Mtsogoleri wakale wa dziko lino a Bakili Muluzi wati ndiokhumudwa ndi imfa ya mkhala kale pa ndale a Gwanda Chakwamba.
A Chakwamba amwalira dzulo pa 24 Okutobala masana pachipatala cha Blantyre Adventist mu mzinda omwewo wa Blantyre atadwala kwakanthawi kochepa.
Sabata latha nyuzipepala ino inakupasilani nkhani kukudziwitsani zakudwala kwa malemuwa omwe amadwala nthenda ya mtima ndipo anagonekedwa pachipatalapo mpaka dzulo pomwe atisiya.

Poyankhulapo pa zaimfayi, mtsogoleri wakale wadziko lino a Muluzi omweso anagwirapo ntchito ndi a Chakwamba, ati ndiokhumudwa kwambiri ndiimfayi.
Muluzi wati adzawakumbukila malemuwa ngati munthu olimbikira komaso osabwelera mmbuyo akafuna kupanga zinthu ndiposo opanda mantha.
“Ndinauzidwa kuti Gwanda wamwalira. Ndimadziwa zoti anali kuchipatala ku Blantyre koma ndimaganiza kuti akhala bwino ndipo nditava za imfa yawo ndamva chisoni komaso ndakhumudwa kwambiri.
Chisoni chikubwera chifukwa ndinawadziwa a Chakwamba zambirimbiri zapitazo, enafe tili anyamata tikuyamba kumene ndale. Tinagwilira ntchito limodzi mu mchipani cha MCP komaso cha UDF ndipo ndikufuna ndipepese kwambiri kumtundu wa a Malawi kamba ka imfayi” wadandaula Muluzi.
Mogwirizana ndi a Muluzi, mtsogoleri wakale wa chipani cha MCP a John Tembo, nawoso ati imfa ya Chakwamba yawakhudza kwambiri.
A Tembo ati ngakhale ndi a Chakwamba nthawi zina samagwirizana, koma malemuwa anali olimbikira pa ndale ndiposo mumchipani komaso amadziwa chomwe amapanga ngati namandwa pa ndale.
A Gwanda Chakwamba amwalira ali Ndizaka 82 ndipo anabadwa pa 4 Epulo 1934 ndipo wasiya mkazi, ana atatu, zidzukulu zitatu komaso zidzukulu tudzi zinayi.
109 thoughts on “Bakili, Tembo akhumudwa ndi imfa ya Chakwamba”
Comments are closed.

BAIBULO LINATI TIDZAFA NDITHU INU MUKUDANDAULA CHANI. MUNTHUYONSO ANALIBE CHAKUDYA/ POGONA INU MUNALI KUTI
Pepani ofedwa amen
Guyz Ziwani Ichi Mu2 Amafuni Akamwalira Bakili Sanayenera Kudandaula, Ndikupanda Zeru Kwawo Mumva Kt Athandiza Maliro Kusiya Mu2 Ali Kuchipatala.
He is a bg fool Malawi ali pa moto lero coz of him Tabela ma vote ndikulowesa alomwe ake aku dzuza Malawi lerowa.
Ziwani ndale zindikila andale .ndiamozi awa timadana ndife osatila
Dziko la malawi ngati lidasauka ndi chifukwa cha iwe bakili, udagulitsa ma company, udapha anthu ofunikira, udayambitsa kugulitsa ziwalo za anthu, ndiye lero ungave chisoni ndi ifa imodzi.