Musamange mahule – Khoti liuza apolisi

Advertisement
prostitution malawi

Apolisi a vakabuali pa chi ntchito choopsa pamene alamulidwa ndi a khoti kuti asiyiletu mchitidwe omanjata azimayi oyendayenda usiku ati chifukwa kutelo ndikuwaphela amayiwo ufulu komanso ndikulakwila malamulo a dziko lino.

Malingana ndichigamulo chimene khoti lalikuluku Zomba lapeleka, a polisi alibe mphamvu yomanga amayi Kamba kot iawapeza mu malo omwela mowa kapena achisangalalo, ngakhale ogona alendo.

sex-workers-new
Amayi oyendayenda apeza ‘ufulu’

Oweluza milandu a mayi ZioneNtaba anagamula izi amayi ena oyendayenda atakamang’ala kubwalo la milandu kuti ananjatidwandi a Polisiati Kamba kopezeka kuti akuyendausiku.

Amayiwa atanjatidwa mu boma la Dedza, anapititsidwa kubwalo la milandu laling’ono kumene anapezeka olakwa.

Koma iwo posakhutitsidwa ndichigamulo cha bwalo laling’ono, anathamangila kubwalola likulu kumene a bwalo anagwilizananawo.

Malingana ndi akuluakulu a zamalamulo m’dzikomuno, mchitidwe wauhule si mlandu m’dzikomuno ndipo palibe ndime imene imanena kuti kugulitsa thupilako munthu ukuyenela kulangidwa.

Nthawi zambiri a Polisi amanjata anthu oyenda usiku ati pa mlandu opezeka oyenda opanda chifukwa pa nthawi yolakwika.

Nthawi zambiri apolisi akagwila amayi oyenda usiku amagona nawo mowakakamiza kuti awatulutse.

Advertisement

255 Comments

  1. Ine ndikukaika ngat mapresident,mp,malawyer,majudge ndi achuma ngat amakhulupilira kut kunja kuno kuli mulungu, kodi mpaka mungafike popereka ufulu wauhure zoona ? Mahuretu ndi anthu okuba, okupha, osakaza, apapa akhoti mwamusiya malawi pamoto basi, ndakwiya nanu

  2. komaso apolice ndinu zitsilu simuganiza mahule anthu akupanga zimenezo chifukwa inu nomwe apolice ndiye mahule akulu akumanga mabanja kubara komaso uhule sikuyenda usiku konkha ayi ambiri ndimahule or apolice akaz amapezeka mabala usiku

  3. pasapezeke wina aliyese pano onyoza mahule ndithana naye chifukwa mahule akuluakulu ndi makolo anu pazomwe anachita pobeleka inuyo ndiye awaso mukuti mahule amachita zomwe makolo anu amachita..eyetu

  4. akutchedwa hule chifukwa choti waenda usiku, nanga awa a day shift sima hule? akhothi mwakhoza musamawanjate akuthandiza anthuwa, milandu yogwilira ikuchepa chifukwa cha azimaiwa, mwakhwana kwambiri azibambo ena mabanja akuwaopa amadalira ma hule omwewa mukamawanjata adandaula,

  5. kodi yemwe ali pa ntchito, akupemphela, ali pa banja, ndikumachita uhule ku seli ndi yemwe akungochita uhule poyela wabwinoko ndani? opeleka chiopyezo chofalisa matenda ndani? bravo court uhule sumachitika poyela umboni amautenga kuti? kodi zoti munthu ali ndi ufulu wa chinsinsi amaziziwa? kodi ogwila mahulewo sachitepo uhule? ngati sanachitepo amawaziwa bwanji?

  6. Lamuloti linachokekera ku south Africa pamene kunali nsonkhano wa ukulu wa aids conference ku durban i cc kuti anthu o gulitsa asamamangidwe koma boma lathu la Malawi likufunika lidzifalitsa uthenga wa aids anthu tidzidziteza ku matenda amenewa mokwanira

  7. aaa mwachita bwino mahule amathandiza ndipo anthu ambili amapulu mukila mwama hule omwewa ambili sitimatha kufusila timango pita kwamahule omwewa chishango mmanja zatheka basi.

  8. kutelo ndikulakwa kwakukulu kumene kwachita boma lamalawi pogumula motele.kodi mukufunamiyoyo yawanthu ikhalemotani ,Nanga mukuonazibwana zanuzomanga mfundo ndikumasula.kodi ndigeni yanji Yopangandithupi Nanga mukuona kut zibwana pa malawi kuti sizingathe?munthu opitakusukulu angalamule kut ndibwinoazimayiwa azipangauhule. Kod a malawi muzakhwima bwanji nzeru kapena kuti liti.

  9. ngati sirimangidwa ifeso amuna asamatimangeka chifukwa hureyo kuti adye tchifukwa chaife kapena ife amuna tiribe ufuru?

  10. Dotoronomo 23:18 galu koma HULE ndizinthu ziwiri zonyansa kwambiri pamaso pa MULUNGU, ndipo musatenge ndalama yomwe yapezeka pogulitsa chimodzi muziwirizi kuti muthandizike nayo!!! Ngati ndalama yokha yomwe HULE wapatsidwa yaletsedwa kuchedwa kulibwanji HULE weniweniyo?? I will bring sharia law to the Malawi’s constitution mxxxm

  11. Azimayi anzanga,,, chonde tiyen tiyesese kukhala mahule kuchipinda,,, cholinga amunathu asatithawe kumalimbana nd nyasi zinazi! xoxoxoxoooo

  12. Yaa”” ndichoncho dziko lili kumapeto ol kt tione mibado yakaley kunalibe zimenez ndepot atumiki ndi aneneli ananena kale zizindikilo zakuza kwatsiku la chiweluzo ndizimene tikumazionazi* tiyeni tingosamala

  13. Mzanga wales,tisadabwe ano ndimapeto anthawi satana ngochenjerakwambiri amaongola pokhota kumaona ngat zirbwino pamene czilbwino tingopempha mulungu atmenyer nkhondo.Amen

  14. Kupusa kwa oweludza milandu ndikumeku,,,, tsono azibambo ufulu mulungu sadawapase?? Apa zikungowonekelatu kuti nonse opanga malamulo mumapembeza tsathana,,,, ndipemphero langa kuti mulungu akuweluzeni

  15. Sindinamvepo kuti apolisi amanga mkazi pa mulandu wochita uhule,koma Rogue and Vagabond ndi idle and disordery,yomwe ndi milandu associated with kuchita uhule usiku,komanso kugonana anthu akuwona.apolisi sagwira vakabu masana,that’s why mahule oyenda masana samawagwira.Tinene kuti court lathetsanso milandu ya rogue and vagabond ndi idle and disordery?Ngati athetsa zawachitira ubwino apolisi chifukwa ziwachepetsera ntchito.kkkk

  16. Munthu Sugula Mpando Ulibe Vokhalira Boma Silingavomeleze Makondomu Nkumaletsa Uhule Ndiye Makondomu Mupangawo Muzidyera Nsima Azitsogoleri Wosakhwima Nzeru Muleletsa Ndeu Anthu Avulazana Kale Mmalo Moleletsa Mkagano Achammatowo

  17. Nkhani yauhule imandiseketsa kwambiri chifukwa chiani amamangidwa ndiakazi okhaokha nthawi yavakabondi,pali mahule ena mmaofesi ana ambiri aliyense bambo ake ena,mabwana kuchita kumasinthana majunior kuchotsedwa mpaka matransfer,profeshonoro hulezi,akuchita zitukuko kwa nkhawa biiiiiiii,freedom of association anthuwa amanzunzika court lakwanitsa amasalidwa anthuwa apolisi inali ngati geni yawo

  18. Apatu palibe chovuta its like a market mahulewa akugulisa zili kwa iwo ofuna mahulewa ,l dont think munthu wopemphela angakhale ndi nthawi yomakafuna mahule,amenewa siwopemphela mowona,komanso mahulewo ayenela kupeza malo ali woyenela kupanga zimenezo osati penapalipose sikuwavomeleza koma mwakufuna kwawo,

  19. apolisi ingoti zilibwino mawa akapezeka munthu wogwiira osammanga chifukwa nayenso ali ndiufulu komanso mahule akaphedwa inu apolisi zisakukhuzeni kuti muzikasaka wapha ndani? inu yankho lanu muzingot walupanga kusonyeza kiuti geniyake yamupha

  20. pomwe akazi/ana anu atayazambe uhule ndipomwe mudzadziwe ubwino wa uhule.pomwe amuna anu atazayambe kugona ndi mahule, ndi pomwe muzadziwe kut hule ndi ndani

  21. kenako tizavaso kut wakuba asamagwidwe.ngat mukutelo ndiye khondo yolimbana ndi matendawa muyikwanisa.masiku osiliza cilicose ndi wufulu.

  22. ulamulilo otsutsana ndi mulungu ,izi ndizosaloledwa kuwapatsa mphamvu azimayi kuti azigulitsa thupi ,komatu mulungu sakondwela ndi anthu osokolesa anthu ngati amene akupeleka mphamvu yoteleyi, mulungu si munthu muzalangidwa nazo makamaka atsogoleli amene mukuwapatsa mphamvu anthu amenewa

  23. muletse a trafc osati mahule mahule amango ima sama imitsa munthu koma nyele zili ndamunanu mumawa imitsa tamuoneni ameneyo wango ziimila samalakwa ma hule osawa letsa mukawa letsa mahule tizikaku dyelani ku bwaila ama tithandiza tikamati dziko ndi anthu anthu ake timanena mahule wa

  24. Ma udindo ambiri komaso akulu akulu pa dziko pano timawalumbilitsa ndi bible koma ulamuliro umakhala wa satans, kodi dziko loopa Mulungu ndi kumalimbikitsa uhule mumanganiza bwa bola2 apa tisamanamizane kut dziko loopa mulungu koma dziko lopikisana ndi Mulungu

  25. Apolisi Nonse Taimani Tikuwowozeni Kaye. Mwaima 0oooooooooooo Tawoneni Maunifomu Awowa.Kukonda Kunyenga Mahule Lero Mwang’ola

  26. Zovuta Kuzivetsatu Izi Nanga Huleyo Akapezeka Ndimwamuna,Ndeye Kuti Azimangidwa Ndimwamunayo? Nanga Sikumuphela Ufulu Opezeka Ndikasitomala?ZA CHAMBA.

  27. Inde Khothiyo Yanena Zoona Azimayiwa Amaphwanyilidwa Ufulu Ndi Apolisi.Akawagwira Amayamba Kuwanyenga Molandizana Kenako Kuwatsekera Mchitokosi Kukacha Anyengenso Kenako Apitenawo Kukhothi

  28. Ndikana sangalala kwambiri kuti anthu amenewa azidula tax.ZOONA wamandasi azidula ticket musika azimayiwo ayi?komaso sachita ku order ayi.

  29. wopezeka kuti akutukwana mukuti amangidwe!! Pomwe mahule mukuti asamangidwe!! Tsiku lina tizamva kuti akuba asamangidwe!! DPP woyeee!!!

  30. Olakwa ndi anthu omwe akugula malondawo chifukwa akawalipira mawa adzayalatso poti zokudyadzi ndi zaulele Real man never buy sex, Don’t hate Satan or Jahoveh Kadzi wa dzeru ndi odzidalira sagulitsa thupi lake, Boma likuchita bwino kutsitha malamuro Ndende dzitsamadzaze ndima small case.

  31. amen!!! God ll punish u(amene mumati abomanu)coz mumalumbira bible/kolan lili manja.kodi mumaopa mulungu wake uti? God deniel saul with the spirit of what you are doing,read what God did in 1 samuel 16:1-11

  32. More rights to women’s , higher percentage of people to be positive of H, I V as a result higher percentage of orphans as well

  33. Chabwino tamva koma akanyengedwa ulele asamapite Ku police chifukwa malamulonso samalola kuti mahule azipeza ndalama pogulitsa matupi awo.

  34. A court alakwa kwambiri chifukwa mahule kuwaloreza kumayenda usiku azipangisa kuti HIV ifale kwambiri mmalawi….chifukwa Satan amazera kwambiri kwa azimayi komaso inuo a Court pomavwomeleza zithu zachabachabe koma inuo simpanga zimenezo

  35. Uhule ndi anthu awili, sono akapezeka HULE ndimwamuna pa msewu muzinjata mwamuna yekha?. ngati mkutelo, Kodi simunaphwanye ufulu wa mwamunayu ngati kasitomala? Chenjelani ndi SATANA yemwe panopa akusangalala ndi kuvomeledzedwa kwa tchimo lake kukhala lokhadzikika ngati lamulo.

  36. Apolisio amasowa chomanga eti shatapuzao,mahule aja ndiazicheri athu choncho xool,kudya kuvala rent ndizina zofunikira pamoyo zimachokera muuhure momwemo.pamenepo bwa kusiyana ndikuba

  37. Now game is on….to all those who stopped and became born again to go back to their roots as they abandoned this because of the fear. Game is on now to all husbands whose wives act as if their husbands only have eyes to see them only, Game on to all of upcoming sex workers who could not join the bandwagon for fear of police, Game is on now that the HIV and AIDs pandemic the country was boasting to have been successfully controlled to came back and lay it’s carpet in Malawi, the Game is on now that our favourite bar starts loading these women kachikena as police used to surround it each night. Game Iain now that prostitutes get rich and fight over their competitors. Game is on now that night economic power grows.

  38. Mmmm guyz ma comment ambiri akuonekeratu kuti mkati mwanu Yesu mulibe,tiyeni tipemphelere dziko lathu kuti santana asakhale ndi gawo mkati mwathu,Yesu atimenyere nkhondo mkati mwathu cauz mchitidwe wa uhule ukusonyezeratu kuti mkati mwathu mulibe Mulungu,tikadziwa Yesu zonyasa zonse zidzatha,akhoti akupeleka mphamvu chomcho bwanji?Cauz santana wamanga linga mkati mwao,tiye tiwenge Yohane 3;1 kumatsika m’musi mkhani yakubadwa mwatsopano.

  39. Mmmm guyz ma comment ambiri akuonekeratu kuti mkati mwanu Yesu mulibe,tiyeni tipemphelere dziko lathu kuti santana asakhale ndi gawo mkati mwathu,Yesu atimenyere nkhondo mkati mwathu cauz mchitidwe wa uhule ukusonyezeratu kuti mkati mwathu mulibe Mulungu,tikadziwa Yesu zonyasa zonse zidzatha,akhoti akupeleka mphamvu chomcho bwanji?Cauz santana wamanga linga mkati mwao,tiye tiwenge Yohane 3;1 kumatsika m’musi mkhani yakubadwa mwatsopano.

  40. Achita bwino kuwasiya nanga tikakafika kuulendowo kaya nku Mangochi……..tikadya chaaa?Enafe tinazowera kugona ndi bulangeti lamaso.

  41. Aaaah basi tingoyamba nawo basi mmene ntchito zikusoweramu malipiroso akuchepa pamene hule akumanga nyumba ya plan kuposa civil servant Kkkkk

  42. Mulungu potilenga sanatipase ufulu otere, ufulu winawu ukuchokela kwa Satan and panopa waonjezela mphavu pamene dziko lafika kumapeto,,,,,,, nkhani yayikulu,,,, democracy,,, uwu ndi ufulu omwe unachokela kwa satana, akuti munthu ali Ndi ufulu waku sankha “demos or Christ” democracy.. satana kuchenjera kwake he is dealing with people amene ali Ndi ma udindo akulu akulu,,, poziwa kuti akapanga lamulo enafe tingosatira nanga titani, nonse opanga malamulo komanso amene mukuti achita bwino kutero musamale, God is watching u,,, if u will miss Heaven, u will never miss Hell

    1. It was very easy for Jesus to tell his enemies kuti Nonse amene mwatengapo mbali pondipachika God is watching you or you will miss heaven but you will not miss hell .

      But instead he said “FATHER FORGIVE THEM ….” Sizoopsyezana izi.

      Inu amene mumaoneka umulungu kwambiri pamasonu ndi nu amene mukuononganso kwambiri .

      Ana akubadwa kuchokera ku ma overnight prayers ndi misonkhano ina yosadziwika .

      Ngati ma statement anu mwanena moopa Mulungu praise to God .

      Koma ngati mwangonena ndi pakamwa koma ntchito zanu ndi zachabe…Sibwino kuweluza…
      MULUNGU AKUKHULULUKILENI .

    2. Anthu amene muku wakambawo amakhala ziwanda zotumidwa ndi satan kuti akatero anyozetse dzina la Mulungu ndi kufookesa ambiri,,,,,mmene mwayankhulila apa man u need deliverance coz u don’t know the meaning of Jesus’s death.

    3. ulibe ulamulo uliwonse wopanga judge pple iwe musiyile mulungu.uli ndi nyasi zako zomwe umapanga mwanseli.sionse amene akuti ambuye ambuye akalowe ufumu wakumwamba.

    4. Deliverance angandipange ndani poti ambirinu ndi business.

      Mu nthawi ya Yesu anthu achisembwele analiko werengani bible.

      You you know Jesus’s death then what have you done?
      Wales Jmw Jeremiah
      Stop judging that you may Not be judged for with the judgment you are judging you will be judged.

    5. At Joseph,,,the reward of sin is dearth and righteous/born again will see the kingdom of God,,to be born again/righteous is to repent and receive Jesus to be our saveor and avoid sinful life,,,and the life after death there is only two place Hell and Paradise,,and is impossible to miss both places,,,if we repent no perish at all,,,shalom

  43. Anthuni maufuluwa atichosesa pamapa Mlungu, kodi Mlungu wathu tamsiya kuti chisoni chikundigwira ndi mmene ziko liliri, tayamba kuleme keza chiwanda chifukwa uhule si munthu koma chiwanda koma abale , Mlungu yekha ndi amene akuziwa zose

  44. Mumene… zinthu… zafikamu… ife… kulibe… kwina… kothawila… koma… kwayinu… Yesu… tipulumuseni… Satana… atchela… misampha… yambirimbiri… kuti… ife… tikalangidwe… nayo… limodzi… Poti.. chilango.. chamukulila

    1. Kungoti… mulungu… amatikonda… ndichifukwa… chake… atipasa… nthawi… yomaliza… kuti… tilipe… Koma… zovesa… chisoni… anthufe… adziko… lapasi… tikungochimwilabe.

  45. mmmmmm koma abale mpaka wina kumati am mtumbuka n i don’t know d meaning of prostitute chikhalilecho wakulira momuno tixit kumpoto it’s another country

  46. Kodi ma khothiso amatsutsana okhaokha? A khothi laling’ono akuti anapeza kuti anthuwa ndi olakwa, pomwe khothi lalikulu lapeza anthuwa kuti ndi osalakwa koma onsewatu ndi makhothi. Ndiye tikalakwa bola kuloweratu ku khothi lalikulu

    1. Mahule amagulitsa thupi lawo ndiye palibe chifukwa chowamangira pamene mbava zimatenga zinthu zoti sizawo iyayi akanakhala kuti akubawo amazibela wokha sibwezi akumangidwa chifukwa akutenga zawo

    2. This judgement is invalid and let me repeat it is invalid. Police officers are law enforcers and they cannot stop arresting people on charges of rogue and vagabonds unless this penal code law is revised and amended by Malawi Law Commission.Don’t forget prostitution is illegally in Malawi as stipulated in the penal code.

  47. Zoonadi apanga bwino azimayiwa amatithandizapo ife anyamatafe mtown mu

  48. ufulu wamahule.Izi zilichomwechi kambakakuti azimayi ndi ambiri pamene amuna ndiwochepa.mwachitsanzo mahulewa alibe mabanja ndipamene abambo amachoka kwa mkaziwawo ndikupita kwa hule kodi pamenepa wolakwa ndindani?akasiya kugula malondawo nayenso wogulitsa adzaleka.Nthawi yakwana mawulosi onse am’buku loyera akwaniritsidwe .

  49. A khothi aganiza mofatsa.
    Mahulewa akuthandiza kwambiri.

    Koditu akunyozedwa chifukwa nkhani ili pa media koma uhule ulipo wa mitundu.

    Azimai ena sapita kukaima mumsewu koma akugona ndi mamuna wamwini…ndi uhule basi.

    Ngati uli pa banja komanso uli ndi chibwenzi..ndi uhule basi.

    Ngati siunakwatiwe koma ukugonedwa…..ndi uhule basi.

    Ndiye tisawanyoze chifukwa choti abwera poyera.

  50. Mogwirizana tonse tiyime ndipo tiwombe manja mwakhoti kmanso judge ameneyu,waonetsa kulimba mtima kt lamulo amalitsata.
    Ichi ndichilungamo chokhacho chachitika kwanthawiyo mumbiri ya Democracy Malawi muno.
    Wodyazake alibiretu mulandu olo mpang’onopomwe,tiyeni takakumane pamseupo.

  51. Dziko lolephera ili nanga akatipatsa matenda sikulakwilanso ufulu wa ife?? Mukatere muzifalitsa uthenga wa Hiv edzi kuti chonde zisamareni kunjaku kwaopsa pamene muli bussy encouraging mahulewa kuti azifalitsa matenda eishh ambuye bwerani muzalitenge dzikoli pitala lamukanika..

    1. Kkkkkk R U Sure Moti Osewa Amawonesa Tchafu Mumisewu Ndimahule Lyf Iz Changing Bro What Matters Iz To Know Whow U R And What U Want Ngati Wapita Kaya Kumowa Ziwa Chomwe Wapitira Mahulewo Sakakamiza Munthu Or Kukamutenga Kunyumba Ayi Kungoupeza Basi Coz Dziko Likusitha Man

  52. Yayaya iiii amanyanya nawo apolice kulephera kugwira mbava zoopsa ndimamanga ma hule zautsilu mahule achizibambo ndikumawasiya kp it up

  53. Fosek zao apolice mukawachosamo muwapasa zochita? Mahule nonse ndawala panseu timache…ndakwiya nazo,,tiyeni muzikagwira mbava uko osalimbana ndi kudya kwathu ife apaulendofe.

    1. Prostitution is illegally in Malawi as stipulated in the penal code. Rogue and vagabonds law is still valid in our penal code. Police officers as law enforcers can’t stop arresting people including mahule who are suspected to have committed this offence unless this controversial law is amended to suit what is also stipulated in the constitution.

  54. Zowonadi amapangira kuvutika amafuna apeze ya chakudya ndi ya fees ya mfana ndi ya rent mene vepi zikusoweramo mumafuna a zingokhala

  55. Yah let them carry on bcoz amuna omwe amatenga ma hule ndima hulenso so why arresting the woman only every human being should behave at owners risk

  56. Azimayi ena amapangira kuvutika mzimayi oti sali pa banja sagwira ntchito koma akufuna kuti adye, ngati amatha nzeru munthu wa bambo amatchuka ndi mzeluyo kuli bwanji munthu wa mayi

Comments are closed.