Bakili, Tembo akhumudwa ndi imfa ya Chakwamba

Advertisement
Gwanda Chakuamba

Mtsogoleri wakale wa dziko lino a Bakili Muluzi wati ndiokhumudwa ndi imfa ya mkhala kale pa ndale a Gwanda Chakwamba.

A Chakwamba amwalira dzulo pa 24 Okutobala masana pachipatala cha Blantyre Adventist mu mzinda omwewo wa Blantyre atadwala kwakanthawi kochepa.

Sabata latha nyuzipepala ino inakupasilani nkhani kukudziwitsani zakudwala kwa malemuwa omwe amadwala nthenda ya mtima ndipo anagonekedwa pachipatalapo mpaka dzulo pomwe atisiya.

Gwanda Chakuamba
Gwanda Chakuamba: Adatisiya dzulo.

Poyankhulapo pa zaimfayi, mtsogoleri wakale wadziko lino a Muluzi omweso anagwirapo ntchito ndi a Chakwamba, ati ndiokhumudwa kwambiri ndiimfayi.

Muluzi wati adzawakumbukila malemuwa ngati munthu olimbikira komaso osabwelera mmbuyo akafuna kupanga zinthu ndiposo opanda mantha.

“Ndinauzidwa kuti Gwanda wamwalira. Ndimadziwa zoti anali kuchipatala ku Blantyre koma ndimaganiza kuti akhala bwino ndipo nditava za imfa yawo ndamva chisoni komaso ndakhumudwa kwambiri.

Chisoni chikubwera chifukwa ndinawadziwa a Chakwamba zambirimbiri zapitazo, enafe tili anyamata tikuyamba kumene ndale. Tinagwilira ntchito limodzi mu mchipani cha MCP komaso cha UDF ndipo ndikufuna ndipepese kwambiri kumtundu wa a Malawi kamba ka imfayi” wadandaula Muluzi.

Mogwirizana ndi a Muluzi, mtsogoleri wakale wa chipani cha MCP a John Tembo, nawoso ati imfa ya Chakwamba yawakhudza kwambiri.

A Tembo ati ngakhale ndi a Chakwamba nthawi zina samagwirizana, koma malemuwa anali olimbikira pa ndale ndiposo mumchipani komaso amadziwa chomwe amapanga ngati namandwa pa ndale.

A Gwanda Chakwamba amwalira ali Ndizaka 82 ndipo anabadwa pa 4 Epulo 1934 ndipo wasiya mkazi, ana atatu, zidzukulu zitatu komaso zidzukulu tudzi zinayi.

Advertisement

109 Comments

  1. Guyz Ziwani Ichi Mu2 Amafuni Akamwalira Bakili Sanayenera Kudandaula, Ndikupanda Zeru Kwawo Mumva Kt Athandiza Maliro Kusiya Mu2 Ali Kuchipatala.

  2. Dziko la malawi ngati lidasauka ndi chifukwa cha iwe bakili, udagulitsa ma company, udapha anthu ofunikira, udayambitsa kugulitsa ziwalo za anthu, ndiye lero ungave chisoni ndi ifa imodzi.

  3. Choti anthu inu muziwe musiyanise nthawi yaka mpeni ndiya imfa ndi zithu ziwiri zosiyana anthu nthawi yakampeni amayankhula zandale cholinga awine kumbali yawo koma akachoka pa msonkhano anthu aja amagwirizana palibe cholakwika Tempo & Bakili chifukwa si nthawi yandale inu ngati muli mbuli pa ndale ndichifukwa chake mukuyankhula kuti Bakili &Tembo asayankhulepo kathu ndiwe mbuli pandale ndale siwudani ayi mbuzi ya munthu iwe asiyeni anthu akhuze maliro

  4. Amalawi tiyeni tisiyanise ndale ndi imfa chodandaulisa ena akunyoza why munthu amamvera chisoni munthu nzake tiyeni tikhudzike ngati amalawi

  5. Bakile wati wachita bwanji ndi imfa ya Chakuamba? Koma anthufe mulungu azingotikhululukira. Chomwe timayankhula nthawi zina sitimachidziwa, zomvetsa chisoni kwambiri.

  6. Kodi mukamati Mtsongoleri wa kale wadziko lino mukukutathauzanji? Poti ena amene akuwelenga nkhaniyi ali kumaiko akunja. Ndiye adziti Dziko lake liti pofuna kuitsata nkhaniyi?

  7. Chakuwamba pa 17 septmber 1972 ndiamene anamenya makofi mafumu okwana 19 kwa achikula including amfumu achikumbu ndan sakuziwa bwino. Muse mumtendele madala zimachitika

  8. paumunthu ayenela kutelo takumbukilini pakati abingu ndi abakili zinali bwanji? koma kumwalira kwa abingu abakili anakhala nawo zimasiyana ndichidani cholimbilana ufumu wa pamudzi chimakhala chamutima koma zandale zimakhala zanthawi yomweyo akulimbanayo zikatha amayambaso kumwela limodzi inu kutsala tikulumana zopanda tchito

  9. we are proud of you guys, you did a lot to our country and we still appreciate your presence as retired soja we rilly appreciate and we will still consulting you in different ways, but now give us the room, I mean give the chance to us the youth and let us develop this country technologically, machinery and man power development we have capacity to build this country but our chances are limited and we are here now to break that boundary our slogan is POWER FOR THE YOUTH POWER FOR DEVELOPMEND

  10. Bakili muluzi ngakhale atakhetsa msozi kwa ine sindingakhulupirire madalawa amanyoza kwambiri munthawi chisankho nde chakuamba akome lero?????

  11. Bakili simunthu oyenela kunenapo kalikose kokhuza Chakuwamba osangomusiya ause mumtendere bwanji lero Bakili aziti ndakhumudwa ndiliti adakhalapo wabwino Chakuwamba kwa Bakili Mulungu akanachita maye Bakili ngati amava chimunthu choipa chinaononga mtendere wa dziko lathuli samafunika ngakhale kukaponda pakhomo la maliro Bakili

  12. Aliyense wakhumudwa sizonena za anthu otchuka okha apa mawa mulembe kut Lucius George wakhumudwa ndi imfa ya Gwanda Chakwamba

  13. Apa mpomwe amalawi tiyenera kudziwa kuti andalewa amatipusitsa amaoneka ngati amadana koma kuseri akuchezerana.Ndikudziwa simungadabwe mukaganiza mmene muluzi amkanyozera gwanda koma agwanda anapitanso kukapanga mgwilizano ndi muluzi,tembo ndi muluzi bwa kunyozana wamagazi mmanja pamapeto pake kuzapanga mgwilizano ndi muluzi.Munthalika ndi muluzi bwa?koma ife atimkenaofe bwanji nkhani yomweyi inatchuka ya peter yi ndi chakwera kunali kutukwanizana pano pokomemta koma ayeni akewo akuimbirana ma phone mkumacheza patsogolo muzava apanga mgwilizano opusa mumakhala inu akumudzi mumakangana nkhani zaiii zo lerotu ndi awa

  14. Ya ndikudabwananu a Bakili inu mwaziwa kuti a Gwanda!(ka ya mukuti a shati)alikuchipatala ku Blantyre inu osapita kukawaona anzanu andale ndiye mukuti mwakhumudwa ndichani pamenepo ?mukanakhumudwa alindimoyo ndikupita kukamuona mkulu wakalamba eti?koma uziti ndakonda potisiya agwanda ndiye zimveka ndimau anu oyamba aja

  15. Zonsezi!! Ndichifukwa Chakusamvela Kwa Kholo Wanthu Adamu Ndiye Uchimo Unalowa Dziko Ndiye Chifukwa Chake Timafa” Aloma . 5: 12. Komabe Ngakhale Zili Choncho Pali Chiyembekezo Choti Akufa Oose Ali M”munda Adzaukaso .Yohane 5: 28,29. Tilile Ndi Chiembekezo!!!!

  16. Thats way how lyf goes osanenedwa palibe pa dziko even our bst frnds talksmore about us bt still wen ths thng comez they can’t rmembr wat they did R.I.P BAA.

  17. muthu ukamwalir zonena kuchuluk. ati ndkumanena kuti R.I.P.koma mwaiwal kuti mumamunyoz adakal ndimoyo. ndkumapitiriz kuti adali ofunika pandale. bushiti

  18. Akapeza azake amkawapha aja___amkaziyesa shasha akuthira anthu chitedze kukhoma misomali mmitu ya anthu wosalakwa kuwaguza mafumu ena atawayika mziguduli kukhazikitsa malamulo onyasa wakhauka watsala iwe Tembo pamaliro ako anthu adzasangalala

    1. Iwe ndiye chitserekwete chenicheni zitayeni zandalezo.Koma ndalenso suzidziwa.Umadziwa kuti Hwanda chakwamba anali true soildier Msirikali wankulu.Amene uja samaopa amuyesaye kuti amuphe analephera.Anachita kunena kuti ndayesedwa kwambiri kuti andiphe.Koma nkhabe ndinafa ndekha namatenda afuna alandire ulemu waukulu ndi a Malawi Defence Force.Ungafanane naye ameneyo zimene wakambazo adziwe ndi mulungu osati iweyo ayi wamvaaaaaaaaa

    2. Bwanawe ndiye kuti iwee mwana apa palibe ndale koma Nana ndi mzake Tembo ndi anthu awiri ofunika akanalapa asanafe achotsa miyoyo yambiri kuzuza mkatiiiiiiiiiiii

  19. Paja munthu akamwalira amakhala wabwino.Bakili akuyamikira nawo?Tili nawotu ma audio clip a mmene amamunyozera Gwanda.Choncho poti ndi ndale!!

  20. Iwe Bakili bwanji sunakhumudwe ndi infa ya Matafale?iweso John Tembo bwanji sunakhumudwe ndi infa ya Gadama,ndi Aron Sangala?musamatiphimbe mmaso anthu oipa inu.nthawi nde yatha ofunika kulapa basi.

  21. Uthenga wa imfa ndimatenda ndiye chodabwitsa ndichiyani ngati munthu amadwala? Plus he was old already! Did U guys who shows to the public with your fake glieve soul done some thing better to help him while he was sick? Or its just apolitic issues?

Comments are closed.