Musaletse mowa; a Malawi akwiya ndi malingaliro ofuna kuletsa mowa

Advertisement
Beer

Gulu la a Malawi okonda chakumwa lakwiya koopsa ndi malingaliro omwe mabungwe ena kaunena oti pakufunika malamulo oletsa a Malawi kumwa mowa pa nyengo zina.

Pothilira ndemanga pa nkhani yomwe ife a Malawi24 tinalemba yoti bungwe lina lomwe si la boma la Drug Fight Malawi likupempha boma kuti lichite machawi kuvomeleza ndondomeko yoona za kamwede kamowa yomwe pachingelezi ikutchedwa National Alcohol Policy, a Malawi anasonyeza kuti ndi osakondwa kuti anthu ena akufuna pakhale malamulo a padera oona za kamwedwe ka mowa.

“Linotu si dziko la chipembedzo chinachake, musayese ndi la Chislamu kapena Chikhristu. Tisiyeni tizipyoza mowa wathu,” wina analemba monyangala.

Beer
Mowa usaletsedwe ku Malawi.

“Aaah mukufuna mudziko muno mukhale anthu ochepatu chifukwa tonse a mowa tisamukila ku mayiko amene kuli mowa,” wina anaopseza motelo.

Wina popowa kulankhula zambiri, anangonena kuti: “zopusa zimenezo!”

Koma mkulu wa bungwe la Drug Fight Malawi amene akutsogolera mabungwe amene akufuna kuti pakhale malamulo okhwima pakamwedwe ka mowa, a Nelson Zakeyu ananena kuti cholinga chawo ndi chakuti boma liteteze anthu ku mowa, makamaka a chichepere.

“Boma likuyenela kuvomeleza ndondomeko zatsopano izi zomwe zikukhudzana ndi kamwede, kagulitsidwe ndi kapezekedwe ka mowa. Cholinga chake ndi choti titeteze anthu ku mowa, makamaka achinyamata amene akuonongedwa ndi mowa,” anatero a Zakeyu.

Koma mawu awo sikuti akondweletsa a Malawi amene akuoneka kuti amakonda chokumwa chawo moopsa.

Advertisement

272 Comments

  1. Ndalama zomwera mowa zimakhala zake.munthu akhoza kumwa mowa nthawi yimene akufuna as long as drinking joints are open

  2. kkk mw moto kuti buuuu. musamwe mowa koma iye akumwa mowa odula. kkkkk ife tizimwa kachasu emweyo. nakhanso aligulu lamowa. mw watani

  3. Kumowa kuli phindu lanji?ena aumati atamwa atagona akumalota akukukuta chinangwa apa akudyelela pamphasa kkkkkkkk zopusa basi

  4. Mukulimbana ndi mowa zaziii mmalo moti mulipemphe BOMA kuti lipemphe kumaiko akunja macampany ochuluka kuti ulova uchepe mungokakamila kulima heee koma amalawife.

  5. Ndiye matsire amachita madzulo?Leave beer alone! Wachitukuko ndi wachitukuko.Inu simuwaona ma sober ali pa bawo mmawa,umphawi uli thoo

  6. tathanani ndi mavuto monga #kamlepo_kaluwa wagwa pakati pathupa kkkkk mowa tizamwa mpaka kale kkkkkkk mongamso kubanda mpaka kale kkkk

  7. I support the move. Ena amapezeka atalezera as early as 9:00am chonsecho nkazi ndi ana agona ndi njala panyumba. Alteast pakhale malire ma hours omwera mowa. Lets borrow a leaf from Tanzania. Nthawi yoti mzikalima mumapezeka kumowa, njala ikabwera u blame government chonsecho inuyo simulima.

  8. Maphunziro ndiye kuti chani, kodi tosefe tikaphunzira tnchito zake zilikuti sibola kumwa mowa. Muli makampani angati muno simukuona anthu ali ku joni akuthawa chani? Sikuti akuthawa mowa koma umphawi zikakukanikani mukunamizila mowa anyapala inu kkkkkkkkk….!

  9. Just raise the tax and make it more expensive. …change the package no packing in small packs…..then that way beer consumption can be reduced. …

  10. omwe ayambisawo ndi masoba en Kodi macompanies omwe amafula mowawu ali ndi fans yochuluka bwanji yomwe imagwira ntchito? Ndiye akaseka macompanies amenewa fans imagwira tchitoyi mutani nayo? sikuchulukisa kuba ukufuna? fuck yu all omwe mwabweresa fundo iyi chifukwa simukuganixira ovutika Koma kuzikunfikira chuma.

  11. Posted in: Corruption. 4 Comments

    We as Malawians, we ask President Peter Mutharika to send on force leave the seven cashgate concerned cabinet ministers. Recently Malawi Electoral Commission has suspended its top bosses to pave way for justice and this must apply to civil service and cabinet ministers or else Mutharika must resign as well.

    On 29th August 2016, George Chaponda minister of Agriculture and Irrigation was chased and stoned in Mulanje by angry citizens. People started Stoning him and the function was disrupted and Chaponda had to run into his vehicle to save his dear life. People of Mulanje have rejected their own son in his homeland as they consider him to be a betrayer and a cashgate thief. Let us learn hold hands and learn from our brothers and sisters in Mulanje for unity and say ENOUGH IS ENOUGH.

    These people are political thugs, they are politically corrupt to finish every little resource Malawi ever had.

    Political corruption is the use of powers by government officials for illegitimate private gain. This corruption include bribery, extortion, nepotism, influence of murder, robbery of public funds etc. This government of DPP facilitate criminal enterprise such as drug trafficking, money laundering, and misuse of government power for other purposes, such as repression of political opponents and general police brutality.

    Above all DPP and Mutharika are influencing bad politics, threat to elections process e.g (Mchinji elections undermined), bribing MPs to pass bills, bribing Judges and authorities in defending them over corruption (Cashgate), favouring them e,g(20 May 2014 Elections), diverting funds for food, health, development and delaying salaries for civil servants.

    In politics, corruption undermines democracy and good governance . Corruption in elections and in the legislature reduces accountability and distorts representation in policy making; corruption in the judiciary compromises the rule of law; and corruption in public administration results in the inefficient provision of services http://www.dzukamalawi.wordpress.com

  12. Zandivesa chisoni athu ambili omwe a kukana ku lesa mowa omwe amatiso opa mulungu mulungu salola mowa salola chiwelewele ndiye mmakhala pasogolo ziko lopa mulungu ikasowa mvula tipephe mulungu zokwatilana amuna ai inu athu a mulungu tichepese mowa ai mowa okha musiye chimo ndi chimo mowa chigololo zonse ndi chimo

  13. Mpofunika kuti boma liyike malamulo makamaka pa nthawi yomwe ingathandize kuti anthu azikhala ndi nthawi yokwanira yogwira ntchito malo mongokhala malo omwera mowa nthawi ndi nthawi,umbanda womwe wakula kwambiri Ku Malawi nchifukwa choti anthu ambiri sagwira ntchito chomwe Iwo amalingalira ndi kuba akatero akamwere mowa .Koma pa kakhala malamulo zidzathandiza kuti anthu azigwira ntchito chifukwa malo azisangalalo akhala atatsekedwa taganizirani mayiko omwe tayandikana nawo monga Tanzania Ali ndi nthàwi yomwe anthu amakagwira ntchito akaweruka ndipamene amapita malo azisangalalo (boma liyenera kuyika nthawi yomwe anthu angamamwere mowa osati nthawi ili yonse)

  14. I don’t drink beer and recommend drunkenness,but what i have observed is that our country,malawi,is now becoming more satanic .Why people don’t mention about kicking out homesexuality [mathanyula] and other wickedest sins from our country that claims to be a God -fearing nation?

  15. ah kma mabungw enjw bas mukukhal bzy nd zamoa muktan kuthan kae nd njal kvta kwamages maz ah ndie mwapez kt chophwek nd bawa thanan kae nd mfans omwe ikupha malubnoh

  16. Kunena zoona timamwa mowa pofuna chisangalalo Panthawi Imeneyo ndiye Munthu wakonza kuti umwe mowa masana kuti kukada uzipita nde akuletse Kuti Koma Kude Kaye kapena kuti umwe lachiwiri aziti ai koma Friday Ufulu wanga uli pati? Ku Malawi Ukapolo Sunathe.Ma Bungwe Osowa Zochita. Iyi yokha Simupeza Nayo Donation, Funani Ina.

  17. I cannot Support that move of stopping the Beer because iam here iam from the profits of beer so those who are depending on it muwapatsa zochita? Inunso Mwaiwala zoti mwaphunzira Kuchokera Mukachaso?Malamulo Adziko Lino Amakomera Ndani Kodi?Mukachita bwino musaononge ntajiwa a nzanu. Mutisamale!!!

  18. Akalesa Bawa ndyeno tizipanga chain enafe ndi maswazi akazi sititenga timatenga Bawa asalese ayi apeze chiganizo China koma

  19. Tikasiya mowa mutipasa azikazi anu kapena ana anu kt tiwakwatile?nanga okonda fanta muwatani?azinjoya okha?osakalimbana kae ndi zombe ku lower shire bwanj,maguja anu mwanva!

  20. Iyeyu sanamve kuti Nowa analedzera after kutuluka mchombo muja munthu wa Mulungu amene ndiye inu mukukamba chani apa mowa ndi wakale kale inu musanabadwe mudzausiyanso kambani zina apa

  21. enafe kuchipatala ana tiuza kutiuza kuti tikadzangosia mowa tidzafa mutitha ndiza bwanji, mmene mumamwela mowa ma mp ma loya pa bwandilo mudzasia kubwela?

  22. Ngati mwalephela kulamula dzikoli pasani anzani. Anthu anayamba kumwa mowa inu musanabadwe ndiye mkumati tiletse mowa za ziiii

  23. Nde bwenzi kamuzu atatsegulira company ya carlsberg za ziii popeza akulu akulu ali m’bomamu timamwa nawonso sitingawatchule amapapilanso kwambiri, a Bakili anatsitsanso mtengo wa mowa musaiwale izi nde ziti

  24. Mukamva kuti kupusa ndiye kumeneku.mukaletse mowa kuti wakulakwirani chani?osalimbana ndiokupha alubino bwanji? Yeserani muone timatcha maliseche muonanso……

  25. Koma Koran ndi Bible zilimo mwati zimenezo. …tiyeni tigwire ntchito apa kuzolowera ulesi basi. ..mowa mowa ndekuti chani? ZOPUSA! !!

  26. mowa letsani!!! nose amene mukut mowa ndinu vitsiru simudziwa matendawa amafala kwambili kumowa? y mahule saima pa stage ya bus kusaka amuna? amapita kumowa coz amadziwa ndikumene kuli vitsilu vizawo. mowa ndigwero laumphawi mudzaziona tintchito/biznz mukudyadilato tikadzatha. mowa aletse bas, kaya tizimwa mobisa~ usat uzingopezeka palipose ngat frozzy ayii!!

  27. Mowa sulepheretsa chitukuko ndipo ambili olemera ndiwomwe akumwa mowa mukamati mowa umasawukitsa inuyo zangokuvutani nkhani simowa kopusa kwanu mumati zikukuvutani kamba ka mowa

  28. ndalama zimene amamwela mowa sizikukhuzani amabungwe inu,zingoadyerani azungu kunjako,muli ndintchito zambiri zoti mupange mzikomuno.Mowa anayambisa ndi makolo athu kale ndie inu lelo ndi lelo mulese,tapangani kae za albino amene miyo yao ili pa ciopsezo osati zamowazanuzo

  29. anthu amenewo asatenge malamulo akunyumba kwao awaike mdziko muno, bola #chanba nzoveka ndiye atilese kumwa #mowa afuna tizitani tiyambe #ufiti, muuzane mwanamizana mowa palibe uyo angaleke , ndibwerezeso mowa sitileka kumwa

  30. nawoso ndzidakwaa aletsa bwanji ndziko lit analesa mowa komw samamwa mpaka lero!! bungwelo kuliso zidakwa heavy lesan tiwone osamalimban cashgate ku hillko kupusa etiih kukamwa woyankhulawe

  31. im nt a beer bt galu aliyese ali nd tsiku lake!! chtukuko akucta kma kulesa mowa dis can’t b gd way to solve the prblem we hv nawoso aleke kudyera masuku pamwamb pa anthu osawuka nd makape a mabungwee

  32. Muyambe mwamanga Kaye azibambo onse osamwa mowa chifukwa iiii nduaumbombo kwambiri amathawa ana kukamwa tea mu tea room wamkaka ndi sikono.

  33. Inuuu asiyeni aMalawi nawo azizipepesa.Abale maiku enawa antu angoledzela daily koma angopitilizabe kulemela. Mowa siugaletse chitukuko chadziko. Ngati lililosauka ndilosauka basi. Pezani njila ina yoti antu achite kuchepesa upawi. Asiyeni antu osaukawo nawo azizi pepesako

  34. Kkkkkk drug imadula hevy koma anthu amaipezabe nde mowa oti wa polisiso amamwa lawyer amamwa ka ndi Mr President ndunena pano ma grass awiri amwa kale nde mwati mwaletsa? Hahaha

  35. Maganizo abwino asiye ndikupanga ndithu coz anthu ambiri aonongeka ndimowa maka ana achichepere kwa ine ndikuti muyesese asiyilethu ndipanga vyimowavo paja ndikaviona ndimakhala ngati ndaona bb la agalu

  36. Mulesa bwanji Vinyo kt asamamwedwe,bwanj osaletsa opangawo kt asamapange ?,,,,Komanso ngat mumatipasa ndalama zokamwera mowazo Tisiya

  37. Zikuoneka kuti anthu tonse tikukambapo zamowa pamalo ano, tingapanga mpikisano ulankhula kosatherapo ngati titakumana pamodzi (debate). Zidakwa zikuoneka kufika potukwana KKKKKKKKKKK

  38. Paja chambanso ndi cholesedwa koma timasutabe nde you think mowawo tingakanike kumwa?? hahahhà mukunama amabungwe ife simungatiletse chimene tkufuna coz dolla ndi yathu! i rest my case

  39. Apa pokha amabungwe mukutidelera,pankhani yamowa yokhai pafunika referendum timve maganizo aaMalawi.Chifukwa mowa ndi source of income kwaanthu Ena.Ndiye mukaletsa zizangoonjezera umbava ndi umbanda,chitetezo chovunda kale.

  40. Hello my name is john I want to give a testimony about my HIV virus that was cured by a great spell caster. Since last 4years I have being a HIV AID patient. I never think I will live long again and am so grateful to Dr sule who help me cured my HIV AIDS last 3 weeks. I was in a great pain so I told one of my best friends; he told me that there is a great spell caster that can cure my VIRUS. I asked him if he had his contact, he gave me his contactl, I contacted him he talked to me and he perform the necessary things and sent it to me through corrier delivery company and deliverd to me at my place and he told me that after two weeks I should go for a test. Which I did, when the doctor told me that am now a HIV negative I couldn’t believe myself I went to see another doctor the result was still the same, I was human on planet earth, so I emailed him and thanked him. Please if you are having a similar problem please visit him/contact him via whatsapp +2348162447651

  41. Ndakaika ngati zingatheke unless mutawapezela chakumwa china chokhala ngati mowa komaso choledzeletsa otherwise mutiuza ndinu zochita

  42. aaaaaaaaaa koma zitheka malo mot mulimbane ndi anthu amene akupha alubino mufuna muletse mowa mayazi kulibwino ngat zakunyasani osangosamuka bwanji ndi

  43. Mukupanga masewera eti mulese mowa zausilu eeeee ndye pavuta mukufuna tizigona sober tizilota njoka amabungwe pliz mulese ana anu ndzizukulu zanu ndapota nanu

  44. Inu mukuzinamiza kuti Mmalawi ndiye odziwa kumwa mowa? Boza pitsno pa Zambia ndi Kenya mukawone anthu okumwa mowa. Ngati Malawi ndi dzilo LA anthu okonda mowa bwanji samawinako chokho cha ziko lomwe lamwa mowa kuposa maiko aku pajatu ndi kumwera limene imakonda kuwina ndi Zambia kapena Kenya
    Asiyeni anthu asangalare ndi mowa palibe chifukwa
    Inu thanani ndi anthu skins

  45. My name is Bogadi kgaogano and this a testimony of how i became HIV NEGATIVE, i have been suffering from HIV for the past four years, i have spend a lot of money finding cure for HIV/AIDS until i found this true man who cured me completely with his powerful herbal medicine, i have tried different means to get this virus out of my body, all the possible ways i tried did not work out for me, i came across doctor olumo through some amazing testimonies concerning how Dr Olumo has cured different people from various kind of sickness like HERPES,HIV/AIDS, CANCER, with the help of his powerful Herbal Medicine, so i was encourage and i contacted Dr Olumo i told him about my Sickness, He told me not to worry that he was going to prepare some Herbal Medicine for me, after some time in communication with Dr Olumo he finally prepared for me the herbal medicine which he sent to me through courier service and he also gave me prescriptions on how to use it, after taking the Herbal medicine for some days, i went for test to confirm and the result was totally negative ,i went for test again in a different hospital still the same negative , Today i am fit and healthy to live life again, I am so happy for the good work of Dr Olumo in my life, if you are having a simillar problem kindly email HIM on { [email protected]} OR CONTACT HIM WITH HIS NUMBER OR CHAT WITH HIM ON (WHATSAPP) (+2348138956767) together we can live an HIV free life.

  46. Mabungwe ena ndi zisende zomwa madzi ometera, zidepete zenizeni, zisilu zotheratu. Pa mavuto onsewa omwe a malawi akukumana nawo mwapangapo chani? Kuphedwa kwa albino, mathanyula, njala mwapangapo chani. Ndiye lero mumvekere kuti mukufuna kuthesa mowa umene loti ndi nowa amapapira. Olo mutandithira doom kamwa sindingasiye kunyopola bawa.

    1. Read the post before making full comment. Sakukamba zakuletsa ku mowa. Akukamba za nthawi yomwera mowa. Anthu ena amapezeka atalezera as early as 9:00am. Nanga ntchito za chitukuko akagwira nthawi yanji? Nanga chakudya cha ana ndi nkazi panyumba akafuna ndani? Imagine mwamuna waledzera 8:00am koma nkazi ndi ana agona pa line ku admarc for 2days fighting for 5kgs maize! Kumaganiza polemba ma comment ena. Borrow a leaf from Tanzania. Analetsa kumwa mowa morning hours and ku Tanzania kulibe njala…wamva m’bale??

  47. Ndalama zomwe akuba andalewa misonkho yake yambiri imachoka kumowa nde mukuona ngati angalore kuti mowa authese…cash gate nde mowao

  48. Asowa zokambilana ama bungwe amenewa akalmbane ndmowa zilnd phindu lanj cifukwa ena mwaio asyasya mowa nde bas atpatse phuma enafe?timwabe mikala bongo

  49. zidayamba masiku awo….. Padziko pali anthu opatulika, inu ndindani kut mukaletse mowa? Pamanu…… Mwxiiiiiii…….

  50. Zoletsa mowa-zo nde zausiru..! Ngat mwakalamba mungomwalira basiii..!! Zoletsa mowazo nde zachamba kwambrii…!!

  51. Maganizo ochepetsa kumwa mowa apangidwe. Amene akwiya ndi zimenezo ndi adani a chitukuko cha Malawi. Dziko silingatukuke ngati muchuluka zidakwa, a ulesi, a bawo, ntchuwa ndi a miseche, atambwali a ndeu, akuba, a katangale ndi ziphuphu. Zinthuzi zimaendera limodzi. Tiyeni tigwirane manja tiletse ndi kuchepetsa maka mowa. Mowa ndi wabwino pa nthawi yake. Osati kuchoka m’mawa mpaka m’mawa wa tsiku linali. Hmmmmmmmm…. Zoona????

    1. We are talking about Malawi. If you have nothing to say just keep quite. It looks you are big hearted and always fighting oeople including your own wife. Change your mindset!

    2. Kuletsa its really shows how primitive malawian we are sizikufanana ndi kupedza nzeru yopezera chuma cha dziko, i can agree atati mowa wa spirit okha but not mowa onse zachamba eti

    3. Iwe #Madimbo?,,,,,mukutichitisa manyazi mwamva eti,,,kodi muzazindikila bwanji kalowedwe kandalama mziko mwanu? Pamenepo ainiwakenu mukuti mwaganiza mwanzeru pamenepo uku ndiye kusowa chochita amalawi uku,,kutha nzelu,,

    4. ine ndimamwa and i live a happy life, ana anga amapita ku school ya bwino so whats wrong with drinking, am a cross boarder business man and i pay tax,hahaha ngati simumwa zanu zimenezo,,

    5. Ukunamatu iwe kuyaka,ku blaka ndizmene tmakonda.iwe ndmfit et?mowa muletse,koma mudzindphera mtundu wanga ma albino sichoncho?galu

  52. Mowa kwa omwe amamwa ulibe tchito.ubwino wamowa ndikuchotsa munthu pa umunthu wako,kukusupula kumaso,pena utaumwa opanda kudyela umafa. phindu kumowa lili kuogulitsa bcoz it get a proft

  53. ngat mungaletse mowa ndi bwino kut Marijuana mulolezeso tizisuta mwaufulu… Nanga monga kwa munthu wamuna azitan. Kumowa timapewako zambiri.. Mukundiuza kut kulesa mowa aliyese azakwanitsa kulipira ma college mene mwakwezawo.?

  54. Koma guys kumakhala serious eti. Malawi ali kale ndi mavuto ambirimbiri. Ena mwa iwo ndi awa; njala, kusowa kwa mankhwala, umphawi, #Kamlepo_Kaluwa, kusowa kwa ntchito, kusowa kwa madzi ndi magetsi angozima. Pongofuna kutchulapo zina. Ndye amabungwe nkhani ya chakumwa ichi cha mtengo wampesa sinkhani ayi. Tiyeni tithane kaye ndi mavuto eni eni monga kamlepo kaluwa yemwe watigwela pakati pathu. Zikomo. #wodandaula

  55. AMabungweadali ndi maganizo abwino kma tikati tione kwathu kuno padakhala kuti Employment siyimavuta ndikadavomerezana nao kuti Mowa uzimwedwa kuyambira 17:00 PM kma tikatiso pabwere lamulo limeneli Umbavaso ukula chifukwa tchito kwathu kuno ndiyosowa.

  56. kuletsa kumwa mowa sizingathe,koma kukoza bwino masiku omwela mowa zitha kutheka.monga kumwa mowa friday,surtuday,sonday bola cifukwa malawi waonongela cifukwa cha mowa.

  57. Kodi amagula ndani? Kodi boma linagulapo mowa kupatsa anthu? Even we can have drought have u ever heard kuti kumowa kwalowa drought? Letsani katangale wanuyo. Kodi ufulu uja wapita kuti? I thought everyone has a right of choice. Mwasowa chochita. Drought yalowa mubrain momwe.

  58. TISEKE KWAKANTHAWI KOCHEPA
    Nkazi wina amafuna kumuyesa
    mamuna
    wake…. Analemba ka note
    nkukasiya pa bed
    iye nkumbisala pasi pa bedi…
    kanalembedwa motele:” Ndanganiza zopita kaye
    kwathu
    kukapuma kwa miyezi iwiri,
    Musale bwino!”
    Mamuna uja atawona kapepala
    kaja analemba mawu ena kuseli kwake. Kenako anatenga
    phone yake……(mamuna pa phone)
    “honey
    Ndikubwera pompano
    Ndizakutenge,
    pumbwa uja wapita kwawo ati mpaka miyezi iwiri
    Ndiye tinjoyatu!” mamuna uja
    atasitha zovala ananyamuka
    kumapita.
    Nkazi anatuluka pansi pa bedi paja
    misozi ukuvumba m’maso
    ngati mvula. Anatenga kapepala kaja
    kuti
    awone zimene mamuna uja
    analemba kuseli
    kwake……. Kunalembedwa kuti: “STOP PLAYING
    SILLY GAMES HONEY, MIYENDO
    YAKO
    IKUONEKERA KUNSI KWA
    BEDIKO. TELEKA TEA
    NDIKUKAGULA ZOMWELA

  59. Alese mowa kma umathanyula azilola? Akuziwa kt even mugabe game imeneyo sangailore? Mbuzi imeneyo.

    Sitinayambe kumwa pochita kumenyera ufulu ngat zqumathanyula zqwozo

  60. Muone athu Aku malawi ambili ndi osauka ndikupanda zeru mumangokhalila Kachaso ma presedent ose a kumalawi anali zidakwa mutukuka bwanji azanu amagwira tchito kuti atukuke inu magwira kuti mukabwe Kachaso fuck malawi

  61. Enafe sitimamwa mowa komano nkhan iyi siyowona amabungwenu ngati zochita za sowa pezan zina not kuletsa chakumwa cha anzanu mdziko muno muli mavuto ambiri bwanji kulimbana ndi mavuto amenewo kuti athe musalimbane ndi mowa’.

  62. Kuletsa mowa ndiye amene amaphunzitsa ana ake ndi ndalama zogulitsa mowa ali pavuto. Ana saphunzila school. Vuto lalingono lipangitsa mavuto akulu. Tangolimbanani ndi ana amene mumawapeza kumowawo basi.

  63. Eyyy amabungwenu,,,tamangani malo osamalira ana amasiye
    Tayesani kupeza njira zothesera katangale/ziphuphu
    Tampezeni njira yoti okalamba ndiolumala akhale mwamtendere mdziko mwawo
    Tatenganipo gawo loteteza abale athu achi alubino!!

    Mowa wayambira kumtunda kukasilizara kapolo nde muyambira pati????

  64. It is a good idea to have regulated period of drinking beer because I have seen some drinking joints that open like groceries. It is surprising that people patronize such places as early as 7am and you wonder when such people make money for drinking and fending for their families. It is therefore important that such wasted time should be devoted to developing our national economy.

  65. Nonse osamwa khalani chete nkhaniyi sikukukhubzani.komanso sizingatheke kuletsa mowa mapeto ake Angonife mutishosha dala.

  66. aletse mowa siwabwino aletse chifukwa amalawi ndianthu osaganiza kale bwino pachibadwidwe chawo amakanika kuganiza zinthu zoti ziwathandize paokha ndiye akaonjezera mowa zimaonongekelatu amachita kukanika kulipira fees za ana awo ku xul kuona ana ambili anafika fom 4 xul,,,, koma akukanika kupanga cos chifukwa bambo pakhomo akuti zake ndalama ndizomwera mowa choncho ana anthu amenewa omwa mowa ndizimene zikumakhala mbava zikuluzikulu chifukwa sizikupitiliza maphuziro zikumangoyambaso nazoso kumwa ngati abambo awo …

    1. Uyankhula mbwelela bwanji munthu wa mowa umamu dziwa iwe munthu wamowa akamapita ku mowa amakhala kuti chili chose wapanga kale zaku nyumba kwake nde pali anthu omwetsedwa mowa ndi amene uku nena iweyo amakhala kuti kwawo sana pangekali kose amango bwela ataledzela panyumba nde aja amawa danda ula kuti akungo ledzela sikuti amakhala amwela zawo ai

    2. inu Malawi ndi dziko laumphawi kuti muonetsetse makomo ambili kukacha amamwa tea opanda mkaka bola ali ndi sugar kusonyeza umphawi akakhala bonya ndiye ndiwo zimene zasamala makomo ambili kumalawi ndiye pa lyf imeneyo muzimwelapo mowa kumati mukunjoya ?

    3. ndinu ana inu ndi mpake mukuchemelera mowa muzitifusa ife tinayamba kumwa mowa chibuku chili pamtengo wa K15 tinasiya uli pa k150 mowa ulibe chitukuko chilichose mowa umakupatsa courage zauchitsilu umatha kukupatsa mwano kumayambitsa ndewu chosecho ndewuyo sungawineso umakhala unagobola kale ..mowa umakupatsa chilako chogona ndi mkaz chosecho mphamvu zokwelera mkaz ulibiletu unagobola kale …muzaziona ndinu ana simunakhwime pa mchombo mwangoyamba kumene kuuva kukoma mowa

    4. kkkkkkk ine ndine m’Malawi koma ndimamwa mowa & zonse ndimakwanitsa ndimaposa osamwa mowawe.kungoti ambili kulakwisa kanenedwe am ngoni and ndiyenera kumamwa mowa ndikakhala free

    5. ndalama yako sungapange nayo mpikisano ndiine ndalama yanga iweyo singakupindulire olo nditakhala ndi ma million..chimodzmodz ndalama yako iweyo olo utagwila ntchito yokumba chimbudzi ndikukulipira ndiyako ine singakupindulire panjira iliyose

    6. Mowa athetse lero, ndi angati apezeke pa ulova ku makampani ofulula mowa? Ma Trading Centre opanda ma Bottle Store ayima? Ngati zomwera zinakutherani, khalani chete apa!

    7. panja mtundu wakatsonga umakhala wamakani,zakumtundu kwanu osamabweletsa kuno kupusa eti, unava kut olemera samafa? Maxson Mbendera,Bingu,kungotchulapo ochepa,Mabus amasiyewo munyadira kut muli ndi chumawo? Demmmeet

  67. Ndipo ndifebe okwiya kamba kamanong’onong’owa…Malawi hav so many problems as of now rather dan ds isue yoti somhw ikuthandza boma financially…gues how much chibuku breweries…calsberg..ie southern bottlers contributing to nation develop in sports..health & da like…how many pipo ar stil employed from ds companies coz of mowa brewering…somehow opanga fundo zoyendetsera dzikowa akumakambirana ataladzera beyond or iwowo akufuna atasiya nde aganiza zotero…komabe sitiwalorera kudza nd mfundo za ziii…tidakakondwa nao mowau…coz za bible izi

  68. Aku letsa mowayo mumu uze pantumbo pake akaletsa mowa tizi panga chani zaku n.nyelo zimenezo aletsemowa aku phuzila ku esa zida koma sizitheka muziti ama bungwe akufuna ma hule ose awa pezele mabanja nde abweletse ma hule atsopano munmalo azi sangalalo osati tingave zomwe nkhutu ku ve ina iku bwela ndi fundo zopoila akamati dziko anthu aku sangalala amanena chani mesa mowa wo popanda mowa ndepanga khale dzikoso zandi nyasa ndima phuzo ndaikawo ngati angathe kuona andi hale ku inbox mwana ophusayo

  69. Hehehe kma ndiye amabungwe mwasowa zochitatu.kma mumadziwa kuti enafe kt tigwire ntchto bwinobwino timayendera mowa or kt tigone turo tabwino ndi mowa omwewu ndiponso kt tilankhure zomveka pa guru ndi mowau?aaa stop that nosense..

    1. @Sam nde wati kut uyankhule zomveka umafunika kut umwe¿¿¿¿¿………nde apa ukuyankhula zaziiii tiziti sunamwe et? (just joking)

  70. khwimisani kapezedwe ndikagulitsidwe ka mowa basi koma zoti anthu asiye kumwa mowa sizingatheke…..

Comments are closed.