Sindipepesa – atero a Ndau pokhudzana ndi matenda a Mutharika

Advertisement
President Peter Mutharika
Peter Mutharika
Peter Mutharika -Adati adali ndi nyamakazi.

Nduna yoona zofalitsa nkhani imenenso ili mneneri wa boma a Malison Ndau auza atolankhani ndi mabungwe ena amene amafuna kuti iwo apepese ati kamba koti ananena bodza pa za umoyo wa mtsogoleri wa dziko lino kuti iwo sangapepese.

Mabungwe ena omwe si a boma anakhala akuyimba milandu a Ndau kuti apepese pouza mtundu wa a Malawi kuti a Peter Mutharika ali ndi moyo wangwiro ku Amereka. Koma a Mutharika atabwela ananena kuti io nyamakazi inawasautsa ku Amereka kutanthauza kuti amadwala.

Koma poyankhulapo pa nkhaniyi, a Ndau amene amanenela boma ndipo anaopseza kuti anjata anthu amene anali kutchukitsa kuti a Mutharika anali akudwala anayankhula kuti sangapepese.

Malison Ndau
Malison Ndau: Sindingapepese.

“Ine sindinaname iyayi, ine ndimanenela boma ndipo ndinanena zimene a boma amadziwa. Ku boma timadziwa kuti a Mutharika ali wangwiro ndipo sitinaname konse,” anatero a Ndau.

“Choyenela kudziwa ndi choti a Mutharika ali ndi moyo wawo umene pena umayenda opanda a ku boma kudziwa, nkhani ya matenda iyi sitinauzidwe poti sanali matenda enieni,” anaonjezelapo a Ndau.

A mabungwe anapsela mtima a Ndau ati chifukwa ananena kuti Mutharika ndi wangwiro koma mwini wache ananena za nyamakazi. Koma ngakhale zili choncho, a Mutharika ananena kuti nyamakazi imene inawavuta sinali vuto kwenikweni.

“Kanali chabe ka nyamakazi kamene kanavuta, ndipo ine ndikudziwa palibe munthu anafapo ndi nyamakazi kupatula mwina ku Zodiak,” anatelo a Mutharika polankhula ndi atolankhani lachisanu.

A Mutharika anakhala ku dziko la Amereka misonkhano imene anapitila itatha. Iwo anaonjezela kukhala kwawo ndi masabata awiri. Izi zinapangitsa anthu kuyamba kufalitsa nkhani.

Zinatchukitsidwa kuti a Mutharika akudwala. Iwo atabwela mdziko muno anaonjezela mphekesela izi pokanika kugwilitsa ntchito mkono wawo ma dzanja la manja.

Advertisement

94 Comments

  1. kukhala m’malawi gyz sikophweka m’malo momawona zamagetsi tili bzy nd za munthu m’modzi modzi gyz think twice zichite kutha mwezi nkhani zosatukula dzikoziiii ???????????

  2. Sometymc i blame myslf y i was born in teritory of malawi bcoz of same issues like this akuti apepese kaya akufuna apepese chani kaya , kukakamira zinthu xopanda phindu basi God forbid n mercy on u Amen

  3. Atumbuka akut matenda bisan nyifwa tizamulira tose nde ngat a president ankadwala kumene anali palibeso zopepetsa apa stupid well done Mr Ndau

  4. Ukukana kupepesa ngati ndani iweo? koma ukutidziwa bwino bwino kuti ndife ayani?uona polekera come 2019 khala choncho usapepese!

    1. Palibe chomwe ndingapange atapepesa,koma nkhani ndiyakuti ali kumeneko kutumikira ife a malawi,nde asamabise chinachilichonse chizikhala poyera tonsefe ndife amodzi nde that guy akuyenera kapepesa ku mtundu wa a malawi chifukwa chosanena zithu zoona.

  5. Dzimenedzo ndiye mdzauchitsilu,kodi nkulu wako uja alikuti? Ngati adapita iyeyo nangaiwe ndiye ndani?kodi ukuganidzakuti ungadziombole ndi chuma chako?chibwana chimenecho,mulungu wakuchilitsani kuti mube komaliza akubwela adzakutengeni,ngati nthawi yakwana palibe kupsatila,payele payele basi,kapumeni mwaba mokwanila,

    1. Iwe ukunena mozitama ngati suzafa? uyambe wafunsa anthu akwanu kuti abale ako ena ali kuti before kulankhula moputsa chomcho wamva #James nkhumba yamunthu iwe. Ndipo uyambe kufa ndi iweyo before APM

    2. Iwe Nkanda choyamba ndikuti panyopako, ngati umalodza anthu ndikwanukomweko mfiti iwe. Ukuwona ngati kuti iye atamwalira angavutike maikidwe, ameneyu dziko lonse kuziwa kusiyana ndi mphawi ngati iwe odya zotoleza ngati nkhumba. Uwona, ufa ndi cholera akubwera posachedwapa tione ngati anthu angamve zoti fisi winawake wamwalira. Usazayambilenso kulankhula mopusa, panyopako basi ndapita ndikukagona uyetse kuzanditambira ndikutchola pomwepo.

  6. Mwina akuziona ngati chitsulo. Palibe kupepesa PETER ndi odwara basi, olo zibagera sangalimbe nazo. Wa miyoyo nine amaliliranso kupepetsedwa utsilu eti?, mwaiwara kuti manda aja akutidikira a moyofe. Utsogoleri muzawasiyira ena ku dziko kuno akulamulira iwe{peter} uzapita ulibe kali konse.

    1. Anthu a kugona mu mdima wopanda magetsi anayamba wapepesa who is he to people If he is failure to deliver even little thing to Malawian citizen shame on you

  7. Ukadwala ikhala nkhaniso.Mulungu amaona sungabitse chinachilichonse.sungabitse matenda pamene ukudwala.Tithokoze Poti Chauta Anatipatsa Moyo.Anthufe timatenga moyo ngati wathu mwini wake alipo.moyo 2 sagula ngakhale ukhale ndindalama zochuluka bwanj sungagule moyo.Heart is a precious

  8. Mutharika ananena pa press conference kuti if there is any1 to blame is him,not mgeme or Ndau.ma journalist aku Malawi simumamva olo pang’ ono.APM is the 1 to apologize not ndau or mgeme,koma mukumuopa that’s y mukulimbana ndi mgeme.

  9. Honourable wa analeledwa pachilolo kwao,ziwani izi kamba ukamzampeza ali mumtengo alipo anamukwezamo,tikutsisani 2019 madolo alero ndimakape amawa.

    1. Angati tinawina tili ku opposition nanjino pano tili m’boma kale ndiye 2019,tingalephere kulamulilaso sumadziwa ndale iwe ukatenge social ngati umaphumzila

    2. Iweyo umadziwa chani?u youth mulalo wakowo komko pano ayi,kuzolowera kuyimba ng’oma kumitsokhano yandale eti? Malo mogwira ntchito otukuka ndi Honourable inu mkumatuwa ngati nsomba yabakayao.

  10. choncho malawi can it be developed,let look kodi munthu wanjala nkutukula dziko? amalawi amavutika popeza money koma akaipeza kugula chimanga(food) but zikumapezekazo kuti magetsi kulibe. ndiye tiyeni tidzikambirana nkhani ngati za magetsi kuti titukule dziko lanthu osati zosathandizazo.lets change malawi

  11. Bwanji sanapepese atanena kuti anthu azidya ,mbewa makoswe ngumbi udzudzu nkhanu ndi dziewala.nkumaseka kkkk ndi joke ndiye ndau amatha joke nayeso

    1. Sitikuopa 2019 dilu ndi chimanga tizalamulilaso ngati tinatenga boma till ku opposition ndiye tikakanike kuwina 2019 manyazi mulibe

  12. Kupepesa dzi chani azi patse ulemu amuthalikawo asadzi tukwanitse koda kale ngati kuno sindikufuna ndi tsuke nkamwa prz kodi n.yeyo ndi chitsulo akati adzi uza anthu kuti apepese kuntundu wa amalawi muthalikayo ngati wadzipopa ango ima po ela ndikuuza anthu kuti ali bwino osati nkhani zama #buzi akunenazo fuck muthalika upange zaineyo bwanji ineso ndimodzi amene ndima uza anthu bolani mr ndau siama uza anthu kuti iweyo ukudwala koma ine nde ndima uza anthu kuti iweyo wa mwalila nde azungu kwamerika akupanga prastic sajaly akufuna amu veke waku banja la amuthalika iweyo ndi fake piter muthalika kana ngati ndiku nama nyamakaz ya chani vuto la atsogoleli okwatila pokha pokha mukapatsidwa npando ndi choncho banja ukalilowa uta kula kale zima telo ndinkani makolo amango wasiya ana akamapanga chibwezi kuti a chotsane uviligo amakana zodwala dwalazo kaya zako izo adah

  13. Apology not needed, Muntharika and the rest of his crews knws kuti ndi zooona. Aliyense amadwala and adzadwala, chokanira ndi chiyani. Yamikani Chauta kuti wakupatsani moyo, tsiku la wina aliyense likakwana basi ndi ulendo basi. Kumvomereza ndi kwabwino abale.

  14. Funso ndi loti kodi abwanao sakudwala full stop? Apepese ngati sakudwala koma ngati akudwala palibe chopepesa. Nokha mukuona nkonowo tu kuti muthuyu ngodwala tasiani zopusazo tu.

  15. anakulera mopusa,uzautaya mchele 2019 mumat munakhalitsa kuamericako 4 the benefit of malawians palibe ndimfundo yogwila ntima pa presidential press tiyembekeza kut mutiuza mfundo zenizen!zachison kwambiri childish gvt

  16. unaleredwa mopusa,uzautaya mchele 2019 mumat munakhalitsa kuamericako 4 the benefit of malawians palibe ndimfundo yogwila ntima pa presidential press tiyembekeza kut mutiuza mfundo zenizen!zachison kwambiri childish gvt

  17. A Muthari nd mstongoleri wadzi iwo akalamakhula asamakhale akupanga point zala kuti koma ZBS AI! And a Ndau musaiwale kuti izakwananso thawi inja imene mudzawafune anthu kuti akuikeninso pamene mulipo. Mtsongoleri Is not God kuti iye sangadwale AI kaya inali nyamakazi kaya zinali zina ife sizikutikhuza. Pano zibisani zonso nafe tizabisa mthawiyo muzatifuna

Comments are closed.