Boma lipemphedwa kuti lizimanga onse onama pa FACEBOOK

Advertisement
Billy Banda

Inu nonse amene mukutchukitsa kuti mtsogoleri wa dziko lino akudwala ndipo akuganiza zotula pansi udindo, akuti muzimangidwa.

Anthu ena omenyela ufulu wa anthu wa chibadwidwe ndiwo apempha boma la Malawi kuti liyambe kuunika bwino nkhani zimene anthu amaika pa Facebook ngakhaleso mu ma WhatsApp.

Billy Banda
Billy Banda: Boma libweretse lamulo latsopano

“Anthu akuchulutsa bodza pa Facebook ndi pa WhatsApp, papezeke njira yowalangila anthu onse abodza,” anatero a Billy Banda amene m’mbuyomu anali patsogolo kumenyera ufulu wa anthu.

Iwo anagwilizana ndi a Undule Mwakasungula amene nawo anapempha kuti boma lithetse chibwana pa Facebook ndi pa WhatApp.

“Anthu akumangonena bodza basi, pakufunika malamulo okhwima oti azilanga anthu otelewa,” a Mwakasungula anatelo.

A Banda ananena kuti m’mene anthu amanenela za umoyo wa mtsogoleri wa dziko lino panthawi imene anali ku America kunali kongoyenela kuti ena alangidwepo basi.

Anthu anatchukitsa kuti a Mutharika akudwala pa nthawi imene anatchona mu dziko la America, ena anati atsogola ndithu. Pamene a Mutharika anabwela dzanja lawo lamanja liri looneka lopuwala ena anati a Mutharika angobwela ngati chiphimba mmaso ndipo usiku atengedwa kumka ku chipatala.

Advertisement

463 Comments

  1. kkkkkkkkkkkkkkkkkkkkk kumangana pa Facebook…. umbuli upose pamenepa kkkkkkkkkkkkk……. mukamamva kupusa kapena kusowa zochita nde kumeneku…… I wish mtakhala omangidwa oyamba ine ndithu

  2. koma boma lopepera ngati ili sindinalione ine.. Chovuta ndichakuti this government doesnt have that confidence kuti ayendese boma chomwe akungotaya nacho nthawi ndikulimbana ndi anthu instead of planning zaphindu.. Asa educated savages. With empty brains

  3. Muyambe kuzimanga inu, Kodi mukamati boma mumatanthauza chani? Mesa mumanena ife timavotafe? Kkkkkkyambani kuzimanga nokha

  4. .Are you good in bed ?Do you really need a rich sexy sugar mummy or sugar daddy that can change your life completely with money and influence, so get the opportunity to meet sugar mummies from all works of life,politician,bankers,oil ladies,executives,directors,gold ladies,cash money ladies,Global Network group friends,doctors, ladies, willing to pay as much and get the best exclusive VIP arrangement anywhere in Nigeria,LAGOS,ABUJA,CALABAR,DELTA,ANAMBRA,PORTHARCOURT,,RIVERS,KOGI,KADUNA,JOS,ABIA,KANO,BAUCHI, SOKOTO,BAYELSA,ONDO,OSUN,OGUN,BENIN,IBADAN,ONDO,BENIN, call admin on 09036713792 or 08117333727 for your connection,like page before calling.

  5. No one shall be arrested. Opposition party & NG0 s argue DPP not arrest anyone who post info on social media saying that pple hv right to access info.

  6. Ayambe kumanga okodza pa mtengo,,,odya mizimbe,nthochi dowe mkumangotaya zinyalara paliponse ,,kenaka amange ma minister 7 akuba aja …..pomaliza onama pa fb

  7. Aboma amati sakudwala koma iye wanena dzulo kuti nyamakazi yakhala ikuvuta kwambiri and zinafika povuta kwambiri aboma akuyenera kumangidwa chifukwa chotinamiza.

  8. Inu malawi 24 ndi yemwe akutumaniyo pa ujeni panu shupiti muuzane. Obwera kwa ine akhale olimba chiwindi. Magetsi, njala, umbava ndi zina zotero mukulephera kuthana nazo. Koma mwaponda gear pa fb. Fuck u all. Demet, tidakali kutokota, poyamba pitala anagwa kamba ka njala pa msonkhano, pano dzanja lake lalowa ma virus. Kod ife tiziti munthuyu za umoyo zilipo? Ndalama za amalawi ovutika zinabedwa zankhani nkhani palibe mfundo yeni yeni ikuoneka. Inutu inu ohooo. Musamatenge ngat mukamakhala mu ma office mwanu aliyense ndiopusa. Kumanga muyambire atolankhani coz ndamene amafalitsa nkhani za bwampini. Ndipekenso ina.

    Pitala anati ziii ku america, a malawi 24 anapeza umboni woti abwanawa anali ku holiday ya mothers day. Amakasangalala ndi amayi awo ku america. More news clink here >>>>> malawi24.com

  9. kodi akulipempha Boma kuti liyambe kumanga onse amanama pa fb ndindani? Inu a Malawi 24 mwazitenga kuti tufuna nafeso tikawafuse amene amaterowo, nde pamenepa inu a Malawi 24 Lies ndi kuyambanitsa mulipati pofalitsa za bodza ndikuayanitsa a Malawi kapena ofalitsa zoona ndi zoluzanitsa mtundu wa a Malawi?????? Be a tool of Peace u Malawi 24 not of destruction pls!!!!!

  10. Segulani ndende zambiri kuti mumange amalawi onse. Koma choti muziwe ndi choti tizavotanso 2019. Mpando umenewo timakuikanipo ndife amalawi,siwamuyyayaaaaaaaaaaaa.

  11. Aaaaa inu mesa ine ndikukhala kuno Ku Pretoria moyandikana ndi chipatala chachikulu. ndizoona wabwera kuno kodi muzabisa mpaka liti ? Aaaaa oky yambani kumanga ine bisani matendawo koma maliro nde tizamva

  12. zachamba zokhazokha inunso a Malawi24 chilunga mukuchdziwa kaya mukupepelanso nd chan kaya, poyamba ndnkakudailan koma ndaona chanzeru palibe!

  13. So the issue is to arrest pple who lies, n what about him Peter he lied to us that he’s gonna change things while we’re still getting poor and poorly and also worse? tell me!

  14. Kumangidw kkkk koma ndiy zafikapo kumalaw,muyambe mwamang kaye onse anaba ndalam zaboma aja kenaka amene azilengez zabozawa,kkk komans mutuluse kaye anthu onse omwe ali ndimilandu yocepa amphaw ali kundendeko coz ndikuth kuona kuti tonseeeeee timangidwa malo ndiamene atakhale ocepa

  15. He’s arleady old he doesn’t fear death.He should know that he is in injury time and therefore he should ask God to forgive him his sins of geting GVT by stealing.The living God is not happy with his leadership.we want 2019 to be tomorrow so that we can take him out together with chilima.

  16. UYU MUKUTI BILLY BANDA NDI MMODZI MWA AMALAWI OPUSAA WOMWE AMAFUNA KUWONEKERA PA ZINTHU ZA ZIIII!!! NGATI ALI WOMENYERA UFULU WA ANTHU BWANJI ZAMAGETSIZI!? sukudzgg566f

  17. kkkkkkk koma abale nde amalawi tonsetu kundende, boma liwonjezere ndendende zina coz apapa chifukwa chakuchuluka kwa anthu mapeto ake adzidzangoti takukhululukirani kuli kusowa kokatiyika kkkkkkkk

  18. Mitu yanu idadzadza mamina ndithu kusiya aja anapha ma aludino waja ndi awo anasololawo kulimbana ndi amphawi akapuntha buye aaaa ndiye mumanga anga angati poti ndiwa zaka 4 zomwe mwana akudziwa bwino kuti bwampini akudwala kkkkkkkk koma kwathu kuno umbuli siudzatha bwanji kupachikidwa ambuye ndi khanda lomwe lidadziwa ndiye kuli bwanji mbava nhgati imeneyi sangadziwe 4 seck un emputy tin think nothing & react

  19. zoti akupapereka moni ndidzanja lamadzere ndidzabidza? akudwala mvomerani tsikuti ndioyamba kudwala iyeyo.ngwazi ija amkati mkango yamuyaya inadwala ndikufa ndiye inu zinsinsi zake ziti apa.

  20. Dziko lopanda mtsogoleri ndi chomcho,alomwe ndi ndi ntchito zawo,amawona ngati kulamulira dziko mkophweka ngati kubela mavoti

  21. Mumakamba mau oti inu olopang’ono simungakwanise bwanji azikumangani kumene athu opanda chikondi inu mulungu azikukhululukirani ife wathu ndiyemweyo basi mufune musafune. Ky akukutumani akupwetekesani

  22. Eish #Malawi wanyung’unya mpaka wamiseche azimangidwa?Yambani kumanga a Malawi 24 ndi #Lazarus_Chakwera amenewa ndiye oipa oipisitsa safunira anzao zabwino.

  23. Mmalo moti muziti mupanga bwanji kut magesi aziyaka, mukunena izi…. demet… ngat amanama omuyankhulirawo awone mkwiyo basi… u think malawianz ndiogona eti?? Hahaha thesan njala kaye ndi kuzima kwamagetsi

  24. Mukulephela kumanga mbava zikudyerela thukuta la a mphawi ku DPP kooo ndiye mukamange wotiuza zochitika kwathuko? mwasowa chochita. Muyambe mwamumanga Mutharikayo posauza mtundu wa a Malawi komwe anali ndipo amataniko? kokudya misonkho ya amphawi ndiye mukubisa? kungomva kuti akakhala pa nkhate sapheka Khoswe? Ndiye mumanga angati? Boma la Malawi likufunika mzika yeniyeni ya Malawi osati Man wa ayi ndi okonda ku maiko a Zungu basi ndimangani

  25. Ndebwino amange kumenene ndipo boma mukafuna kafukufuku ndikuthandizani mundipeze,chabwinomukhale oyipa koma mubwezeletse chikhalidwe ndi Ulemu

  26. Ndiye mulanduwo uzitchedwa kuti chiyani bwanji osamanga akulu akulu a ku escom bwanji kuchokera thawi yonseyija tinatenga ufulu odzikamulira mpaka pano simunapenzebe njira zothetsera mavuto a magetsi mmalawi muno ndiye pano mukufuna mulimbane ndi social media bwanji tinavotera multi party kuti tiziyakhula za kukhosi lero mukufuna muyambe za chipani chimodzi sithani

  27. Munyanya ma comment ,khani simukuyiziwa mwinaso simunayive bwino inu ma comment mpaka 500MB khani yake kunyoza tsogoleri malo 500MB kupangila chaphindu lyk kuyitanila malonda,kulengeza za uthenga wabwino Wa Mulungu,kufusila tchito,even kuchezetsa ndi tapambali,muli busy kulowelera za ndale ngati kuti amakolo anu even agogo anu

  28. komanso aboma nganiyo sakuyitenga bwino chifukwa ngati anthu akunena kuti akudwala mwina sakudwala koma ngati sakudwala kungoyamika mulungu osati kumanga anthu alakwa chani?

  29. kwaine fb palibe bodza kukakhala udwala mzoona yekha wavomela kuti nyamakazi. nde wabodza ndani? ine nuona aneneli amtsogoleri nde abodza amabisa matenda amunthu wamkulu. nde omangidwa akhala ndani?

  30. Mwaine ndekha kaya inu mumadziwa kumanga anthu kamangeni koma ngati pali chomwe chanve anthu ayenela kukambapo kanthu ngati inu aboma simukukamba chilungamo ifeso tidutsa momwemo komaso kodi kuopako tidziopa inu chifukwa choti mutimanga timangeni ngati inu muli achilungamo pankhani komaso ngati kuli kuopa ine sindimaopa humanbeing I only fear Almighty Allah and Allah alone none of you’s ndiye ngati kuopyeza awopyezeni omwe mukuwaona olakwawo ndipo amangeni komaso ngati inuyo simmafotokoza reality ndiye munthilidweso zingwe ndinu osokoneza ponama mulungu sakuona mbali2 ayi chiweluzo chiyende same manyaka aboma anthu opanda pabwino*******

  31. koma muwakwanitsa anthu wonse amene akugwiritsa ntchito facebook kkk iwe ukunenazimenezi ngati akupatsa yogula bread wagwanayo pitalayo

  32. koma muwakwanitsa anthu wonse amene akugwiritsa ntchito facebook kkk iwe ukunenazimenezi ngati akupatsa yogula bread wagwanayo pitalayo watizuza mokwana

  33. koma muwakwanitsa anthu wonse amene akugwiritsa ntchito facebook kkk iwe ukunenazimenezi ngati akupatsa yogula bread wagwanayo pitalayo watizuza mokwana

  34. Amangidwe kaye president chifukwa chowanamiza anthu omwe anamuvotela, ngati ukudwala ungovomela kuti ukudwala sikuti tikuchosa pampando mwinanso anthu omwe ukuwanamizawo atha kukuthandiza mankhwala.

  35. Oyamba kumangidwa nde ndinuyo,coz mwayesesa kupeka #Mabodza koma mwaona kuti sizinatheke izo munkafuna.f***ck M24

  36. Never ! Never ! Never ! Ngati mwasowa chonena kungowutura pansi udondo chifukwa mulibe fundo zotukula dziko ( stupit officials)

  37. Nde zausiru zimenezi akuona ngati ife ana awo eeeti mutu wake amene wayambisa zimenezi ndipo andisamale nditha kumu……….. Mbuzi

  38. Anthu aziwopa kunena chilungamo kukuwopani inuyo? zausilu zopusa basi. tizinenabe sitisiya. iweyo amene ukuyambisawe kuti anthu azimangidwa pamnyopako.

  39. Boma si anthu kodi? Osayamba kumanga a cash gate bwanjiiii? Mwasowa chonena? This is not Zimbabwe kuti ukanena za Mugabe a kumanga chamba chimenecho

  40. Atimanga bwanj pot ma 4n timagula ndi ndalama zathu en palibe chifukwa cholesesa kuyankhula zmenezi ndipo pomangapo muziti tatan pot nkhanio wina aliyese akuiziwa zot president wa dziko lovutika la malawi akudwala ndye poyankhula muziganiza muzizitukwanisa zithu zazi ngat mufuna kumanga anthu aboza ndye kut hall malawi ikuyenera kumangidwa mmalo mothesa umphawi mkumalimbana mza fb mwanya ndithud bozalo lipitilila

  41. aaaaa zaziiii!!! akandipezera kut iwowo? dzina langa lapansonkho lisali limel kkkkk adzitan kumanga kwake?zachamba ife nde sitisiya kma kunena pomwe tikuyenera kunenapo iwo ngat sakumanena chilungamo kuliuza dziko amat ife titaa? alongosoke!!!

  42. Zaziiiiiiiii mwasowa chochita mumdzikomo? Ntchito zogwila zakusowani? Anthu amanamizilidwa aja kuti amwalila ndindani anadandaula kapena kumangidwa? Ngati mwasowa chochita dzikalimani

  43. Zaulamuliro wa asamunda basi,mwasowa ntchito chani,mukusiya mbava zomwe zacashgate,ndalama yomwe mukanagulira magenerater amagetsi amakono,malawi nkutukuka,ndiye kulimbana nzazii inutu inu mutilankhulitsa pobowoka!!!!!!!

  44. Kuli Zigulu Zamaufulu Zimenezo Nimbiri Yamake Dzana Zomaopsezana Patsani Timaudindo Timene Anyamata Muone Kukoma Kwake Dzikoli

  45. Kkkkkk Koma guys ..mmmm tazandmangen ine pano ndkadye zaulele pa prison kkk zachamba iz wadwala wadwala bas szobisaso apa kut munaona plzdnt akupeleka Mon nd reft hand mmmmmmm

  46. Amaufulu alipo oyamba kunamizilidwa kuti wamwalila pano padziko lapansi si peter yekhayo tiyenazo bola chipepeso musungeso bcs mabungwe adzakhala mbali ya olangidwayo

  47. Ine nde ndizinamadi osati sewelo tione ngati andandimange ,zitsiku zopanda mzeru m’malo mwakuti azimanga omwe anaba ndalama za cash get ndiyeno muti manga ife chifukwa chani? Eeeeeeee!!!! Ndizoonadi ineso ndinamva kuti wamwalira ndiye bwelani pompano muzandimange agalu inu, ngati ndanama

  48. anyani inu ,a Malawi24 ,mwayamba kuzemba ?? mesa ndinu nomwe mumatiuza zonsezo?? 1agalu, 2 afiti .Manyaz bwanji mukamakamba zaboza zanuzo??

  49. Oti samakweza dzanja lamanja tsono bodza lili pati? Abodza ndinu a boma mumanama kuti Mutharika akunjoya thanzi pamene munthu akudwala inu khalidwe lanu ndilotani? Muyambe kumanga amene amati he is enjoying robust healthy chifukwa a Manama.

  50. Bomalo ndilauchitsilu ndipo ndikuchalenja kuti ine sangandimange.ndipo mwauze amene ayambisa kulipemphwa bomayo pachakuti pakepo sindikumuopa sukamnyoko yakeyo

  51. kunamatu ndi mtima wamunthu bola usamanene zabodza za munthu wina , chifukwa mwini akadzafuna kunena chilungamo zidzakhala ngati kukuchititsani manyazi. zonamizirana kudwala ndikumufunira munthu moyo wautali. heeee ife tinanenedwa kalekale kuti tili ndi aids koma lero tilibwino, tikadwala kupita ku chipatala, amangopeza negative. tsoka kwa onena kuti tili ndi aids.

    1. hehehe munthu wa Mulungu abale, kungoti ndili ndi mwana, bambo ake anamwalira, ndiye mumadziwa munthu akamwalira amati wamwalira ndi aids, nkhani imeneyo nditaimva anthu amangokanirana kumangoti anayambitsa nkhani ndi wakuti, winanso akuti ndiwakuti, mafunso akamabwera timangoti tiyeni mukapeze zoona. mwa modzi yemwe nkhaniyo inamupeza ndi modzi amene ndinamuonetsa ma result. ndimafunitsitsa nditatenga pomwe analemba ma result koma amakaniza kuchipatala, South Africa ukadwala ndikupita kuchipatala yimasiya ma file, timangopita kunyumba ndi mankhwala basi,koma ndinafunitsitsa kuti nditenge ndidzaonetse onse amene amanena, poti ena mwa iwo ndinapanga mark.

  52. fb idzakalako mpaka muyaya iwowo angomanga maprison oti adzawasungile antuwo. mgaiwaso uzapezeke wambili woti tizadye

  53. Walipemphayo ndani popeza limanamakwambili ndi Bomalo osapemhpa kuti nawonso azimangidwa bwanji? simunanamizidwe nsapato inu amapemphayo ndi mbalame

  54. muyambe kumanga ine ndikupasani address yanga …. kasungu TDCC P B x yasenya airport .mwandipeza .President pitala anamwalila kale guys . koma mundibwelele bwino plz .musandibwelele ku mazele

  55. The word says, aliyense wabodza ndi mwana wa mdyerekezi coz satan is a father of lies kotero akanena bodza iye amaona ngati wanena chilungamo popeza mwaiye molibe chilungamo. Nde onse amakonda kufalitsa nkhani za bodza pa fb bambo wao ndi satana

  56. Kkkk yambani purezideti, kenaka onse amuboma , andale chifukwa sakwaniritsa malonjezano kenaka muzalowe mmafoni mu fb. Kkkkk pamutu panu mwapanga nzeru pamenepo eti.

  57. Kodi azindikira liti kuti anthu akunama pa fb, adatani kulankhula muja adali ku American? Ngati ndi zotero nanu a Malawi 24 mumangidwa chifukwa mumaika zanu pa fb.

  58. Nanga dzanja linafalo sikudwala kumeneku? bwanji mukusewela ndi mulungu.mulungu akuwonen mukuyambisa kubisa matendanu.sadwala ndan mesa ose anafawo anayamba ndi matenda.

  59. Zimene akunenazo ndizosaveka ai,ndipo cndikukhulupilira kt angazikwanitse,dziko la Malawi asalitenge ngat Zimbabwe kt anthu azilephera kuyankhura zakukhosi kwawo,bomalo likamatero ndiye kt likuwatumira tumira anthu kt asasiye kunena za President mapeto ake anthu sangasiye kukamba nkhan imeneyo

  60. Ok kutanthauza kt anaba mabillion aja zinatha basi osawamanga kma afuna amange anthu osalakwa amene akungozichezera pa fb yawo kodi nanga matsiku onsewa ku US ko amataniko awawuze anthu?

    1. zomangana zinatha ndi kamuzu .Tisazuzike ndi kadegree ka Peter komwe anakarenga ku america ifenso tilinayo koma sitidzikundikila .Analanda boma ndi Bakili ndi Chihana awa anabwera ataona zothaitha Anali kuti ?Zopuaa eti mukagwere uko .

  61. Ana anjoka inu kungo kula mutu koma maso awili okha tamakambilanani zanzelu prz atsogoleli mutapanga chonchi wina ata tenga part ya magetsi wina ndikutenga part ya madzi kuti zisama vute wina ndiku tenga part ya aziphuzitsi kuti azilipilidwa mosavuta kapena kwabela ndalama zawo ayi ndibwezi ana aku phuzila wina ndiku tenga part ya school fees kuti isamakwele mwapa n.gong.o wina ndiku tenga part ya mavuto omwe ali nmamidzi wina ndiku tenga part ya zaulimi mukhoza kupindula osati zopusa mukukambilana zo mamanga anthu aku malawi osamakamanga anthu akwanu ku zimbabwe bwanji zausilu eti nthawi zino ndinthawi yoma uza anthu kuti prz prz ntundu wanga malawi mvula yayandikile tiyeni tizipita kumunda kuti mvula yoyambilila yo tizave zoti chimanga chatuluka koma nkhani ndikuva apa za ma buzi zokha zokha yen.yo ndi chitsulo kodi ine ndi dwale nzanga ndikudziwa zoti ndiku dwala ndingaka musumile chifukwa choti aku mauza anthu ena zoti ndadwala ine ku mwalila anthu akhoza kudanda ula end anthu amafusa kuti wamwa lila chifukwa chani nanga bwanji simunati uze zoti munthuyu amadwala matenda sama chititsa manyazi mwauze a bro anuwo kuti kuno siku zimbabwe siti mabisa matenda atsogoleli achifolenawa prz kumawa uza musana wapatse mwayiwo kuti pepani inu ndalendo kuno timadana ndizopusa ngati nkhani mukubudula apazi zandinyasa nkhani zama buzi zi bwanji ndikakhale kundende ine chifukwa chama tenda awina hahahahaha kunali aphwanu ankadzi tcha chitsulo cha njani koma ifa ilibe kuti uyu ndi shakazulu nde ali ndi anyamata owayang.anila koma nyumba yomwe amagona munali ma camela koma pano or muta kayang.ana muma memory card anuwo simu ngaka iwone imfa nde dolo padziko lose ndemuka mati muziti manga kwa merica ko mu nchipatala ana kugonekani inumo muna libemo odwalaso ngati inu baba muthalika from zimbabwe

  62. Aaaaa akuluakulu mukuiwala kt nd democratic gvm? Ngat mukufuna zimenezo sinthan dziko libwerere ku 1 party system. Bwanj osamanga akuba osewa ndalama zipezeke

  63. Bwerani muzamange ine kuno ngati mungati opusa inu . Boma lakulephelani ndiye mwasoba chochita . Chifukwa chache timakuthani Ku Malawi Chifukwa chaumphawi . inuso ma pulezideti muzimangidwa Chifukwa mumanama kwambiri nthawi yakampeni malonjezo anu sitiyiwala ife agalu inu

  64. Chabwino ndaona pakhota mchira nyani achinyamatawa akukunyozani coz akusowa chochita muyambe mwachotsa nkhalambazo kubomako then muike achinyamatawa, nkhalambazo zikagone basi sadzakunyozanixo kkkkkk

  65. aaaaaaaaaa mutsaopyseze athu ngati ma phone akutenga awulele ku boma fakosheee ngati akunama bwanji iyo bingu akugwiritsa ntchito mkono umodzi kwa anthu wabwela ndi ebola ameneyo

  66. Zake izo amene uja aziona jadgement yamupeza. Mulengi wakwiya naye,tsono asatiopsyeze palibeso angamangidwe olo atabweretsa ma contaner 10000 aunyolo, fotsek m’mene zikubedwera ndalamamu kumati amange munthu ot akungogwiritsa ntchito ma units a K50 za usiluu…NDAKWIYA NANU.

  67. Enafe tiri ndi ma account awiri pa FB, inayo tinaikapo dxina komanso Galu wa #ALEXIS-SANCHES pa profile,, nde ngati tinganyoxe Mtsogoleri kudxera pa account imeneyi,, mukundiuxa kuti mudxapita ku England kukamanga Galu ameneyu?

  68. Akulephera kumanga omwe adaba ndalama za boma ngakhale akuwaziwa ndie amanga bwanji muthu oti sakumuziwa…akuwona ngati aliyense amaika zowona zokhuza iye mwini…

  69. Osakamanga a Escom akungothimitsa magetsiwa bwanji usikuxo andiotchera computer yanga yomwe adandipatsa azungu, azungu atandiphwanyira mphika wanga umene adandipatsa agogo anga atandidyera mbatata yanga yootcha adandipatsa a Phungwako? Zausiru

  70. onama pa fb azmangidwa, how about them who are always lying to citizens, tipange chathu nafe chilango? ok then wa ndale aliyese yemwe sazkwanisa malonjenzo ake will be executed… Sounds good right?

  71. A Malawi 24 ndinu anthu opusa kwambili ķodi mumusowa źolembà eti mumatega anthu ģati zitsilu ndinu nomwe kunkati muthaliķa wamwalila , aķuďwala mukukambaso ziña agalu inu a malàwi 24 musova

  72. Boma liyambe kuzimanga lokha, then litimange ifeno. Iyeyo asadwale ndi chisulo kapena ndi ndani? Muuzane kuti kunali munthu amaitanidwa kuti wamuyaya, kodi akadalipobe? Mulungu akamufuna leo kapena nkucha amutengatu or popanda kudwala zopusa bas, kagwireni zigandanga mudzimage.

    1. Yo such a brainless idiot.. First the msg here says spreading nkhani zabodza about the president or any other issue that risks national security will be punishable by law..and man you need to go back to school..yes kamuzu was called life president..but not immortal president you idiot..there is a difference..life president means someone who will legally stay in power till his death..not that he can’t die…you got that you dumb ass??next time think first before commenting

    2. Fortune, Musatiopseze Ayi.Zomwe Zimakambidwazo Ngati Ndizabodza Muyambe Makoza Ndende Zambiri Chifukwa Mumanga Dziko Lonse.

    3. Fortune usandinyase ma Thousands of pipo suffering just becoz of one Person Mr IBu,,ameneyu si Munthu ngati sasintha aziona za Brother wake,,,,,,Mlungu sangakondwere anthu azivutika ambiri Chifukwa cha one Man,,,,,,

    4. Fortune D Boy Simmons akukhala ngati amakhala zimbabwe kapena kuti ndi khungu saona. Mwina walozedwa ndi anzakewa. Mwina ndiodwala mutu.

  73. But you cant control gossips and in this case you cant catch anyone here …fact remains he’s our leader elected by people and evryone shud respect hm.

  74. Choyamba ndipereke moni kamayi anga kudedza uko!!!! Mayi tchito munagwira pondilera bwino mulungu akpasen moyo wautari,ndimakunyadiran Mayi……..mwana wanu ine pano…miss u mom

  75. Mwati nchani? I read the post 4rm Malawi 24 this morning that the president is sick. They heard rumours. First arrest Malawi 24 then the rest will follow.

  76. Aaaaaa zabho ine sangandigwire poti ndili kubt komkuno ku ndilande sangandipeze anamwaliradi kma azuka mwachisomo ok

  77. Kikik dont talk about left handed. Have u forgot he was in America all cars are left handed u drive on yo right lane and keep left. Kwaaah

  78. Akuyambe kaye iweyo admin coz ndi iwe amene umatiziwisa zonse,Chachiwili uliuze bomalo kti bisani matenda maliro tizamva.Matenda sichinthu chomabisa coz wina aliyese amadwala.Ndikatelo ndamaliza

  79. Bwanji osalipempha bomalo kuti limange anthu omwe asakaza chuma chathu (public funds)? Mwasowa choti mutchuke nacho. This is cheap point scoring…

  80. kkkkkk eeee muzimangadi mwina maboza athe athu anatailila fb sinyozera muthu koma yokambilana za chitukuko tsopano iwe mbuli kwako kulalata

  81. kkkkkkk zomwe ndikuseka zoti kodi amalawi24 ali pachani..mesa iwoso ali pa fb bwanji akazipeleke awamange….zipangizo zamakono ziti zili padziko lathu zoti munthu angamupeze komwe ali….nanuso olengeza mumangolengeza zamutu mwanu.ngati msogoleliyo amaona ngati sazadwala pamoyo wake onse aziwe kuti anabadwa kwakadzi wauchimo ndipo matenda azimusata monga mumene tonse tikupezekela ndimatenda….kaya ndi ifa naye ikumudikila monga mene tonse tizafele.asaope ifa koma aziopa kupanga tchimo lomwe limabwelesa ifa yoti osakhalaso ndimwayi okhululukidwa ndi Mulungu,monga kunama,kusowa chilungamo zonsezo zoopsa.

    1. #chiyesa ooo ndimanyazi agwiladi nane kuona chocho.#Lucky J zoonadi panado weniweni kusowekela muzipatala nde angapange scan pa satilite munthu??

  82. Childish mind” kodi pakati pa inu ndife wabodza ndani? & muzitimanga bwanji popeza izi ndizapa air? ok ndayambapo ine president Peter Muthalika akudwala ndipo dzanja lake lamanja silikugwira ntchito linafa ndione ngati mungandimange

  83. Basi nkhaniyake imeneyo nankha aja ananama kuti Mulungu anakwiya nkuuza Ngelo kuti angoyimbilatu Lipenga lomaliza ameneja nawo akuyenela kumamangidwa

  84. Nde muyambe mwamanga plezdntyo cz ndamene amatinamiza kt ali ku msokhano k USA chonsecho akumva nyunyunyu ku hospa.kenako omwe amamuyanganira onse cifukwa amatiuza ife amalawi zonama.

  85. Some of these things are easier said than done, it may be a good idea to regulate social media but prosecuting those suspected to have violated the law may be a mountainous task. I wish the govt could try to implement that, but authorities shd also be ready to be dragged to court for providing false information, its strange that official lies are just too many these days. The bottom line is that the govt triggers some speculations from the public sorely bcoz the former seem to be allergic to the truth,. Why shd pipo be hunting for information when there is an entire ministry responsible for that? The ans is just simple, untruthfulness!

  86. No wnder mulungu akulanga malawi mkusiya akuba ndala za boma mukamange wa facebook, nanga bwanji samapereka kono wamanja bwa popeleka moni kuwanthu it means alibe ulem iyeyo powapatsa moni wa kumadzere sinchoncho ?

  87. Face book ili ngati kuonera movie, 98% zimakhala zaboza munthu ozindikira amaziwa, mbuzi yosazindira ndi imene ikuyambisa zopusazo, nanga akanama munthu oti ali kunja, umbuzi basi

  88. Ok ayambe ine “NAZI NKHANI MWA CHIDULE”

    President Peter Mutharika akudwala mwa kaya kaya moti pano akumapereka moni ndi dzanja lake la manzere,Izi zikuchitika chifukwa Chakudwala komaso posachedwapa akhala akupereka udindo wa u President kwa wachiwiri wake a SAULOSI CHIRIMA….

    1. mmmm akuti akuyendela ma juction aphavu kwambili oposa maARV amapangisa muthu ukali phavu zikangotha amangogwa thi kuti azuke pamenepo eeeee ma drip a mazi 4

  89. moti president akudwala ndizabodza ? osamatipusitsa ife ndi ozindikila f.b ili bo inatiziwitwa kuti president akudwala mwa kayakaya

  90. tsano ozimanga individual or nomanyuzipepa omwe? nde muyambile kunjata o malawi punch,Malawi 24,Nyasa times, face of malawi ,zodiac online,maravi post kenako ifeyo mtinjate tonse poti phone mdatigulira ndinu

  91. Iwowo Anene Kut Azimanga Onse Onena Chilungamo Nanga Palinso Zobisa Apa Ndi Mwana Yemwe Kufunsa Kod Mon Ayamba Kupelekela Ku Manzere? Mwinanso Adangotibweletsela Chiloboat Chofanana Ndi Mr Ibu! Coz Chimaenda Mwachangu Komanso Chosayankhula

  92. Mangani ineyo ndikhale oyamba kumangidwa,koma musanandigwile muzandilole kuzagwila dzanja la apresident la kumanja tizawone ngati sazakuwa pa gulu.

  93. Mukuyambitsa Ndinu A Media Tsopano Ife Titani Poti Tikuma Comment Zomwe Mukutiuza Pa Post ,if So Ayambe Kumanga Inuyo , Koma Dziwani Kuti Matenda Amabisika Koma Maliro Muzatiuza !

  94. asaaa,zambiri zolembedwa pa fb ndi zabodza,ayamba kumanga poti ananena za president??…..iwo pomwe sankanenapo kanthu amaona ngat tziganiza zichani ifeyo??…..to be continued

Comments are closed.