Nyerere, RVG akukupatsani theng’eneng’ene

Advertisement
Ronny Van Geneugden

Pamene masewera a chikho cha ma timu asanu ndi atatu mu chikho cha Airtel chomwe chifumbire kuyambira lowelukali, anthu ena otsata za masewera a mpira wa miyendo ati chikhochi chikhalangati ngati kukumba madzi pa thathwe kuchipambana kuti wina akachimwelere.

Ambiri akuti kubwera kwa m’phunzitsi wa timu yayikulu ya dziko lino Ronny Van Geneugden (RVG) kupereka mpishupishu kwambiri kwa ma timu omwe amachalira kuti mwina ayenda moyera potengera mbiri zawo.

Ronny Van Geneugden
Geneugden wayambapo kusaka osewera.

Malingama ndi yemwe adali technical director wa timu ya Nyasa Big Bullets Billy Tewesa, iye wanenetsa kuti za ulendo uno zikhala za mlingo wina chifukwa osewera aliyense afuna kuti awonedwe ndi RVG mcholinga chofuna kudzigulira malo mu timu yayikulu ya dziko.

M’mawu awo a Tewesa ati Airtel top 8 ipereka mwayi kwambiri kwa osewerawa chifukwa ukhala mpikisano wa ma timu owerengeka chabe kusiyana ndi chikho chachikulu mdziko muno cha TNM super league chomwe chimaitana ma timu 16.

“Anyamata alimbikira kwambiri nthawi imeneyi kuti m’phunzitsi ndi omuthandizira ake awawone kotero kamba ka zimenezi ukhala mpira wa dzaoneni munditsimikiza ndipo kutenga chikho chenechi sukhala mtunda wa masewera” adatero Tewesa poyankhula ndi wailesi ina mdziko muno.

Koma malingana ndi wamkulu wa timu ya Wanderers Steve Madeira, iwo atj ali ndi chitsimikizo chonse kuti chikho cha Airtel chomwe changokhazikitsidwa kumene chaka chino atenganso kumka nacho ku nsewu wa Lali Lubani monga mwa mbiri yawo. Pamene iye wanena kuti 15 million ndi ndalama zomwe iwo ali nazo nkhuli kwambiri.

Madeira wanenetsa kuti Manoma akomzeka kwambiri kuti ateteze mbiri yawo yotenga chikho chilichonse chomwe mchoyamba m’maso mwa a Malawi ku nkhani zododa chikopa.

Koma m’mawu ake sabata zapitazo RVG adati iye ngati m’phuzitsi adzisankha osewera malingana ndi umo m’mene akukankhira chikopa pa bwalo, osati mbiri ya munthu kuti wakhala akusewera kwa zaka zochuluka mu timu ya dzikoyi. Izi zatsimikizadi kuti masewera a chaka chino afumbiradi zomwe sizikhala zophwekwa kwa akatswiri omwe akhala akunyamula dzikho monga cha Standard Bank, Carlsberg, Presidential, FISD.

Chikho cha mu Airtel top 8 chiyamba ndi ma timu a Silver Strikers kuphana ndi Bullets pa Bingu national stadium, pamene MAFCO idzalandile asilikali amzawo a Moyale pa bwalo la Chitowe ku Nkhotakota.

Sizidathere pompa koma lamulungu lake Beforward Wanderers idzaphana ndi timu yomwe iwo amatapako mphamvu zawo nthawi zambiri ya Azam Tigers pa bwalo la Balaka ndipo akatswiri a chikho cha 2016 super league Kamuzu Barracks asulana msulizo ndi Blue eagles pa Civo.

Advertisement

82 Comments

  1. Nkhani yanuyi sikugwilizana ndi mutu wakeo. Apa nyerere zalakwa chani? Kodi ma player a national team amangosankha Ku nyerere kokha? Inutu mutiuza bwino chomwe mukutanthauza chifukwa zikusonyeza kuti wonderers mumadana nayo, kapena mumaiopa kwambili. Mtola nkhani sakhala ndi mbili. Zamkutu!! Utola nkhani umeneu munauphunzila kuti makamaka???

  2. Gayez Pa 14 Ndikukumbukila Tsku Lmene Ndnayamb Kulowa Pa Fb Ndnso Kucheza Ndi Mafrend ,ndye Mundthandnze Pachisangalaloch,,

  3. Haaaa kungokhala osalemba bwanji?? nanga timve ziti apapa kkkkk koma zinazi kufuna kutchuka kuti mumalembako nkhani? muphunzilenso kachikena kuti mawa muzalembe zolongosoka tsiku lina

  4. Ngati mwasowa zolemba, awuzeni omwe adaita abduct hon Kamlepo Kalua akuti atsanzikiretu kwa abale awo apafupi ndi kutali chifukwa ulendo wawo ngomangamanga. Abale awowo asadzatisokonse amvekere ‘bwanji simudatitsanzike ‘?

  5. Kodi RGV amasewera Tigers? Or editor yo kumati nkhani yopanga post imeneyi? Aka nde ka Newsletter kapa Namphungo community day secondary sch. Kkkkk

  6. Kk-kkk-kkkkiest, the post is not clear… Otherwise, the impression here is that many people are afraid of Manoma.

  7. Ine am Bullets 4n koma apapa ndisaname palibe chomwe ndamva koma, RGV, nde ndani and yamukhuza bwanji nkhaniyi muzilemba za nzeru timataya nthawi yathu kumawerenga zinthu Zopusa ngati iziii asaaa

  8. koma yaa!! ma admin a BB sasowa, kukanika kulemba zomveka chiyakhuro cha makolo anthu!! chomwechi. kapena ndi 1 points mwaza nayo ku mpoto ija idakazunguzabe m’mitu mwanu eetiii!!!.

    1. kKkkkKkkk 1 points?koma zinazi eish paja ati masapota a team yawo amakhala ozindira apadi mwaonetsa kuzindikira kwanu.

  9. muwerenge nkhani yose ku website yawo not za pa fb ponkha …thus why mukuona kuti zikusemphana …mukuumira airtime yomalizitsa kuwerenga kwinako thus why mukungotukwana kkkkkkkkkkkk

  10. NDE pamenepo theng’eneng’e lili pat? Kmaso osewera aliyese akufuna kuonedwa si a wanderers okha ! Kunena zoona akuluakulu 5 games k15 million aaaa ndani xangaifune?

  11. Maphunziro athu sakutithandiza ndithu. Mtolankhani wantundu wanji wolemba chichewa chophwasuka! Nanga izi n’chiyani? (chikhalangati ngati kukumba madzi pa thathwe kuchipambana kuti wina akachimwelere.)

Comments are closed.