Oyenda usiku asamamangidwe; a Malawi akufuna malamulo a vakabu asinthidwe

Advertisement
Malawi police

Mzika za dziko lino zapitiliza kulira kuti malamulo amene amagwilitsidwa ntchito pomanga ndi kumenya anthu opezeka akuyenda usiku athe.

police malawi
A polisi akumanga anthu zedi.

Anthu akupempha kuti malamulo amenewa asinthidwe Kamba koti malamulowa amangopweteka anthu osauka. Mwa zina, malamulowa amapatsa mphamvu apolisi kuti anjate ndi kuimba mulandu anthu omwe apezeka akuyenda usiku.

Ophunzira wina wa ku Yunivesite amene sanafune kutchulidwa dzina koma wamangidwapo pachifukwa choyenda usiku anauza mtolankhani wathu kuti lamulo limene limatchuka kuti la vakabu limangopweteka amphawi kusiya olemera amene ali ndi kuthekela kopalamula milandu yoopsa usiku.

“Ine tsiku lina ndimachokela ku layibulale ndi amzanga. Kumene timagona ndi patali ndi sukulu. Ndiye tikupita kogona tinakumana ndi apolisi amene anayamba kutichita nkhanza ati chifukwa timayenda usiku. Pamapeto anatimanga ndi kutitsekela mu chitokosi,” anadandaula motero ophunzilayo.

Mkulu wa bungwe lomwe limaphunzitsa, kulangiza ndi kuthandiza anthu pa nkhani za ufulu wawo la CHREAA a Victor Mhango anauza atolankhani a MANA kuti nthawi yakwana kuti dziko lino lithetse malamulo omanga anthu opezeka akuyenda usiku.

Victor Mhango
Mhango; Malamula a vakabu aunikiredwenso.

“Bungwe lathu ndiye likulimbana ndi makhalidwe omanga anthu opezeka akuyenda usiku, posachedwapa tinakumana ndi atolankhani amene tinawaphunzitsa kalembedwe ka nkhani zokhudza vakabu. Tinawauza azifotokoza kuti ndi nkhanza kumanga anthu pa chifukwa choyenda usiku,” anatero a Mhango.

A Mhango ananenanso kuti bungwe lawo likukumana ndi apolisi ndi oweluza milandu kuwalimbikitsa kuti aleke kulanga anthu opezeka akuyenda usiku.

Mneneri wa ku mabwalo a milandu, a bamboo Mlenga Mvula ananena kuti milandu ya anthu omangidwa Kamba kopezeka akuyenda usiku ikuchulukila.

“Nthawi zambiri ife a mabwalo basi timangowapatsa chilango choti alipire chindapusa, sitingawatumize kundende chifukwa ndiye kungadzadze,” anatero a Mvula.

Advertisement

144 Comments

  1. Kugwira oyenda usiku sikolakwika koma pazikhala,malo ake,nthawi yake,
    Osati pabara akumwa
    akagwire zigawenga

  2. mukulira chan? Ine ndimachoka kuntchito usiku sanayambe andigwirapo, nanga inu mmakhala mukuchoka kuti? Isathe vakabu ndichitetezo chathu cha anthu olungama ife. Mukufuna muzitimenya ngati kale eti? Nkumatilanda zinthu

  3. Zoona zimenezo, malamulo asinthidwe chifukwa a polisi a Malawi alibe luso pantchito yawo. Amangofikira kumenya ndipo nthawi zina amamenya anthu osalakwa ndipo amadziwa mochedwa kuti amenya munthu wosalakwa. Mu Johannesburg mtawuni a polisi akapeza munthu akuyenda usiku choyamba amamusecha kuti awone ngati ali ndi zida ngati mpeni kapena mfuti, kenako amamfunsa kumene akupita, pomalizira pake amamfunsa identification document. Ngati zonse zilibwino amamutaya. Nanga zikuvuta bwanji Malawi dziko la mtendere?

  4. Mapazi awo azilonda komaso akapolo achabechabe lamulo lichoke ndilabwino koma ma enforcers sadziwa ntchito komaso yanthauzo lake salidziwa amangopanga zinthu muchimbulimbuli so the best way is to elliminate the law completely.thank u.

  5. Ine ndye ndilibe nawo mau pandalama zomwe anditengela n amachita kumandidikila malo amodzi omwe omwe koma chosecho akuziwa kuti ndimapanga biznes yoweluka mazulo

  6. Malamulowo pawokha ndi abwinobwino koma the way our police officers are utilizing them eish zovuta kumvesa, i remember ndinagwidwa vakabu 11pm galimoto yanga ili pambalipo, kundimenya , ndikundibera ndalama zanga zonse, mmodzi kukwera nane mgalimoto mwanga ulendo waku cell, spent a night mu cell. Have heard alot of similar stories. Enforcement ya lamuloli ndi yomwe ifuna kusinthidwa

  7. Ndinagwidwapo ineo ku Kanjedza Lodge yet ndinali ndi Id,Driving Licence,psssport,and nthawi imeneyo ndimachindana mchibwezi changa,atatigwira anapita nafe pa Limbe police station,usikuo ku station kwaoko wapolice wina anandichindaso mondiumilidza

  8. apolice akumalawi sanayendepo mayiko ena m’chifukwa chake akadali m’tulo.masana timafuna ndalama ya ndiwo usiku ya ufa.

  9. Instead of kumamka nayendera makomo kut azigwira mbava zavutazi koma kuyenda ma bar kumafuna ati ndalama zaulesi akamawatulusa anthuwo

  10. these laws do not reflect the reality on glound.. imagn uli pa night shift & or overtime & u want to go home early kenako ukumane ndi vakabu.. its high time we change thsese laws otherwise akupanga benefit ndi a police…

  11. Eti mpaka disturbing business men in rest houses. Akakupeza ukuyenda usiku pa msewu akumenye, akupeze ukugona ku rest house akumangenso. It once happened to me in 2011. I had all the legal documents but was nothing to them, POLICIA CORRUPTOS E ESTÚPIDOS!

  12. Ine ihate this law coz imakondera, munthu akakhala pa galimoto samamugwira kma woyenda pansi nde kumugwira, nde zichan zimenezo. Ndekut lamuloli nd la anthu osauka bas? Aganizepo bwino pamenepo.

  13. Zoona chifikwa a police a ena udindo wawo kapena ntchito yawo saitenga munthu ampeza sakuthawa koma amayamba kumumenya komanso munthu oti wagwidwa vakabu mumveee bail yokhayo ngati kuti anaba zisithe kapena malamulo achepe mphamvu

  14. Apolice avcb ndiwomwe akumaba kwambili ndipo apolice sakuyenela kwaletsa anthu kuyenda usiku ? Koma akawapenza awafunse chifukwa chomwe akuyendela usikuo

  15. Dat true zanyanya ena amakhala akuchokera kuntchito,kumaliro,mapephero ndi malo osiyana siyana kma apolice alibe nazo amangoti mukanenera konko akudziwa kuti mulandu wa vakabu munthu sukana chimakhala chili chani..?

  16. Anthu ena amagwila ntchito usiku nde kukumanga opanda reason yomveka bwino a polisi tiziwalodza. Aziyenda usiku for protection yes osati kukapanga ndalama zomwela mowa ndima hule.

  17. Lamuloli ndilabwino koma vuto apolice anapezerapo pothesera mavuto akunyumba kwawo.They missuse power ena amati vakabu akuba ndi iwowo FOR example am late ndikuyenda usiku coz ndikuchoka kuxovuta ukawafoktokozera chabwino kuwapempha kandisiyeni kwathu use ur car for u to blieve am not thief amakana moreova galimoto fuel akugwirisa ntchitozo Ndizatonxe our taxe

  18. Ulemu ndiofunika apolice ku rest house anthu amagona maliseche inu mumagogoda ngati munthu waba apolice ambiri ndiakuba, ndiomwenso amasokoneza kwambiri munt.hu osamufunsabwinobwino ai mwayambakummenya samalani ndichifukwa apolice ambiri timaphedwa chifukwa cha moyooipa pewani moyoochitila nkhaza dzanufe

  19. Kungoti sionse oyenda usiku ali akuba ena amakhala adeledwa , ena amaperekeza matenda kuchipatala mwina maliro amene koma azingofufuza bwino bwino mwina nkumaqapelekeza npaka kwao

  20. Timasongoneza zinthu, kuyenda usiku sikuti ndiwe wachiwembu kapenna okuba ayi, kungoti Amalawi kuyipa ntima kunachuluka

  21. Amatibela amenewa apolisiwa pafunika zitheletu Zimenezi apeze zochita zina amapezeka akumutenga munthu kumalo ogona alendo atagona akut tidziwane mapeto make unva tiye kwera galmoto ukanenela konko ndichilungamo kutelo

  22. zithe zavakabu mwinatingawoneko mwezi kugona six okolock zoon olomwezi waladan osawuna zoona
    ?

  23. Asalichoseyi umbava uzachuluka ,muzayamba kudandaula so kuti bomali they are not protecting the citizens yet mkufuna alichose, komaso what is latest time kuti everyone should be indoors? ????

  24. Kwa inu nonse amene mukufuna kuti vakabu ithe mukufuna kuti muziba? Kapene mukufuna chan? Zimenenzo zisachitike vakabu ipitilile kugwila ntchito yotamandikai umbamva uthe

  25. This law is just there to make this country poor how can the all people go to bed @ 6 in the evening and start working @ 8 in the morning and expect to be economically sound, Malawi wake up.police must work around the clock and in truth there are more criminal activities happening during the day than at night in this country.laziness laziness until when???wake up.

  26. ये सांस भी मेरी, मेरी ना रही,
    ऐ इश्क जबसे तू है हमारी…
    दोनों हम है तलाश मे चैन के,
    खो गया हैं जो साथ मेरे यार के These are my breath, I’m not,
    AI love you, since our …
    We are both in search of peace,
    Who lost my love

  27. Best news l heard in years, while other countries are trying to have 24hr cities to make alot of revenew for their economies ife kuno tikadalimbana ndi malamulo a chisamunda ngati vacab work up malawi, dzuka malawi dzuka, those police persons are suppose to protect drankers not aresting them.

  28. Ndiuchisiru kumene kumenya munthu woyenda usiku ndikumanga .bwanji bola likulephela uyu akumalimbikitsa nchitidwe wokupha Albino.Absolute no xance.

  29. Ayi zisathe chifukwa umbanda ndi kumba kukula and dziko lili lonse limatelo koma amalawi ufulu meautengela pamgong,o ufulu uli ndi malore ake mawa ndi inu iwe ukupangidwa chiwembu uzifzalira kuti Boma sili kuchitapo kathu dzikotu tikuliwononva tokha chifukwa ati ufulu

  30. Ine ndilibe nayo mau Police ndinagwidwa ndikuchokela ku ntchito koma makofi ndinalandilao ngati ndatukwana boma kenako amvekere zipulumuse wekha

  31. Koma oaanama a police akuonjeza nthawi zina akugwila anthu osalakwa ndikumawa menya zingachite bwino zitatha bas

  32. Umphawi umawapweteka apolicewa kwambiri thats why amapanga zosiyana ndizomwe lamuloli likunena, ngat lamulo likuti munthu akuyenela kumangidwa akapezeka pa public place akuoneka kuti alibe chochita, so apolicewa akumatimanga akatipeza ku resthouse so my question to them is,,,kod resthouse ndi public place??? Nanga ngat ili public place timalipila chifukwa chan??? Fuck_them_all, i stand on truth #osaopa…

  33. Kkkkkkk koma kwathu ku malawi,,,,, tsopano ndalama mkumachita thawi yanji? Ndiekuti kulibe tchito zina za overtime? Athu akuenera kuenda 24hrs apolice nawoso 24hrs akamudabwa muthu kumufusa wachilungamo sasowa. Koma zoti basi kungokumana ndi police kuthawa ndie Juberg depotee imeneyo.

  34. Umphawi umawapweteka apolicewa kwambiri thats why amapanga zosiyana ndizomwe lamuloli likunena, ngat lamulo likuti munthu akuyenela kumangidwa akapezeka pa public place akuoneka kuti alibe chochita, so apolicewa akumatimanga akatipeza ku resthouse so my question to them is,,,kod resthouse ndi public place??? Nanga ngat ili public place timalipila chifukwa chan??? Fuck_them_all, i stand on truth #osaopa…

  35. Umphawi umawapweteka apolicewa kwambiri thats why amapanga zosiyana ndizomwe lamuloli likunena, ngat lamulo likuti munthu akuyenela kumangidwa akapezeka pa public place akuoneka kuti alibe chochita, so apolicewa akumatimanga akatipeza ku resthouse so my question to them is,,,kod resthouse ndi public place??? Nanga ngat ili public place timalipila chifukwa chan??? Fuck_them_all, i stand on truth #osaopa…

  36. Umphawi umawapweteka apolicewa kwambiri thats why amapanga zosiyana ndizomwe lamuloli likunena, ngat lamulo likuti munthu akuyenela kumangidwa akapezeka pa public place akuoneka kuti alibe chochita, so apolicewa akumatimanga akatipeza ku resthouse so my question to them is,,,kod resthouse ndi public place??? Nanga ngat ili public place timalipila chifukwa chan??? Fuck_them_all, i stand on truth #osaopa…

    1. Kkkk Komaditu Kwinikweni ukavala ngati ukuchokera kuchigayo ndie shaaa zavuta kodi mmesa tili ndi ufulu wakavalidwenso?

  37. ine ndimakhaulitsa vakabu usiku ndimavula zovala kunyamula mujumbo ndimayenda maliseche ena akhala akuthawapo a vakabu kuyesa mfiti …

  38. Choyamba ndikuthokoza chifukwa cholemba nkhani mu CHICHEWA pali nkhani zina komanso zambili zomwe zimafunika kuti a Malawi azizimva bwino ngati m’mene amachitila mayiko azathu.
    KUMANGA ANTHU USIKU PAZIFUKWA ZODZIWA OKHA KUSATHE
    – Izitu zimachitika mayiko ambili munthu amene afuna asamangigwe ndibwino aziyenda ndi mapepala omuloleza kuyenda usiku
    – Izitu zikhoza kuchepetsa umbamva umene wachuluka dziko lathu la Nyasaland.

  39. Anthu amene akuti zithewo nde mbava zikulu zikulu ziku funa zikaba zizi enda mofewa kazi gwilani usiku imakhala nthawi yogona amapita kuti bola akanati adzimufufuza munthu bwino bwino asana mugwile ndipoveka nanga munthu uzienda usiku 3 koloko sugwila ntchito umatani kazizi umbudzani mbavazi usikuwu isathe dihlu yo mbuzi imadya pamene ai mangilila akugwilani muku choka kwakuba muku enela ku gawana kumene adziku siyani ndi ngini zoti mwaomba kwina nde sali ntown tu apolice wo tu

    1. sunakumane nawoko a bvakabu iwe,anthu amenewa amazuza,olo akupeze ndi makiyi agalimoto savomera kukusiya mpakana galimoto kugona pamene unayimikapo,udzaziwona ukadzakumana nawo.coz siwonse amene amayenda usiku ncholinga chokaba.

    2. Zoti anzanu akuphedwa usiku wu mumazi dziwa apolice saku siya ku mene iwe una ku manako ndiwa kuba panjila ndikungo ku secha osaku peza ndikanthu ndikuku uza kuti ulibe dohla kazi vaya mesa amaku siyila mnpeni kuti uzikumbukila kuenda ndi dohla usiku zotiso akuba ama panga hayala magalimoto omwewa simudziwa ama funa aku welenge chifukwa amakhala kuti adziwa kuti suli wekha amzako ajowa mnpanda wawina akukapanga atuck kumeneko

    3. Kkkkk eti man anthu aku bakila zoti zithe chifukwa sana kumaneko nda galu amichombo usiku ndinkani akungo yankhula kale ukamaenda usiku chomwe umaopa chinali fisi mankwala ake tima enda ndi tochi paja fisi amathawa akango ona kuwala kwa tochi pano nditokha tokha tiziopana nkhani yake kwagwa n.dima kkkk

  40. Nnachita kumva wapolisi akulankhulana ndi judge wina wake pa chichiri ku high court akuti, maluzi ndiye apweteka bwanji, winayo amvekere, osakangogwira vakabu usiku uno bwanji azidzanyema pang’ono pang’ono kuti tiwataye basi mawa siukhalanso mmaluzi. It’s a system and sad that dzikoli is just rotten from top to toe

    1. Yes zikumachitadi bro.koma ichi sichifukwa chokwanira kuti vakabu isiye kugwira ntchito yake.tangoganizani bro umbava ndi uchigandanga ukuchitika pamene vakabuyo ikugwira tchito yake what more ngati kulibe vakabu zingakhale zotani?

    2. Vakabu yili ndi ubwino wambiri kwabasi. Isaphatikizidwe ndi nkhani ya corruption,aMalawi wasangosanduka mnkhalidwe wanthu ndipo tili pa mmbalambanda dziko lonse la pansi.

    3. The law is good braz, but the intentions of police in handling the matter makes it look bad. Tiyeni zinthu zina tizidziongola mosalekelera zikamakhota. Those in authority take advantage of our ignorance and disunity

    4. Yes it was a certain her worship waku magistrate. The magistrate word did just run away from me. Take off the liar word, mmakonza basi mwinanso ndinu akonko mukuzidziwa bwino kuti tikudziwa izo mmachita

  41. lamulo linali labwino koma apolice, anapezelapo mwayi wobela ndalama za amphawi, bcoz 8koloko ayamba kale kugwila anthu ati vakabu, nde , komanso lamuloli kuti lithe kukhala umbava wazaoneni utsiku, nde tingoti lithe chifukwa apolice wa agugwila nthawi yabwino komanso sakumamvesa ukamawadandaulila kumene ukupita kapena komwe wachoka akungoti vakabu basi…

  42. Sionse omwe amaenda usiku amakhala ndi zolinga zenizeni,ambiri amakhala akuba, Ubwino wake mukamaberedwa ovutika ndinu nomwe.

  43. ndikugwilizana nazo zimenezo makamaka enafe timagwira ntchino ya u balaman,,amachita kunditchera ndikaweruka cha m’ma 2 kuti andikolopore timachange muzina la Vakabu,,Futsek vakabu!!!

  44. Lamuloli ndi labwino. Only that a police akulipanga abuse. Nawonso alowa kubera anthu using lamulo lomweli. Just like Paul Banda’s song. “Ambiri tikulephera kugwiritsa…… Ndipo zimaoneka ngati zoipa

  45. Vakabu Isathe Kma Akhale Nd Nthaw Yoyambira Yeniyeni Osati 6 O’clock, Ambiri Amakhala Aderedwa Ku Ntchito nd kuma Business Amamangidwa Osalakwa

  46. Malawi is indeed the world’s poorest country.
    Chimenechi nkukhala chifukwa chomangira munthu

  47. Koma ufulu pamenepadi ukuphwanyidwa. Bwanji osalimbana ndiumbava koma? Oyenda pagalimoto kaya akukaba osamumanga koma ochoka kumowa akupita kunyumba kwake kulimbana naye.

Comments are closed.