt boma lanyong’ola kt amalawi aziyenda juga, our country is damage by stupid leaders

  2. Mhhhh!!! Kukadakhala kuti kuli mwayi, osinthanitsa kutenga Wa moyo munthu nkukamuika kumanda nkukatenga wakufa kuti akhale ndimoyo chinali bola kukasiya Pitarayu nkukatenga Bigu chifukwa bolani ada ajawo ankakana za chifinezi ,osati INJA uyu/ ( Galu uyu )

  3. Kkkkkkkkk ndinali ndisansione nkhaniyi Mwati Boma kupempha Amalawi kuti ayambe kukonda njuga? kkkkkk Mukamamva kuti uchitsilu wa Anthu akulu akulu ndiumeneu basi kufatsa nkufatsa amvekele Amalawi azikonda njuga asaaaaaaa!!! mukauze akwanu zopusazo mwamva kuganiza uku nde bolanso Mwana anganize zanzerutu Mbuzi za wathu

Comments are closed.

Discover more from Malawi24

Subscribe now to keep reading and get access to the full archive.

Continue reading