Nonse okonda kutukwana chenjerani: zaka zisanu kundende mukapezeka mukutukwana

Advertisement
Maula prison

Palibe kutsuka mkamwa mwachikunja, mukatero mukapezeka kujere ndi kugwira ya kalavula gaga.

Mkulu wina ku Ntchisi amulamula kukakhala ku ndende kwa zaka zisanu pa chifukwa chotukwana mayi wake ndi kutchula ziwalo zobisika.

Maula prison
Wa ku Maula kamba kotukwana

Malingana ndi bwalo lalin’gono la mu boma la Ntchisi, a Pilirani Banda omwe ndi a zaka 27, akuyenera kukakhala kundende chifukwa anatukwana koopsa mayi wawo.

Bwaloli linamva kuti pa 2 August chaka chomwe chino, a Banda anapsetsana mtima ndi mayi wawo. Anasinthana Chichewa chosakhala bwino ndipo a Banda anakwiya kwambiri ndi kuyamba kutukwana mayi wawo chikunja, kutchula ziwalo zobisika za mayi wawo ndi kuwaopseza kuti awapweteka ku malo obisikawo.

A Banda atafunsidwa za mlandu uwu iwo anauvomela.

Woweluza milandu pa bwaloli, Yohane Nkhata, sanachedwe koma kuwagamula a Banda kuti apite ku ndende akagwile ukaidi wa kalavula gaga kwa zaka zisanu.

A Banda anagamulidwa chotere pa chifukwa chogwilitsa mau otukwana amene anali ndi cholinga chofuna kupsetsa mtima munthu ndi kumupangitsa kuti apalamule mlandu.

A Malawi ambiri saona cholakwika ndi kutukwana maka achinyamata a mu sukulu za ukachenjede amene akakwera basi zawo amatulutsa mitu pa windo ndi kumatukwana anthu. Mwina posachedwa nawo amangidwa.

Advertisement

4 Comments

  1. a Malawi 24 musiye kumalemba nkhani mu chiyankhulo cha english, muzilemba chichewa chomwechi. izi zakhala chonchi chifukwa mumavutika kulemba kwambiri, nthawi zonse nkhani yonse imangokhala ndi zolakwika

  2. Iyi ndi nkhani yabwino kwambiri ku mtundu wa Malawi ofunika malamulo amenewa azigwira ntchito ngakhale malo omwera mowa ndi malo achisangalaro aliwonse chifukwa mchitidwe onukhawu ukuchulukira ena amalankhula mawu olawula ngakhale mu mini bus “nthawi ina ndinatukwanidwapo ndi driver ndi conducter wa minibus chifukwa chakuti tinakangana pankhani ya mtengo umene ndinawona kuti unali okwera kwambili ati chifukwa patsikuli ma transport amavuta ndiye a ma minibus anapezerapo mwayi obera anthu chonde a Police tithandizeni pogwira ndikumanga anthu onse opanda ulemu komanso odzetsa chisokonezo mdziko muno popanda kuyang’ana nkhope kapena chipani chi ochimwayo ndatha ine wanu Kantukodooka Buluku lasato sasita

  3. iyeyo ndiwachamba
    zoona anganatukwane amai ake zoona
    yalakwa imeneyo

  4. Muthu kutukwana mayi ake kaya Bambi ake ofunika kupha straight.alibe mzimu ameneyu,zasiyana kuyamba ndiwapadela,opo pokha mphunzo silichedwa ayi not your parents no

Comments are closed.