Musaope, gumulani nyumba zonse zomangidwa mu phiri – Khoti liuza a khonsolo ya Blantyre

Advertisement
Soche

Bwalo lalikulu la Milandu tsopano lamasula khonsolo ya mzinda wa Blantyre kuti ndi yololedwa kugwetsa nyumba zonse zomwe zamangidwa mu phiri.

Khonsolo ya mu mzinda wa Blantyre inauza anthu onse omanga nyumba mu phiri kuti asamuke. Koma anthu aja m’malo mosamuka anapita ku Khoti kukatenga chiletso.

Anthony Kasunda
Kasunda

Kwa zaka zisanu, a khonsolo akhala asakuchita kanthu ati kamba ka chiletsocho. Koma tsopano chiletso chija chachotsedwa.

Ndipo tsopano a khonsolo apeleka chenjezo kwa anthu amene akukhala mu mapiri a Soche, Ndirande kudzanso Mpingwe kuti asamuke ndi kugwetsa nyumba zawo.

“Ali ndi masiku 60 anthu amenewa, miyezi iwiri yeniyeni. Ikatha tikubwela tokha ndi galimoto zathu kuzasalaza,” anatelo mneneri wa Khonsolo a Anthony Kasunda.

A Kasunda ananenanso kuti a khonsolo apeleka malo kwa anthu 65 amene asamuke.

Iwo anati pamene nkhaniyi imayamba, anali ma banja 65 okha amene amakhala ku phiri.

“Tsopano alipo 300, koma enawo anabwela akudziwa kuti malowa ndi osaloledwa kukhala,” iwo anatelo.

 

 

Advertisement

69 Comments

  1. Kubwezelesa chitukuko mmbuyo bwanji munthu wamanga nyumba yake inu nde mugumuleso? Tamayendani a Malawi muziona mmayiko anzathu nyumba dzao kuti zili kuti pamwamba penipeni pa phili boma ndikwasatilaso komweko ndinseu opambana kwambili koma kumalawi iiiiiii mmmmh

  2. Malo ake omwewa a Chauta Namalengawa mukuti ndi a inu a boma?Ayi zikomo mukhale ndi moyo opanda malire inu ndi anzeru anuwo oweruza mosaopa Mulungunu.

  3. Anthu onse okhuzidwa apite akatenge chileso chogumula nyumba zawo ku court konko mpaka nyengo yamvula ithe kuti azathe kupeza malo kwina ndikumanga nyumba zawo.

  4. DPP mukubetsa ma voti apa izi mukanadikira zisankho zidutse kaye. Otherwise I don’t expect munthu woti mwamupanga chipongwe chimenecho will vote 4u.

  5. -Kod phiriro ali gumula pomanga nyumbazo? Koma akanakhala azungu nde kuchita kuwapasa kut mpakana mmmmmmm kuwa mmm”ndayiwala”

  6. A malawi tiyeni tizimvera malamulo akati apa osamanga kanthu tizimva taonani mwaononga ndalama kumanga nyumba zimene zitagwetsedwe chifukwa chosamvera malamulo makani opanda nawo phindu ena atengerapo phunziro. Amalawi umbuli uzatithere liti?

  7. Khothi lalakwa pena silinalakwe kumanga zinthu malo osaloledwa ndi mulandu khothi lalakwa pouza kuti agwetse iwowo mmene anthu amamanga amangoyang’anila chifukwa chani ngati agwetse anthu alandile chipukuta misozi

  8. Anawapatsa malo ndani? Ngati panalibe dongosolo lopezela malo asamuke basi. Komabe boma liwathandizeko ndi kokayambila kwina. Phiri ngati la Soche, zoonadi linali phiri lokongola koopsya mu zaka za mma 90s koma lero ngati bodza.

  9. Serious akuyeneradi kuwachosa mopanda kuwanyengelera, tiliso munyengo ya mvure nde tiyeni tizinganiza tokha zoteteza moyo komanso katundu wathu, mupite pa Phiri la Soche mukaone mmene anthu amangira timanyumba pamenepo yet just some 3 years back we lost a lot of people in soche east ndimazi amphavu omwe amaseseleka kuchoka mu phiri muja, ndipo fans yomwe imakhala mu phiri muja mmmm inafa yambiri and ena anavulara modesa nkhawa, lero nde mukubwerelamoso? Ngozi ikachitikaso then muzipanga blame boma kuti silinakuthandizeni? Zinazi mumaziyamba dala cholinga zikakugwerani muzilandira zinthu zaulele kuchoka ku boma, mipingo komanso kumabungwe, I think this time mukapanga makani then akakusiyani wina aliyese asazakuthandizeniso bcoz mumapanga dala!

  10. Apatseni anthu malo oti akakhala Palibe kanthu kuti e nawo anabwera dongosololo lilipo kale mukawachotsa moteromo Akakhala kuti anthuwo Ali ndi ana?

    1. Mukati samaziwa kt molesedwa kd malowo boma likupanga nawo chani chitukuko ayi kma kulimbana ndi dzika basi kuzisowesa mtendele

    2. Ankadziwa komano chinawapanga kuti apezeke mmalomo ndichani? ( amalawi tiyeni tiphunzire kukhululuka ndikulorena wina ndizake mulungu azatikhululukira bwanji ngati tikanika kukhululukirana tokhatokha

    3. Malamuro akuyenerah kutsatidwa kumene, komano Vuto ili ndalikulu munthu a muchotse opanda kukamusiya penapake akakhala kuti

    4. Akakhala Kuti Masikuano Ungapeze Malo Chisawawa Ngati Akukaniza Mantchile Amamakolo Anthu Omwe Bwelani Muzaone Mene Anthu Akuvutikilakusowa Pokhala Pamene Wina Wazala Bluegum 10 Klm

  11. Achotsen, Km Mwanena Kt Pachiyambi Analipo Anthu 65 And Pan Alipo 300- Ndiye #Fuso, Mkumat: Kd Akhosolowo Awapezera Malo Okwanira Anthu 65 Kapena 300- Monga Mmene Aliri Panopa, Pls Gv Answer,

  12. Athamngitseni basi anthu anji osasamala chilengedwe? Kodi mmene anamanga ku phiri amati anyani, apusi ndi nkhwere zikakhala kuti?

Comments are closed.